Oweruza 5 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 5:1-31

Nyimbo ya Debora

1“Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:

2“Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli;

ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu,

tamandani Yehova:

3“Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu!

Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova,

Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.

4“Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri,

pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu,

dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka

nigwetsa madzi.

5Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova,

Mulungu wa Israeli.

6“Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati,

pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa;

alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.

7Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi

mpaka pamene iwe Debora unafika;

unafika ngati mayi ku Israeli.

8Pamene anasankha milungu ina,

nkhondo inabwera ku zipata za mzinda,

ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke

pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.

9Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli,

uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu.

Tamandani Yehova!

10“Inu okwera pa abulu oyera,

okhala pa zishalo,

ndi inu oyenda pa msewu,

yankhulani. 11Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta;

kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana;

akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli.

“Choncho anthu a Yehova

anasonkhana ku zipata za mzinda.

12Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera;

tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo.

Iwe Baraki! nyamuka

Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’

13“Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo;

anthu a Yehova anapita

kukamenyera Yehova nkhondo

kulimbana ndi adani amphamvu.

14Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu;

akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako.

Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri,

ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.

15Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora;

inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki,

ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira.

Koma pakati pa mafuko a Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.

16Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera

zitoliro zoyitanira nkhosa?

Pakati pa anthu a fuko la Rubeni

panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.

17Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani.

Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi?

Aseri anali pa gombe la Nyanja;

anangokhala mʼmadooko mwawo.

18Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa.

Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.

19“Mafumu anabwera, anachita nkhondo;

mafumu Akanaani anachita nkhondo

ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido,

koma sanatengeko zofunkha zasiliva.

20Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo,

zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.

21Mtsinje wa Kisoni unawakokolola,

chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola.

Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!

22Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu,

akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.

23Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’

‘Tembererani nzika zake mwaukali,

chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova,

kulimbana ndi adani ake amphamvu.’

24“Akhale wodala kupambana akazi onse,

Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni;

inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.

25Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka;

anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.

26Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake,

anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja.

Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake,

ndi kumubowola mu litsipa mwake.

27Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa,

anagwa; iye anagona pamenepo.

Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa;

pamene anagwera, pamenepo anaferapo.

28“Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera;

nafuwula mokweza kuti,

‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika?

Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’

29Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha,

ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,

30‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane;

akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri.

Sisera akumupatsa zofunkha:

zovala zonyikidwa mu utoto,

zoti ndizivala mʼkhosi

zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’

31“Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke,

koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa

pamene lituluka ndi mphamvu zake.”

Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.

La Bible du Semeur

Juges 5:1-31

Le cantique de Débora

1En ce même jour, Débora chanta ce cantique avec Baraq, fils d’Abinoam :

2Bénissez l’Eternel :

Voici qu’en Israël ╵on a laissé flotter ╵les chevelures5.2 Geste qui montre la détermination à aller au combat.,

le peuple s’est offert ╵pour le combat.

3Ecoutez-moi, ô rois ! ╵Prêtez l’oreille, ô princes !

Je veux chanter pour l’Eternel,

je veux jouer de la musique ╵en l’honneur du Dieu d’Israël.

4O Eternel, ╵lorsque tu sortis de Séir,

lorsque tu t’avanças ╵depuis les champs d’Edom,

la terre se mit à trembler ╵et le ciel se fondit en eau :

les nuées déversèrent ╵une pluie abondante.

5Devant toi, Eternel, ╵les montagnes ont vacillé5.5 Autre traduction : se sont affaissées., ╵devant le Dieu du Sinaï,

oui, devant l’Eternel, ╵Dieu d’Israël5.5 Voir Ps 68.8-9..

6Au temps de Shamgar, fils d’Anath,

et au temps de Yaël, ╵les routes étaient désertes,

les voyageurs suivaient ╵des sentiers détournés.

7Les villes d’Israël ╵étaient abandonnées,

la vie avait cessé.

Alors, moi, Débora, ╵je suis intervenue,

je suis intervenue ╵comme une mère ╵pour Israël.

8Le peuple d’Israël ╵s’est choisi d’autres dieux,

et aussitôt, la guerre ╵venait jusqu’à ses portes.

Ils sont quarante mille ╵soldats en Israël,

mais pas un bouclier, ╵pas une seule lance !

9Mon cœur bat pour les chefs ╵en Israël,

ceux qui se sont offerts ╵au sein du peuple ╵pour le combat.

Bénissez l’Eternel !

10Vous tous qui chevauchez ╵sur des ânesses blanches,

vous qui êtes assis ╵sur des tapis,

et vous qui parcourez ╵les chemins : pensez-y !

11Ecoutez comme ils chantent, ╵ceux qui font le partage ╵de l’eau près des fontaines :

ils chantent comment l’Eternel ╵a fait justice,

oui, comment il a fait justice ╵par son gouvernement5.11 Sens incertain. ╵sur Israël,

son peuple est descendu ╵aux portes de la ville.

12Debout ! Eveille-toi, ╵Débora, interviens !

Debout, éveille-toi, ╵entonne un chant de guerre !

Toi, Baraq, lève-toi, ╵ramène tes captifs, ╵ô fils d’Abinoam !

13Voici qu’un faible reste ╵a triomphé des grands,

oui, le peuple de l’Eternel ╵a maîtrisé pour moi les braves5.13 Autre traduction : est venu auprès de moi parmi les braves. !

14Ceux qui ont vaincu Amalec ╵sont sortis d’Ephraïm.

Benjamin t’a suivi, ╵il est parmi tes troupes.

De Makir sont venus ╵ceux qui ont commandé,

et de Zabulon ceux qui tiennent ╵le bâton de commandement.

15Les princes d’Issacar ╵ont rejoint Débora,

et toute sa tribu, ╵sur les pas de Baraq,

s’est précipitée dans la plaine.

Dans les rangs de Ruben, ╵on a délibéré

et discuté sans fin.

16Pourquoi es-tu resté ╵au milieu des enclos,

écoutant bêler les troupeaux ?

Dans les rangs de Ruben, ╵on a délibéré

et discuté sans fin !

17Galaad est resté ╵au-delà du Jourdain,

et Dan n’a pas bougé ╵d’auprès de ses vaisseaux5.17 Le port de Jaffa lui appartenait..

Aser est demeuré ╵près du bord de la mer

et il s’est cantonné ╵auprès des ports paisibles.

18Zabulon est un peuple ╵qui a bravé la mort,

et Nephtali aussi,

sur les hauteurs, dans la campagne.

19Des rois ennemis vinrent ╵et ils nous combattirent ;

oui, ils nous combattirent, ╵les rois de Canaan,

à Taanak, tout près ╵des eaux de Meguiddo ;

mais ils n’ont emporté ╵ni argent ni butin.

20Dans le ciel, même les étoiles ╵ont pris part au combat ;

du haut de leurs orbites, ╵elles combattaient Sisera.

21Le torrent de Qishôn ╵les a tous balayés,

le torrent de Qishôn, ╵celui des temps anciens.

Marchons avec hardiesse !

22Comme ils ont résonné, ╵les sabots des chevaux ╵qui martelaient le sol !

Au galop ! au galop ! ╵Fuyez, puissants coursiers !

23L’ange de l’Eternel ╵dit : Maudissez Méroz5.23 Une ville de Nephtali qui n’a pas participé au combat. ;

maudissez, maudissez ╵ses habitants :

ils ne sont pas venus ╵prêter main-forte à l’Eternel,

prêter main-forte à l’Eternel ╵au milieu de ses braves.

24Que Yaël soit bénie ╵entre toutes les femmes,

Yaël la femme ╵de Héber le Qénien !

Oui, qu’elle soit bénie ╵entre toutes les femmes ╵qui vivent sous la tente.

25Sisera demanda de l’eau, ╵elle a donné du lait.

Dans la coupe d’honneur5.25 La coupe est celle dans laquelle on offre le vin d’honneur lors des fêtes., ╵elle a offert du lait caillé.

26Et puis elle a saisi ╵un piquet dans sa main

et a pris de sa droite ╵le marteau d’ouvrier

pour frapper Sisera, ╵pour lui percer la tête.

Elle lui a brisé ╵et transpercé la tempe.

27A ses pieds, il s’affaisse,

il s’écroule, il succombe.

A ses pieds, il s’affaisse, ╵oui, il s’écroule.

Et à l’endroit ╵où il s’est écroulé ╵il gît inanimé !

28Par la fenêtre, ╵sa mère guette au loin ;

à travers le grillage,

elle exhale sa plainte :

pourquoi, pourquoi son char ╵tarde-t-il à paraître ?

Pourquoi n’entend-on pas ╵le fracas de ses chars ?

29Sans cesse, elle répète

ce qu’ont dit les plus sages ╵des dames de sa suite :

30« Sans doute ont-ils trouvé ╵un butin abondant ╵et ils se le partagent :

une fille ou deux filles ╵pour chaque combattant !

Sisera, lui, reçoit ╵des habits de couleur,

des habits de couleur,

deux vêtements brodés ╵d’étoffe de couleur

pour le cou du vainqueur ! »

31O Eternel, ╵que tous tes ennemis ╵périssent de la sorte !

Et que tous ceux qui t’aiment ╵soient comme le soleil

quand, tout éclatant, il se lève !

Après cela, le pays fut en paix pendant quarante ans.