Oweruza 18 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 18:1-31

Fuko la Dani Likhala ku Laisi

1Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli.

Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli. 2Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.”

Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona. 3Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”

4Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”

5Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”

6Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”

7Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.

8Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”

9“Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda. 10Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”

11Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo. 12Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero. 13Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.

14Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.” 15Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili. 16Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo. 17Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.

18Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”

19Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?” 20Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo. 21Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.

22Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza. 23Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”

24Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”

25Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.” 26Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.

27Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto. 28Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu.

Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo. 29Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi. 30Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo. 31Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.

New International Reader’s Version

Judges 18:1-31

The People of Dan Make Their Homes in Laish

1In those days Israel didn’t have a king.

And in those days the tribe of Dan was looking for a place where they could make their homes. They hadn’t been able to take over their own share of land among the tribes of Israel. 2So the people of Dan sent out five of their leading men from Zorah and Eshtaol. They told the men to look over the land and check it out. Those men did it for all the people of Dan. Those people told the men, “Go. Check out the land.”

So they entered the hill country of Ephraim. They went to the house of Micah. That’s where they spent the night. 3When they came near Micah’s house, they recognized a voice. It was the voice of the young Levite. So they turned off the road and stopped there. They asked him, “Who brought you here? What are you doing in this place? Why are you here?”

4The Levite told them what Micah had done for him. He said, “He has hired me. I’m his priest.”

5Then they said to him, “Please ask God for advice. Try to find out whether we’ll have success on our journey.”

6The priest answered them, “Go in peace. The Lord is pleased with your journey.”

7So the five men left. They came to Laish. There they saw that the people felt secure. They were living in safety. Like the people in Sidon, they were at peace. Their land had everything they needed. Things were going very well for them. They lived a long way from the people of Sidon. And they didn’t think they would ever need help from anyone else.

8The men returned to Zorah and Eshtaol. Their people asked them, “What did you find out?”

9They answered, “Come on! Let’s attack them! We’ve seen the land, and it is very good. Aren’t you going to do something? Don’t wait any longer. Go there and take it over. 10When you get there, you will find people who aren’t expecting anything bad to happen to them. Their land has plenty of room. God has handed it over to you. It’s a land that has everything you will ever need.”

11So 600 men from the tribe of Dan started out from Zorah and Eshtaol. They were prepared for battle. 12On their way they set up camp. Their camp was near Kiriath Jearim in Judah. That’s why the place is called Mahaneh Dan to this day. It’s west of Kiriath Jearim. 13From there they went to the hill country of Ephraim. They came to Micah’s house.

14Then the five men who had looked over the land of Laish spoke to the other members of their tribe. They said, “Don’t you know that one of these houses has a sacred linen apron in it? Some statues of family gods are there. That house also has another statue of a god covered with silver. Now you know what to do.” 15So they turned off the road and stopped there. They went to the house of the young Levite. He was at Micah’s place. They greeted the young man. 16The 600 men from Dan stood at the entrance of the gate. They were prepared for battle. 17The five men who had looked over the land went inside. They took the statue covered with silver. They also took the family gods and the linen apron. During that time, the priest stood at the entrance of the gate. The 600 men stood there with him. They were prepared for battle.

18When the five men went into Micah’s house and took all those things, the priest spoke to them. He asked, “What are you doing?”

19They answered him, “Be quiet! Don’t say a word. Come with us. Be our father and priest. You can serve a whole tribe and family group in Israel as our priest. Isn’t that better than serving just one man’s family?” 20The priest was very pleased. He took the linen apron and the family gods. He also took the statue of the god that was covered with silver. Then the priest left with the people. 21They put their little children and their livestock in front of them. They also put everything else they owned in front of them. And they turned and went on their way.

22The men who lived near Micah were called together. Then they left and caught up with the people of Dan. That’s because Dan’s people hadn’t gone very far from Micah’s house. 23Those who lived near Micah shouted at them. The people of Dan turned around and asked Micah, “What’s the matter with you? Why did you call out your men to fight against us?”

24He replied, “You took away the gods I made. And you took away my priest. What do I have left? So how can you ask, ‘What’s the matter with you?’ ”

25The people of Dan answered, “Don’t argue with us. Some of the men may get angry and attack you. Then you and your family will lose your lives.” 26So the people of Dan went on their way. Micah saw that they were too strong for him. So he turned around and went back home.

27The people of Dan took what Micah had made. They also took his priest. They continued on their way to Laish. They went there to fight against a people who were at peace and secure. The people of Dan struck them down with their swords. They burned down their city. 28No one could save those people and their city. They lived a long way from Sidon. And they didn’t think they would ever need help from anyone else. Their city was located in a valley near Beth Rehob.

The people of Dan rebuilt the city. Then they made their homes there. 29They named it Dan. That’s because they traced their family line back to Dan. He was a son of Israel. The city used to be called Laish. 30There the people of Dan set up for themselves the statue of the god that was covered with silver. Jonathan and his sons were priests for the tribe of Dan. Jonathan was the son of Gershom, the son of Moses. Jonathan and his sons were priests until the time when the land was captured. 31The people of Dan continued to use the statue Micah had made. They used it during the whole time the house of God was in Shiloh.