Oweruza 14 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Oweruza 14:1-20

Ukwati wa Samsoni

1Samsoni anapita ku Timna ndipo kumeneko anaonako mtsikana wa Chifilisiti. 2Atabwerera kwawo, anawuza abambo ndi amayi ake kuti, “Ine ndaona mtsikana wa Chifilisiti ku Timna, tsono mukanditengere ameneyo kuti akhale mkazi wanga.”

3Koma abambo ndi amayi ake anayankha kuti, “Kodi palibe mkazi pakati pa abale akowa kapena pakati pa anthu a mtundu wako, kuti iwe upite kukapeza mkazi kwa Afilisti anthu osachita mdulidwe?”

Koma Samsoni anawuza abambo ake kuti, “Kanditengereni ameneyu basi, pakuti ndamukonda.” 4(Abambo ndi amayi ake sankadziwa kuti zimenezi zinali zochokera kwa Yehova, pakuti Yehova amafuna powapezera chifukwa Afilistiwo. Nthawi imeneyo nʼkuti Afilisti akulamulira Aisraeli). 5Choncho Samsoni pamodzi ndi abambo ake anapita ku Timna. Akuyandikira minda ya mpesa ya ku Timna, mwadzidzidzi anamva kubuma kwa mkango waungʼono ukubwera kumene kunali iye. 6Tsono Mzimu wa Yehova unafika ndi mphamvu pa Samsoni ndipo ngakhale analibe chida mʼmanja mwake, iye anakadzula mkangowo ngati akukadzula mwana wambuzi. Koma sanawuze abambo kapena amayi ake zimene anachitazo. 7Kenaka Samsoni anapita kukakambirana ndi mkaziyo, ndipo anamukonda mtsikanayo.

8Patapita nthawi, Samsoni anabwerera kukatenga mtsikana uja. Panjira anapatuka kukaona mkango unawupha uja, ndipo anangoona njuchi zili mu mkangowo pamodzi ndi uchi wake. 9Tsono anakomberako uchi uja mʼmanja mwake ndi kumapita akudya. Atabwereranso kwa abambo ndi amayi ake, anawapatsako uchiwo ndipo anadya. Koma sanawawuze kuti uchi umenewo anawufula mu mkango wakufa.

10Tsopano Samsoni anapita ku nyumba kwa mtsikanayo. Ndipo kumeneko Samsoni anakonza phwando monga ankachitira anyamata. 11Makolo a mkwatibwiyo atamuona, anasankha anyamata makumi atatu kuti akhale naye.

12Samsoni anawawuza kuti, “Bwanji ndikuphereni mwambi. Mukandiwuza tanthauzo lake asanathe masiku asanu ndi awiri aphwandowa, ndidzakupatsani zovala makumi atatu za bafuta ndi zina makumi atatu za tsiku la chikondwerero. 13Koma ngati simutha kundiwuza tanthauzo lake, inuyo mudzandipatsa zovala makumi atatu zabafuta ndi zina za tsiku la chikondwerero.”

Iwo anamuyankha kuti, “Tiwuze mwambi wakowo tiwumve.”

14Iye anati,

“Chakudya chinatuluka mu chinthu chodya chinzake;

ndipo chozuna chinatuluka mu chinthu champhamvu.”

Panapita masiku atatu anthuwo akulephera kumasulira mwambiwo.

15Tsiku lachinayi anthuwo anawuza mkazi wa Samsoni kuti, “Umunyengerere mwamuna wako kuti akuwuze tanthauzo la mwambiwu. Ngati sutero tikutentha iweyo pamodzi ndi nyumba ya abambo ako. Kodi unatiyitana kuti mudzatilande zinthu zathu?”

16Kenaka mkazi wa Samsoni anayamba kulira pamaso pake namuwuza kuti, “Inu mumandida ndipo simundikonda. Mwaphera anyamata a mtundu wathu mwambi, koma ine wosandiwuza tanthauzo lake.”

Samsoni anamuyankha kuti, “Taona sindinawuze abambo kapena amayi anga, ndiye ndiwuze iweyo?” 17Mkaziyo anamulirira masiku onse asanu ndi awiri aphwandowo. Choncho pa tsiku lachisanu ndi chiwiri anamuwuza tanthauzo lake popeza amamukakamiza. Ndipo mkaziyo anakawuza abale ake aja tanthauzo la mwambiwo.

18Pambuyo pake anthu a mu mzinda aja anamuwuza Samsoni pa tsiku lachisanu ndi chiwiri dzuwa lisanalowe kuti,

“Chozuna nʼchiyani choposa uchi?

Champhamvu nʼchiyani choposa mkango?”

Samsoni anawawuza kuti,

“Mukanapanda kutipula ndi ngʼombe yanga yayingʼono,

simukanatha kumasulira mwambi wangawu.”

19Ndipo Mzimu wa Yehova unafika pa iye mwamphamvu. Choncho anatsikira ku Asikeloni naphako anthu makumi atatu, natenga zovala zawo za tsiku la chikondwerero napereka kwa anthu amene anamasulira mwambi wake. Kenaka anabwerera ku nyumba ya abambo ake ndi mkwiyo waukulu. 20Ndipo mkazi wa Samsoniyo anamukwatitsa kwa amene anali mnzake womuperekeza pa ukwati paja.

Thai New Contemporary Bible

ผู้วินิจฉัย 14:1-20

การแต่งงานของแซมสัน

1แซมสันลงไปยังเมืองทิมนาห์ และเห็นสาวชาวฟีลิสเตียคนหนึ่ง 2เมื่อเขากลับมาจึงบอกกับบิดามารดาว่า “ข้าพเจ้าเห็นสาวชาวฟีลิสเตียคนหนึ่งในทิมนาห์ ช่วยไปขอนางมาเป็นภรรยาของข้าพเจ้าด้วย”

3บิดามารดาทักท้วงว่า “ไม่มีผู้หญิงในหมู่ญาติพี่น้องหรือคนชาติเดียวกับเราถูกใจเจ้าสักคนเลยหรือ? เจ้าจึงต้องไปหาภรรยาจากพวกชาวฟีลิสเตียซึ่งไม่ได้เข้าสุหนัต”

แต่แซมสันพูดกับบิดาว่า “นางเป็นคนที่เหมาะกับข้าพเจ้า ช่วยไปขอนางมาให้ข้าพเจ้าเถิด” 4(บิดามารดาของแซมสันไม่รู้ว่าการนี้มาจากองค์พระผู้เป็นเจ้าผู้ทรงหาโอกาสที่จะเผชิญหน้ากับชาวฟีลิสเตียซึ่งขณะนั้นปกครองอิสราเอลอยู่) 5แซมสันกับบิดามารดาลงไปที่ทิมนาห์ ขณะที่พวกเขามาถึงสวนองุ่นแห่งทิมนาห์ ทันใดนั้นมีสิงโตหนุ่มคำรามกระโจนเข้าใส่แซมสัน 6พระวิญญาณขององค์พระผู้เป็นเจ้ามาสถิตกับแซมสัน และประทานกำลังมหาศาลแก่เขา จนเขาสามารถฉีกสิงโตออกจากกันด้วยมือเปล่าราวกับจับลูกแพะฉีกเป็นสองซีก แต่แซมสันไม่ได้บอกเรื่องนี้ให้บิดามารดาทราบ 7เมื่อมาถึงทิมนาห์ เขาได้พูดคุยกับสาวคนนั้นและเขาชอบนาง

8ต่อมาเมื่อแซมสันกลับไปอีกเพื่อแต่งงานกับนาง เขาแวะไปดูซากสิงโต ก็พบรวงผึ้งอยู่ในซากนั้นและมีน้ำผึ้งอยู่ด้วย 9เขาจึงนำน้ำผึ้งติดตัวไปด้วย เดินไปกินไป เมื่อเขาไปพบบิดามารดา เขาก็เอาน้ำผึ้งให้บิดามารดากินด้วย แต่ไม่ได้บอกว่าน้ำผึ้งนั้นมาจากซากสิงโต

10ขณะที่บิดาไปดูตัวผู้หญิงคนนั้น แซมสันจัดงานเลี้ยงขึ้นที่นั่นตามธรรมเนียมเจ้าบ่าว 11เมื่อผู้คนเห็นเขา พวกเขาก็เลือกชายหนุ่มสามสิบคนให้มาเป็นเพื่อนแซมสัน

12แซมสันกล่าวกับคนเหล่านั้นว่า “ขอให้เราทายปริศนาพวกเจ้าสักข้อหนึ่งเถิด ถ้าพวกเจ้าตอบได้ภายในงานเลี้ยงเจ็ดวันนี้ เราก็จะให้เสื้อผ้าลินินพร้อมเครื่องนุ่งห่มสามสิบชุด 13แต่ถ้าตอบไม่ได้ พวกเจ้าก็ต้องเป็นฝ่ายยกเสื้อผ้าลินินพร้อมเครื่องนุ่งห่มสามสิบชุดให้เรา”

พวกเขาจึงว่า “เอาเลย ทายมาสิ”

14แซมสันจึงกล่าวว่า

“อาหารออกมาจากผู้กิน

ความหวานออกมาจากผู้มีกำลัง”

ตลอดสามวันคนเหล่านั้นก็ยังแก้ปริศนาไม่ได้

15ในวันที่สี่14:15 ภาษาฮีบรูว่าวันที่เจ็ดพวกเขาจึงมาคาดคั้นภรรยาของแซมสันว่า “ไปตะล่อมเอาคำตอบจากสามีของเจ้ามาซิ ไม่อย่างนั้นเราจะเผาบ้านพ่อของเจ้าพร้อมกับตัวเจ้า มีอย่างหรือเชิญเรามาร่วมงานเลี้ยงนี้เพื่อจะให้เราหมดตัว?”

16ภรรยาของแซมสันจึงร้องไห้ฟูมฟายมาหาแซมสันและกล่าวว่า “ท่านเกลียดฉัน! ท่านไม่ได้รักฉันจริงถึงได้ตั้งปริศนาทายคนของฉัน แล้วไม่บอกคำตอบแก่ฉัน”

แซมสันตอบว่า “ขนาดพ่อกับแม่ของข้า ข้ายังไม่บอกเลย เรื่องอะไรข้าต้องบอกเจ้า” 17นางร้องไห้เซ้าซี้กับแซมสันทุกวันตลอดงานเลี้ยงทั้งเจ็ดวัน ในวันที่เจ็ดแซมสันก็บอกคำตอบแก่นาง เพราะนางเอาแต่เซ้าซี้เขา นางจึงนำคำตอบไปบอกคนของนาง

18ในวันที่เจ็ดก่อนดวงอาทิตย์ตกคนเหล่านั้นก็ทายปริศนาว่า

“อะไรเล่าจะหวานกว่าน้ำผึ้ง?

และอะไรเล่ามีกำลังมากกว่าสิงโต?”

แซมสันกล่าวกับเขาว่า

“ถ้าไม่ได้เอาแม่วัวของข้าไถ

พวกเจ้าก็ไม่มีวันทายปริศนาได้หรอก”

19แล้วพระวิญญาณขององค์พระผู้เป็นเจ้ามาสถิตกับแซมสันและประทานกำลังมหาศาลให้เขา เขาไปยังเมืองอัชเคโลน ฆ่าชายสามสิบคน ยึดเอาทรัพย์สินและเครื่องนุ่งห่มของคนเหล่านั้นมามอบให้ชายหนุ่มทั้งปวงที่ทายปริศนาของตน แต่แซมสันโกรธมากจึงกลับไปยังบ้านของบิดา 20ส่วนภรรยาของแซมสันนั้น พ่อตาก็ยกให้เพื่อนซึ่งมาร่วมงานแต่งงานของเขา