Nyimbo ya Solomoni 8 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 8:1-14

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,

amene anayamwa mawere a amayi anga!

Ndikanakumana nawe pa njira,

ndikanakupsompsona,

ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.

2Ndikanakutenga

ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

amayi amene anandiphunzitsa,

ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

zotsekemera za makangadza.

3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:

musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,

pamenepo ndi pamene amayi anachirira,

pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.

6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,

ngati chidindo cha pa dzanja lako;

pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,

nsanje ndiyaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti lawilawi

ngati malawi a moto wamphamvu.

7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

mitsinje singachikokolole chikondicho.

Ngati wina apereka chuma chonse

cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,

koma alibe mawere,

kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu

pa tsiku limene adzamufunsire?

9Ngati iye ndi khoma,

tidzamumangira nsanja ya siliva.

Ngati iye ndi chitseko,

tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo mawere anga ndi nsanja zake.

Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa

ndine wobweretsa mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;

iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,

aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.

12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000

ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13Iwe amene umakhala mʼminda

uli pamodzi ndi anzako,

ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14Fulumira wokondedwa wanga,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena mwana wa mbawala

wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Cantares 8:1-14

1¡Ah, si fueras mi propio hermano,

criado a los pechos de mi madre!

Al encontrarte en la calle podría besarte,

y nadie me juzgaría mal.

2Tomándote de la mano,

te llevaría a la casa de mi madre,

y me enseñarías el arte del amor.

Te daría a beber vino con especias,

y el néctar de mis granadas.

3¡Ojalá pudiera mi cabeza

reposar sobre su izquierda!

¡Ojalá su derecha me abrazara!

El amado

4Yo os ruego, mujeres de Jerusalén,

que no desveléis ni molestéis a mi amada,

hasta que ella quiera despertar.

Sexto Canto

El coro

5¿Quién es esta que sube por el desierto

apoyada sobre el hombro de su amado?

El amado

Bajo el manzano te desperté;

allí te concibió tu madre,

allí mismo te dio a luz.

La amada

6Grábame como un sello sobre tu corazón;

llévame como una marca sobre tu brazo.

Fuerte es el amor, como la muerte,

y tenaz la pasión, como el sepulcro.

Como llama divina

es el fuego ardiente del amor.

7Ni las muchas aguas pueden apagarlo,

ni los ríos pueden extinguirlo.

Si alguien ofreciera todas sus riquezas

a cambio del amor,

solo conseguiría el desprecio.

El coro

8Tan pequeña es nuestra hermana

que no le han crecido los pechos.

¿Qué haremos por nuestra hermana

cuando vengan a pedirla?

9Si fuera una muralla,

construiríamos sobre ella almenas de plata.

Si acaso fuera una puerta,

la recubriríamos con paneles de cedro.

La amada

10Una muralla soy yo,

y mis pechos, sus dos torres.

Por eso a los ojos de mi amado

soy como quien ha hallado la paz.

11Salomón tenía una viña en Baal Jamón,

que dejó al cuidado de aparceros.

Cada uno entregaba, por sus frutos,

mil monedas8:11 mil monedas de plata. Lit. mil [siclos] de plata. de plata.

12¡Quédate, Salomón, con las mil monedas,

y vosotros, aparceros, con doscientas,

pero mi viña solo a mí me pertenece!

El amado

13Tú, que reinas en los jardines,

pendientes de tu voz están nuestros amigos;

¡déjanos escucharla!

La amada

14¡Apresúrate, amado mío!

¡Corre como venado, como cervatillo,

sobre los montes de bálsamo cubiertos!