Nyimbo ya Solomoni 8 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 8:1-14

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,

amene anayamwa mawere a amayi anga!

Ndikanakumana nawe pa njira,

ndikanakupsompsona,

ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.

2Ndikanakutenga

ndi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

amayi amene anandiphunzitsa,

ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,

zotsekemera za makangadza.

3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:

musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

Abwenzi

5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,

atatsamira wokondedwa wakeyo?

Mkazi

Ndinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,

pamenepo ndi pamene amayi anachirira,

pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.

6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,

ngati chidindo cha pa dzanja lako;

pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,

nsanje ndiyaliwuma ngati manda.

Chikondi chimachita kuti lawilawi

ngati malawi a moto wamphamvu.

7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,

mitsinje singachikokolole chikondicho.

Ngati wina apereka chuma chonse

cha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,

adzangonyozeka nazo kotheratu.

Abwenzi

8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,

koma alibe mawere,

kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyu

pa tsiku limene adzamufunsire?

9Ngati iye ndi khoma,

tidzamumangira nsanja ya siliva.

Ngati iye ndi chitseko,

tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.

Mkazi

10Ine ndili ngati khoma,

ndipo mawere anga ndi nsanja zake.

Tsono mʼmaso mwa bwenzi langa

ndine wobweretsa mtendere.

11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;

iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,

aliyense mwa iwo ankayenera kupereka

ndalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.

12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.

Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000

ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.

Mwamuna

13Iwe amene umakhala mʼminda

uli pamodzi ndi anzako,

ndilole kuti ndimve liwu lako!

Mkazi

14Fulumira wokondedwa wanga,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena mwana wa mbawala

wothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.

Bibelen på hverdagsdansk

Højsangen 8:1-14

1Hvis du havde været min bror,

som havde diet ved min mors bryst,

så kunne jeg have kysset dig i alles påsyn,

uden at nogen ville blive forarget.

2Så ville jeg have taget dig med til min mors hus,

hende som oplærte mig,

og have givet dig krydret vin og granatæblemost.”

Den unge pige til de andre piger:

3„Han lagde sin venstre hånd under mit hoved

og omfavnede mig med sin højre.

4Jerusalems unge piger,

lov mig, at I ikke vækker kærligheden, før tiden er inde.”

Jerusalems unge piger til hinanden:

5„Hvem er den pige, der kommer gående fra ødemarken,

lænet til sin elskede?”

Den unge pige:

„Under det æbletræ, hvor du selv blev undfanget,

og din mor fødte dig med smerte—

dér vækkede jeg din lidenskab.

6Lad mig være så tæt på dig,

som var jeg stemplet på dit hjerte,

eller sad som en ring på din arm.

For kærligheden er stærk som døden,

lidenskaben er uimodståelig som dødsriget selv:

den brænder med voldsomme flammer, som ikke kan slukkes.

7Vand i mængde kan ikke slukke kærligheden,

floder kan ikke skylle den bort.

Kærlighed kan ikke købes for penge,

den, der forsøger det, får kun foragt.”

Sjette sang: Pigen, som ventede, til tiden var inde

Den unge piges brødre:

8„Vi havde en lillesøster, som endnu ikke havde bryster.

Hvad skulle vi gøre, hvis der kom en frier til hende?

9Stod hun imod fristelsen som en mur,

ville vi ære hende med sølvsmykker.

Men åbnede hun sig som en dør,

ville vi spærre hende af med cedertræsplanker.”

Den unge pige:

10„Jeg stod imod som en mur,

og mine bryster er nu som tårne.

Derfor vidste han, at jeg ville bringe ham glæde og fred.

11Salomon havde en vingård i Ba’al-Hamon,

som han overlod til forpagtere.

De måtte hver betale tusind stykker sølv

for at kunne få høsten af vindruer.

12Min ‚vingård’ tilhører mig,

den bestemmer jeg selv over.

Men jeg har givet den til dig, Salomon,

og du kan godt beholde dine tusind sølvstykker,

men de, der har passet på den8,12 Sandsynligvis den unge piges brødre, som har passet godt på hende. indtil nu,

bør have tohundrede.”

Den unge mand:

13„Oh, du, der vandrer rundt i den dejlige have,

mine venner vil gerne høre din stemme.

Men lad mig være den, der får lov til det!”

Den unge pige:

14„Kom, min elskede,

lad os springe af fryd som gazellen

på de duftende bakkeskråninger.”