Nyimbo ya Solomoni 7 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 7:1-13

1Iwe namwali waufumu, mapazi ako ngokongola

mu nsapato wavalazo!

Ntchafu zako nʼzowumbika bwino ngati miyala yamtengowapatali,

ntchito ya manja ya mmisiri waluso.

2Mchombo wako uli ngati chikho chowumbika bwino

chimene nthawi zonse ndi chodzaza ndi vinyo.

Chiwuno chako ndi choningʼa ngati mtolo wa tirigu

utazunguliridwa ndi maluwa okongola.

3Mawere ako akuoneka ngati ana awiri a mbawala,

ngati mphoyo zamapasa.

4Khosi lako lili see! ngati nsanja ya mnyanga wa njovu.

Maso ako ali ngati mayiwe a ku Hesiboni,

amene ali pafupi ndi chipata cha Bati Rabimu.

Mphuno yako ili ngati nsanja ya ku Lebanoni,

yoyangʼana ku Damasiko.

5Mutu wako uli bwinobwino nengʼaa ngati phiri la Karimeli.

Tsitsi lako lili ngati nsalu yakuda yaufumu;

mfumu yakopeka ndi maonekedwe ake okongola.

6Ndiwe wokongola kwambiri ndiponso wosangalatsa,

iwe wokondedwa, namwali wokondweretsawe!

7Msinkhu wako uli ngati mtengo wa mgwalangwa,

ndipo mawere ako ali ngati phava la zipatso.

8Ndinati, “Ndikwera mtengo wa mgwalangwa;

ndidzathyola zipatso zake.”

Mawere ako ali ngati maphava a mphesa,

fungo la mpweya wako lili ngati ma apulosi,

9ndipo pakamwa pako pali ngati vinyo wokoma kwambiri.

Mkazi

Tsono vinyo ameneyu amuthirire wachikondi wanga,

ayenderere bwino pa milomo yake ndi mano ake.

10Wokondedwayo ine ndine wake,

ndipo chilakolako chake chili pa ine.

11Bwera wachikondi wanga, tiye tipite ku madera a ku midzi,

tikagone ku midzi.

12Tiye tilawirire mmamawa kupita ku minda ya mpesa,

tikaone ngati mitengo ya mpesa yayamba kuphukira,

ngati maluwa ake ayamba kuoneka,

komanso ngati makangadza ayamba kuonetsa maluwa.

Kumeneko ndidzakuonetsa chikondi changa.

13Mitengo ya mankhwala a chisulo ikupereka fungo lake labwino,

ndipo pa khomo pathu pali zipatso zonse zokoma,

zatsopano ndi zakale zomwe,

zimene ndakusungira wokondedwa wanga.

Luganda Contemporary Bible

Oluyimba 7:1-13

17:1 Zab 45:13Ebigere byo nga birabika bulungi mu ngatto,

ggwe omumbejja!

Amagulu go gali ng’amayinja ag’omuwendo,

omulimu gw’omuweesi omukalabakalaba.

2Ekkundi lyo kibya kyekulungirivu,

ekitaggwaamu nvinnyo entabule obulungi.

Ekiwato kyo ntuumu ya ŋŋaano

eyeetooloddwa amalanga.

37:3 Lu 4:5Amabeere go gali ng’abaana b’empeewo,

abalongo.

47:4 a Zab 144:12; Lu 4:4 b Kbl 21:26 c Lu 5:15Ensingo yo eri ng’omunaala ogw’amasanga.

Amaaso go gali ng’ebidiba eby’omu Kesuboni

ebiri ku mulyango ogw’e Basulabbimu.

Ennyindo yo eri ng’omulongooti ogw’e Lebanooni

ogwolekera Ddamasiko.

57:5 Is 35:2Omutwe gwo gukuwoomera ng’olusozi Kalumeeri,

n’enviiri zo ziranga emiguwa egy’effulungu;

Kabaka asendebwasendebwa ebintu byakwo.

67:6 a Lu 1:15 b Lu 4:10Ng’olabika bulungi, ng’osanyusa

ggwe omwagalwa n’obulungi bwo.

77:7 Lu 4:5Oli muwanvu ng’olukindu,

n’amabeere go gali ng’ebirimba eby’ebibala byakwo.

87:8 Lu 2:5Nayogera nti, “Ndirinnya olukindu,

era ndikwata ebibala byalwo.”

Amabeere go gabeere ng’ebirimba eby’oku muzabbibu,

n’akawoowo ak’omu kamwa ko ng’ebibala eby’omucungwa

97:9 Lu 5:16n’akamwa ko nga nvinnyo esinga obulungi.

Omwagalwa

Ne wayini amirwe bulungi muganzi wange,

ng’akulukuta mpola mpola ku mimwa gy’abo abeebase.

107:10 a Zab 45:11 b Lu 2:16; 6:3Ndi wa muganzi wange,

era naye anjagala nnyo.

11Jjangu, muganzi wange tugende ebweru w’ekibuga,

tusuleko mu byalo.

127:12 a Lu 1:6 b Lu 2:15 c Lu 2:13 d Lu 4:13 e Lu 6:11Tukeere tugende mu nnimiro z’emizabbibu,

tulabe obanga emizabbibu gimulisizza,

obanga n’ebimuli byagwo byanjuluzza,

obanga n’emikomamawanga gimulisizza,

era eyo gye nnaakulagira okwagala kwange.

137:13 a Lub 30:14 b Lu 4:16Amadudayimu7:13 Amadudayimu gayamba mu by’okuzaala gawunya akawoowo,

ne ku miryango gyaffe waliwo ebibala ebisinga obulungi,

Ebyakanogebwa awamu n’ebikadde,

bye nkuterekedde muganzi wange.