Nyimbo ya Solomoni 6 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 6:1-13

Abwenzi

1Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo wapita kuti?

Kodi wokondedwa wakoyo wakhotera njira iti

kuti timufunefune pamodzi ndi iwe?

Mkazi

2Wachikondi wanga watsikira ku munda kwake,

ku timinda ta zokometsera zakudya,

akukadyetsa ziweto zake ku minda,

ndiponso akuthyola maluwa okongola.

3Wokondedwa wangayo ndine wake ndipo iyeyo ndi wangawanga;

amadyetsa ziweto zake pakati pa maluwa okongola.

Mwamuna

4Ndiwe wokongola, bwenzi langa, ngati Tiriza,

wokongola kwambiri ngati Yerusalemu,

ndiwe woopsa ngati gulu lankhondo lonyamula mbendera.

5Usandipenyetsetse;

pakuti maso ako amanditenga mtima.

Tsitsi lako lili ngati gulu la mbuzi

zikutsetsereka kuchokera ku Giliyadi.

6Mano ako ali ngati gulu la nkhosa

zimene zikubwera kuchokera kokazisambitsa,

iliyonse ili ndi ana amapasa,

palibe imene ili yokha.

7Kukhalira kumbuyo kwa nsalu yako yophimba kumutu,

masaya ako ali ngati mabandu a makangadza.

8Ngakhale patakhala akazi a mfumu 60,

ndi azikazi 80,

ndi anamwali osawerengeka;

9koma nkhunda yanga, wangwiro wanga ndi wosiyana ndi wina aliyense;

mwana wamkazi yekhayo wa amayi ake,

mwana wapamtima wa amene anamubereka.

Anamwali anamuona ndipo anamutcha wodala;

akazi a mfumu ndi azikazi anamutamanda.

Abwenzi

10Ndani uyu akuoneka ngati mʼbandakucha,

wokongola ngati mwezi, wowala ngati dzuwa,

wochititsa mantha ngati gulu la ankhondo mbendera zili mʼmanja?

Mwamuna

11Ndinatsikira ku munda wa mitengo ya alimondi

kukayangʼana zomera zatsopano ku chigwa,

kukaona ngati mpesa waphukira

kapena ngati makangadza ali ndi maluwa.

12Ndisanazindikire kanthu,

ndinakhala ngati ndikulota kuti ndili mʼgaleta pambali pa mfumu yanga.

Abwenzi

13Bwerera, bwerera iwe namwali wa ku Sulami;

bwerera, bwerera kuti ife tidzakupenyetsetse iwe!

Mwamuna

Chifukwa chiyani mukufuna kudzapenyetsetsa ine mwana wamkazi wa ku Sulami,

pamene ndikuvina pakati pa magulu awiri?

King James Version

Song of Solomon 6:1-13

1Whither is thy beloved gone, O thou fairest among women? whither is thy beloved turned aside? that we may seek him with thee. 2My beloved is gone down into his garden, to the beds of spices, to feed in the gardens, and to gather lilies. 3I am my beloved’s, and my beloved is mine: he feedeth among the lilies.

4¶ Thou art beautiful, O my love, as Tirzah, comely as Jerusalem, terrible as an army with banners. 5Turn away thine eyes from me, for they have overcome me: thy hair is as a flock of goats that appear from Gilead.6.5 overcome…: or, puffed me up 6Thy teeth are as a flock of sheep which go up from the washing, whereof every one beareth twins, and there is not one barren among them. 7As a piece of a pomegranate are thy temples within thy locks. 8There are threescore queens, and fourscore concubines, and virgins without number. 9My dove, my undefiled is but one; she is the only one of her mother, she is the choice one of her that bare her. The daughters saw her, and blessed her; yea, the queens and the concubines, and they praised her.

10¶ Who is she that looketh forth as the morning, fair as the moon, clear as the sun, and terrible as an army with banners?

11I went down into the garden of nuts to see the fruits of the valley, and to see whether the vine flourished, and the pomegranates budded. 12Or ever I was aware, my soul made me like the chariots of Amminadib.6.12 Or ever…: Heb. I knew not6.12 made…: or, set me on the chariots of my willing people 13Return, return, O Shulamite; return, return, that we may look upon thee. What will ye see in the Shulamite? As it were the company of two armies.6.13 of…: or, of Mahanaim