Nyimbo ya Solomoni 5 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 5:1-16

Mwamuna

1Ndalowa mʼmunda mwanga, iwe mlongo wanga, iwe mkwatibwi wanga;

ndasonkhanitsa mure wanga ndi zokometsera zakudya zanga.

Ndadya uchi wanga pamodzi ndi zisa zake zomwe;

ndamwa vinyo wanga ndi mkaka wanga.

Abwenzi

Idyani abwenzi anga, imwani;

Inu okondana, imwani kwambiri.

Mkazi

2Ndinagona tulo koma mtima wanga unali maso.

Tamverani, bwenzi langa akugogoda:

“Nditsekulire, mlongo wanga, bwenzi langa,

nkhunda yanga, wangwiro wanga.

Mutu wanga wanyowa ndi mame,

tsitsi langa lanyowa chifukwa cha nkhungu ya usiku.”

3Ndavula kale zovala zanga,

kodi ndizivalenso?

Ndasamba kale mapazi anga

kodi ndiwadetsenso?

4Bwenzi langa anapisa dzanja lake pa chibowo cha pa chitseko;

mtima wanga unagunda chifukwa cha iye.

5Ndinanyamuka kukamutsekulira wachikondi wangayo,

ndipo manja anga anali noninoni ndi mure,

zala zanga zinali mure chuchuchu,

pa zogwirira za chotsekera.

6Ndinamutsekulira wachikondi wanga,

koma nʼkuti wachikondi wangayo atachoka; iye anali atapita.

Mtima wanga unafumuka chifukwa cha kuchoka kwake.

Ndinamuyangʼanayangʼana koma sindinamupeze.

Ndinamuyitana koma sanandiyankhe.

7Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzindawo.

Anandimenya ndipo anandipweteka;

iwo anandilanda mwinjiro wanga,

alonda a pa khoma aja!

8Inu akazi a ku Yerusalemu ndithu ndikukupemphani,

mukapeza wokondedwa wangayo,

kodi mudzamuwuza chiyani?

Muwuzeni kuti ine ndadwala nacho chikondi.

Abwenzi

9Iwe wokongola kuposa akazi onsewa,

kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana wina aliyense bwanji?

Kodi wokondedwa wakoyo ndi wopambana ena onse chotani

kuti uzichita kutipempha motere?

Mkazi

10Wokondedwa wangayo ndi wowala kwambiri ndi wathanzi

pakati pa anthu 1,000.

11Mutu wake ndi golide woyengeka bwino;

tsitsi lake ndi lopotanapotana,

ndiponso lakuda bwino ngati khwangwala.

12Maso ake ali ngati nkhunda

mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,

ngati nkhunda zitasamba mu mkaka,

zitayima ngati miyala yamtengowapatali.

13Masaya ake ali ngati timinda ta mbewu zokometsera zakudya

zopatsa fungo lokoma.

Milomo yake ili ngati maluwa okongola

amene akuchucha mure.

14Manja ake ali ngati ndodo zagolide

zokongoletsedwa ndi miyala yamtengowapatali.

Thupi lake ndi losalala ngati mnyanga wanjovu

woyikamo miyala ya safiro.

15Miyendo yake ili ngati mizati yamwala,

yokhazikika pa maziko a golide.

Maonekedwe ake ali ngati Lebanoni,

abwino kwambiri ngati mkungudza.

16Milomo yake ndi yosangalatsa kwambiri;

munthuyo ndi wokongola kwambiri!

Uyu ndiye wachikondi wanga ndi bwenzi langa,

inu akazi a ku Yerusalemu.

Het Boek

Hooglied 5:1-16

1Ik ben bij mijn zuster, mijn bruid, gekomen als in een tuin. Ik heb mirre en balsem geplukt en at honing uit de raat. Ik dronk wijn en melk. Mijn vrienden, kom erbij! Eet en drink met mij mee.

2In mijn droom hoorde ik hoe mijn liefste aan mijn deur klopte. Hij riep mij: ‘Mijn zusje, mijn allerliefste, doe open. Ik hou van je, jij bent alles voor mij. Mijn haar is helemaal nat van de dauw.’

3‘Dat kan ik toch niet doen?’ antwoordde ik. ‘Ik ben al klaar voor de nacht. Moet ik mij dan weer aankleden? Ik ben al gewassen, straks word ik weer vuil.’

4Mijn liefste stak zijn hand door de deuropening en toen kon ik hem niet weerstaan.

5Ik stond op om hem open te doen. Mijn handen beefden toen ik de grendels losmaakte.

6Ik ontsloot de deur voor mijn liefste, maar toen die open ging, was hij verdwenen! Terwijl hij tegen mij sprak, trilde ik van opwinding. Ik ging naar hem op zoek, maar kon hem nergens vinden. Als ik zijn naam riep, kreeg ik geen antwoord.

7Ik kwam de mannen tegen die ʼs nachts de wacht houden over de stad. Zij sloegen en mishandelden mij. Zij rukten mij mijn sluier af.

8Meisjes van Jeruzalem, ik zeg het jullie met nadruk: als jullie mijn liefste vinden, weten jullie wat je dan tegen hem moet zeggen? Dat mijn liefde voor hem mij te veel wordt.

9Maar allermooiste van alle vrouwen, wat is er dan zo bijzonder aan uw liefste? Wat heeft hij meer dan een ander dat u ons met zoʼn sterke nadruk toespreekt?

10Mijn liefste blaakt van gezondheid. Je haalt hem er zo tussenuit, al zijn er tienduizend mannen.

11Als fijn gezuiverd goud is hij te onderscheiden van alle anderen. Zijn haar is zwart en krullend.

12Hij heeft prachtige ogen die lijken op badende duiven.

13Zijn wangen geuren naar kruiden en zijn lippen lijken op lelies waar de mirre vanaf stroomt.

14Zijn armen zijn als goud, bedekt met blauwe edelstenen. Zijn lichaam lijkt wel een ivoren beeldhouwwerk, overdekt met saffieren.

15Zijn benen lijken op zuilen, gehouwen uit wit marmer, met voeten van zuiver goud. Zijn lichaam is fier als de ceders in de Libanon.

16Zijn kussen zijn zoet en liefdevol, alles aan hem is prachtig. Meisjes van Jeruzalem, nu weten jullie hoe mijn liefste, mijn vriend, is.