Nyimbo ya Solomoni 3 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 3:1-11

1Usiku wonse ndili pa bedi langa

ndinafunafuna amene mtima wanga umamukonda;

ndinamufunafuna koma osamupeza.

2Ndikudzuka tsopano ndipo ndidzayendayenda mu mzinda,

mʼmisewu yake ndi mʼmabwalo ake;

ndidzamufunafuna amene mtima wanga umamukonda.

Kotero ine ndinamufunafuna iyeyo koma osamupeza.

3Alonda anandipeza

pamene ankayendera mzinda.

“Kodi mwamuonako amene mtima wanga umamukonda?”

4Nditawapitirira pangʼono

ndinamupeza amene mtima wanga umamukonda.

Ndinamugwira ndipo sindinamulole kuti achoke

mpaka nditamulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,

mʼchipinda cha amene anandibereka.

5Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

6Kodi ndani amene akubwera kuchokera ku chipululu

ngati utsi watolotolo,

wonunkhira mure ndi lubani,

zopangidwa kuchokera ku zonunkhira zonse za anthu amalonda?

7Ona! Chimenecho ndi chonyamulira Solomoni,

choperekezedwa ndi asilikali 60,

anthu amphamvu a ku Israeli,

8onse atanyamula lupanga,

onse odziwa bwino nkhondo,

aliyense ali ndi lupanga pambali pake,

kukonzekera zoopsa za usiku.

9Mfumu Solomoni anadzipangira chonyamulirachi;

anachipanga ndi matabwa ochokera ku Lebanoni.

10Milongoti yake anayipanga yasiliva,

kumbuyo kwake kwa golide.

Mipando yake inakutidwa ndi nsalu yapepo,

anakongoletsa mʼkati mwake ndi chikondi

cha akazi a ku Yerusalemu.

11Tukulani inu akazi a ku Ziyoni

ndipo mudzaone mfumu Solomoni atavala chipewa chaufumu,

chipewa chaufumu chimene amayi ake anamuveka

pa tsiku la ukwati wake,

tsiku limene mtima wake unasangalala.

La Bible du Semeur

Cantiques 3:1-11

Pensées nocturnes

1Sur mon lit, au long de la nuit,

j’ai recherché ╵celui que mon cœur aime.

Je l’ai cherché, ╵mais ne l’ai pas trouvé.

2Je me suis dit alors : ╵Il faut que je me lève,

je ferai le tour de la ville ╵par les rues et les places,

je chercherai partout ╵celui que mon cœur aime.

Je l’ai cherché, ╵mais ne l’ai pas trouvé.

3Les gardes m’ont trouvée, ╵ceux qui font le tour de la ville3.3 Les gardes se tenaient la nuit près de la porte (Né 3.29 ; 11.19 ; 13.22) ou sur les remparts (5.7 ; 2 S 13.34 ; 18.24-27 ; 2 R 9.17-20 ; Ps 127.1 ; Es 52.8 ; 62.6). Sans doute patrouillaient-ils aussi dans la ville (5.7)..

Je leur ai demandé : ╵Celui que mon cœur aime, ╵ne l’avez-vous pas vu ?

4Les ayant dépassés,

peu après, j’ai trouvé ╵celui que mon cœur aime.

Je l’ai saisi bien fort, ╵et ne l’ai plus lâché

jusqu’à l’avoir conduit ╵au logis de ma mère,

dans la chambre de celle ╵qui m’a conçue.

5O filles de Jérusalem, ╵oh, je vous en conjure

par les gazelles ╵ou par les biches ╵de la campagne :

n’éveillez pas, ╵non, ne réveillez pas l’amour

avant qu’il ne le veuille3.5 Voir 2.7 et note ; 8.4.. »

Cortège royal

6« Qui donc est celle-ci ╵qui monte du désert3.6 Voir 8.5. Le désert est celui de Judée, c’est-à-dire les collines incultes entourant Jérusalem.

comme un nuage de fumée,

aux senteurs de myrrhe et d’encens

et de tous parfums exotiques ?

7Voici la litière de Salomon

escortée de ses soixante guerriers,

l’élite des guerriers en Israël.

8Tous armés de l’épée,

exercés au combat,

ils ont leur épée au côté

pour parer aux terreurs nocturnes.

9Le palanquin3.9 Sans doute la litière mentionnée au v. 7 et qui devait être richement ornée. royal ╵fait sur ordre de Salomon

est en bois du Liban.

10Ses colonnes sont en argent,

son dossier3.10 Terme de sens incertain. Autres traductions : lit, siège, base, support, trône. est en or,

son siège est fait en pourpre.

Les filles de Jérusalem

ont tapissé avec amour ╵tout l’intérieur du palanquin.

11O filles de Sion, sortez, ╵contemplez le roi Salomon

portant le diadème ╵dont le ceignit sa mère

au jour de son mariage,

au jour où tout son cœur ╵était rempli de joie. »