Nyimbo ya Solomoni 2 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyimbo ya Solomoni 2:1-17

Mkazi

1Ine ndine duwa la ku Saroni,

duwa lokongola la ku zigwa.

Mwamuna

2Monga duwa lokongola pakati pa minga

ndi momwe alili wokondedwa wanga pakati pa atsikana.

Mkazi

3Monga mtengo wa apulosi pakati pa mitengo ya mʼnkhalango

ndi momwe alili bwenzi langa pakati pa anyamata.

Ndimakondwera kukhala pansi pa mthunzi wako,

ndipo chipatso chake ndi chokoma mʼkamwa mwanga.

4Iye wanditengera ku nyumba yaphwando,

ndipo mbendera yake yozika pa ine ndi chikondi.

5Undidyetse keke ya mphesa zowuma,

unditsitsimutse ndi ma apulosi,

pakuti chikondi chandifowoketsa.

6Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzere,

ndipo dzanja lake lamanja landikumbatira.

7Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani

pali gwape ndi mbawala yayikazi zakuthengo:

Musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsa

mpaka pamene chifunire ichocho.

8Tamverani bwenzi langa!

Taonani! Uyu akubwera apayu,

akulumphalumpha pa mapiri,

akujowajowa pa zitunda.

9Bwenzi langa ali ngati gwape kapena mwana wa mbawala.

Taonani! Uyo wayima kuseri kwa khoma lathulo,

akusuzumira mʼmazenera,

akuyangʼana pa mpata wa zenera.

10Bwenzi langa anayankha ndipo anati kwa ine,

“Dzuka bwenzi langa,

wokongola wanga, ndipo tiye tizipita.

11Ona, nyengo yozizira yatha;

mvula yatha ndipo yapitiratu.

12Maluwa ayamba kuoneka pa dziko lapansi;

nthawi yoyimba yafika,

kulira kwa njiwa kukumveka

mʼdziko lathu.

13Mtengo wankhuyu ukubereka zipatso zake zoyambirira;

mitengo ya mpesa ya maluwa ikutulutsa fungo lake.

Dzuka bwenzi langa, wokongola wanga

tiye tizipita.”

Mwamuna

14Nkhunda yanga yokhala mʼmingʼalu ya thanthwe,

mʼmalo obisala a mʼmbali mwa phiri,

onetsa nkhope yako,

nʼtamvako liwu lako;

pakuti liwu lako ndi lokoma,

ndipo nkhope yako ndi yokongola.

15Mutigwirire nkhandwe,

nkhandwe zingʼonozingʼono

zimene zikuwononga minda ya mpesa,

minda yathu ya mpesa imene yayamba maluwa.

Mkazi

16Bwenzi langa ndi wangadi ndipo ine ndine wake;

amadyetsa gulu lake la ziweto pakati pa maluwa okongola.

17Kamphepo kamadzulo kakayamba kuwuzira

ndipo mithunzi ikayamba kuthawa,

unyamuke bwenzi langa,

ndipo ukhale ngati gwape

kapena ngati mwana wa mbawala

pakati pa mapiri azigwembezigwembe.

O Livro

Cântico de Salomão 2:1-17

Ela

1Eu sou a rosa de Sarom, o lírio dos vales.

Ele

2Sim, um lírio entre espinhos;

assim é a minha querida,

quando a comparo às outras.

Ela

3O meu amado é como uma macieira,

no meio das árvores do pomar,

quando comparado com outros rapazes.

Sento-me à sua desejada sombra;

o seu fruto é doce ao meu paladar.

4Leva-me a beber na sala de banquetes

e ergue sobre mim o estandarte do amor.

5Sustém-me com fruta, com uvas, com maçãs,

pois estou desfalecendo de amor.

6Põe a sua mão esquerda debaixo da minha cabeça

e com a direita abraça-me.

7Ó filhas de Jerusalém, conjuro-vos,

pelas gazelas e cervas dos bosques,

que não acordem o meu amado,

até que ele queira!

8Já o ouço, o meu amor!

Lá vem ele, galopando sobre os montes,

saltando por cima das colinas.

9O meu querido é como uma gazela,

ou o filho dum veado.

Vejam, aí está ele, por detrás do nosso muro;

agora, está já a olhar pelas janelas!

10Disse-me o meu amor:

“Levanta-te, querida, minha bela, e vem!

11Porque já passou o inverno;

a chuva parou e foi-se.

12As flores começam a brotar nos campos;

é o tempo de cantar e de podar;

ouve-se o cantar da rola nos nossos campos.

13As figueiras começam a dar os seus primeiros figos,

e os cachos começam a aparecer nas vinhas.

Já começam a cheirar bem!

Levanta-te, amor, minha linda, e vem!”

Ele

14Minha pomba, que te escondes nas fendas das penhas,

no fundo dos desfiladeiros,

faz-me ouvir a tua voz tão doce;

mostra-me o teu rosto encantador.

15As raposinhas andam correndo pelas vinhas.

Apanhem-nas,

porque os cachos estão já todos a desabrochar.

Ela

16O meu amor é meu e eu sou dele.

Ele apascenta o seu rebanho entre os lírios!

17Antes que refresque o dia e caiam as sombras,

volta, meu querido;

faz-te semelhante a uma gazela,

ou ao filho dum veado sobre os montes de Beter.