Numeri 7 – CCL & HLGN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 7:1-89

Zopereka Popatula Chihema

1Mose atamaliza kuyimika chihema chija, anachidzoza mafuta ndi kuchipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. Anadzozanso guwa lansembe ndi kulipatula pamodzi ndi ziwiya zake zonse. 2Kenaka atsogoleri a Aisraeli, akuluakulu a mabanja omwe ankayangʼanira mafuko a anthu omwe anawawerenga aja, anachita chopereka. 3Anabweretsa zopereka zawo pamaso pa Yehova: ngolo zophimbidwa zisanu ndi imodzi ndiponso ngʼombe zothena khumi ndi ziwiri. Mtsogoleri mmodzi ngʼombe yothena imodzi ndipo atsogoleri awiri ngolo imodzi. Izi anazipereka ku chihema.

4Yehova anawuza Mose kuti, 5“Ulandire zimenezi kwa iwo kuti zigwire ntchito ku tenti ya msonkhano. Uzipereke kwa Alevi, aliyense monga mwa ntchito yake.”

6Choncho Mose anatenga ngolo ndi ngʼombe zothenazo nazipereka kwa Alevi. 7Anapereka ngolo ziwiri ndi ngʼombe zothena zinayi kwa Ageresoni monga mwantchito yawo 8ndiponso anapereka ngolo zinayi ndi ngʼombe zothena zisanu ndi zitatu kwa Amerari molingananso ndi ntchito yawo. Onsewa ankawayangʼanira anali Itamara mwana wa Aaroni wansembe. 9Koma Mose sanapereke zimenezi kwa Akohati chifukwa zinthu zawo zopatulika zomwe ankayangʼanira zinali zoti azinyamula pa mapewa awo.

10Guwa la nsembe litadzozedwa, atsogoleri anabweretsa zopereka zawo zopatulira guwa nazipereka paguwapo. 11Pakuti Yehova anawuza Mose kuti, “Tsiku lililonse mtsogoleri mmodzi azibweretsa chopereka chake chopatulira guwa lansembe.”

12Amene anabweretsa chopereka chake tsiku loyamba anali Naasoni mwana wa Aminadabu wa fuko la Yuda.

13Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, ndi beseni lasiliva limodzi lowazira, lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo wopatulika ndipo zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta ngati chopereka chachakudya; 14mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 15mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 16mbuzi yayimuna imodzi, nsembe ya machimo; 17ndi ngʼombe zothena ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi kuti zikhale za nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Naasoni mwana wa Aminadabu.

18Pa tsiku lachiwiri, Natanieli mwana wa Zuwara, mtsogoleri wa Isakara, anabweretsa chopereka chake.

19Chopereka chomwe anabwera nacho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, molingana ndi muyeso wa ku malo opatulika. Mbale zonse zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha chakudya. 20Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110 yodzaza ndi lubani; 21mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza: 22mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yotetezera machimo; 23ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa asanu a chaka chimodzi, nsembe ya chiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Netanieli mwana wa Zuwara.

24Pa tsiku lachitatu, Eliabu mwana wa Heloni, mtsogoleri wa Azebuloni, anabweretsa chopereka chake.

25Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, mbale zonse zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka cha chakudya; 26mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 27mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 28mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 29ndi ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliabu mwana wa Heloni.

30Tsiku lachinayi linali la Elizuri mwana wa Sedeuri, mtsogoleri wa fuko la Rubeni, anabweretsa chopereka chake.

31Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, chopereka chachakudya. 32Mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 33mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 34mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 35ndi ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elizuri mwana wa Sedeuri.

36Pa tsiku lachisanu Selumieli mwana wa Zurisadai, mtsogoleri wa fuko la Simeoni, anabweretsa chopereka chake.

37Chopereka chake chinali mbale yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 38mbale yagolide imodzi yolemera 110, yodzaza ndi lubani; 39mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wamwamuna wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 40mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 41ngʼombe ziwiri, nkhosa zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Selumieli mwana wa Zurisadai.

42Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi, Eliyasafu mwana wa Deuweli, mtsogoleri wa fuko la Gadi, anabweretsa chopereka chake.

43Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 44mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 45mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, chopereka cha nsembe yopsereza: 46mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 47ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Eliyasafu mwana wa Deuweli.

48Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri Elisama mwana wa Amihudi, mtsogoleri wa fuko la Efereimu, anabweretsa chopereka chake.

49Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonsezi monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 50mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 51mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa wamwamuna mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 52mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 53ngʼombe ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Elisama mwana wa Amihudi.

54Pa tsiku lachisanu ndi chitatu Gamalieli mwana wa Pedazuri, mtsogoleri wa fuko Manase, anabweretsa chopereka chake.

55Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndi beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 56mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani, 57mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 58mbuzi imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 59ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu ndi ana ankhosa a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Gamalieli mwana wa Pedazuri.

60Pa tsiku lachisanu ndi chinayi Abidani mwana wa Gideoni mtsogoleri wa fuko la Benjamini, anabweretsa chopereka chake.

61Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka ndi beseni limodzi lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka cha zakudya; 62mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 63mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 64mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 65ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Abidani mwana wa Gideoni.

66Pa tsiku lakhumi Ahiyezeri mwana wa Amisadai, mtsogoleri wa fuko la Dani anabweretsa chopereka chake.

67Chopereka chake chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 68mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 69mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 70mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 71ndi ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahiyezeri mwana wa Amisadai.

72Pa tsiku la khumi ndi chimodzi, Pagieli mwana wa Okirani, mtsogoleri wa fuko la Aseri, anabweretsa chopereka chake.

73Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika; zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 74mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 75mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, za nsembe yopsereza; 76mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo; 77ngʼombe ziwiri zazimuna, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Pagieli mwana wa Okirani.

78Pa tsiku la khumi ndi chimodzi Ahira mwana wa Enani, mtsogoleri wa fuko la Nafutali, anabweretsa chopereka chake.

79Chopereka chakecho chinali mbale imodzi yasiliva yolemera kilogalamu imodzi ndi theka, beseni limodzi lowazira lasiliva lowazira lolemera magalamu 800, zonse monga mwa muyeso wa ku malo opatulika, zonse ziwiri zinali zodzaza ndi ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta monga chopereka chachakudya; 80mbale imodzi yagolide yolemera magalamu 110, yodzaza ndi lubani; 81mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa imodzi yayimuna ndi mwana wankhosa mmodzi wa chaka chimodzi, nsembe yopsereza; 82mbuzi yayimuna imodzi ya nsembe yopepesera machimo; 83ngʼombe zazimuna ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu, mbuzi zazimuna zisanu, ndi ana ankhosa aamuna asanu a chaka chimodzi, nsembe yachiyanjano. Ichi chinali chopereka cha Ahira mwana wa Enani.

84Zopereka za atsogoleri a Israeli zopatulira guwa lansembe pamene linadzozedwa zinali izi: mbale khumi ndi ziwiri zasiliva, mabeseni owazira asiliva khumi ndi awiri ndi mbale zagolide khumi ndi ziwiri. 85Mbale iliyonse yasiliva inkalemera kilogalamu imodzi ndi theka, ndipo beseni lililonse lowazira linkalemera magalamu 800. Pamodzi, mbale zonse zasiliva zinkalemera makilogalamu 27 monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. 86Mbale khumi ndi ziwiri zagolide zodzaza ndi lubanizo zinkalemera magalamu 110 iliyonse, monga mwa muyeso wa ku malo opatulika. Pamodzi, mbale zagolide zinkalemera kilogalamu imodzi ndi theka. 87Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yopsereza chinali motere: ngʼombe zazimuna khumi ndi ziwiri, nkhosa zazimuna khumi ndi ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi awiri a chaka chimodzi pamodzi ndi chopereka chachakudya. Mbuzi zazimuna khumi ndi ziwiri zinali za nsembe yopepesera machimo. 88Chiwerengero cha nyama zonse za nsembe yachiyanjano chinali motere: ngʼombe zothena 24, nkhosa zazimuna 60, mbuzi zazimuna 60 ndi ana ankhosa aamuna a chaka chimodzi 60. Zimenezi ndi zimene zinali zopereka zopatulira guwa lansembe litadzozedwa.

89Mose atalowa mu tenti ya msonkhano kukayankhula ndi Yehova, anamva mawu kuchokera pakati pa Akerubi awiri amene anali pamwamba pa chivundikiro cha bokosi la umboni. Ndipo anayankhula naye.

Ang Pulong Sang Dios

Numero 7:1-89

Ang mga Halad para sa Pagdedikar sang Tolda nga Simbahan

1Pagkatapos nga naplastar ni Moises ang Tolda nga Simbahan, ginwisikan niya ini sang lana kag gindedikar pati ang tanan nga kagamitan sini. Amo man ang iya ginhimo sa halaran kag sa tanan nga kagamitan sini. 2Dayon nagdala sang mga halad sa Ginoo ang mga pangulo sang Israel, nga mga pangulo sang kada tribo. Sila ang gintugyanan sa pagpangsensos. 3Nagdala sila sa presensya sang Ginoo sang anom ka karo kag dose ka baka—isa ka karo sa kada duha ka pangulo kag isa ka baka sa kada isa sa ila. Gindala nila ini sa atubangan sang Tolda nga Simbahan.

4Nagsiling ang Ginoo kay Moises, 5“Batuna ang ila halad agod gamiton para sa mga buluhaton sa Tolda nga Ginapakigkitaan.7:5 Tolda nga Ginapakigkitaan: nga amo man ang Tolda nga Simbahan. Ihatag ini sa mga kaliwat ni Levi suno sa ila tagsa ka buluhaton.”

6Gani ginbaton ni Moises ang mga karo kag ang mga baka kag ginhatag ini sa mga kaliwat ni Levi. 7Ginhatag niya ang duha ka karo kag apat ka baka sa mga kaliwat ni Gershon para sa ila buluhaton. 8Kag ginhatag niya ang apat ka karo kag walo ka baka sa mga kaliwat ni Merari para man sa ila buluhaton. Sila tanan ginapanguluhan ni Itamar nga anak ni Aaron nga pari. 9Pero wala paghatagi ni Moises sang karo ukon baka ang mga kaliwat ni Kohat kay sila ang gintugyanan sa pagtuwang sang balaan nga mga butang sang Tolda.

10Ang mga pangulo nagdala man sang ila mga halad para sa pagdedikar sang halaran sang tion nga gindedikar ini. 11Nagsiling ang Ginoo kay Moises, “Kinahanglan nga sa kada adlaw may isa ka pangulo nga magdala sang iya halad para sa pagdedikar sang halaran.”

12-83Amo ini sila ang nagdala sang ila mga halad:

Sang nahauna nga adlaw, si Nashon nga anak ni Aminadab, nga pangulo sang tribo ni Juda.

Sang ikaduha nga adlaw, si Netanel nga anak ni Zuar, nga pangulo sang tribo ni Isacar.

Sang ikatatlo nga adlaw, si Eliab nga anak ni Helon, nga pangulo sang tribo ni Zebulun.

Sang ikaapat nga adlaw, si Elizur nga anak ni Shedeur, nga pangulo sang tribo ni Reuben.

Sang ikalima nga adlaw, si Shelumiel nga anak ni Zurishadai, nga pangulo sang tribo ni Simeon.

Sang ikaanom nga adlaw, si Eliasaf nga anak ni Deuel, nga pangulo sang tribo ni Gad.

Sang ikapito nga adlaw, si Elishama nga anak ni Amihud, nga pangulo sang tribo ni Efraim.

Sang ikawalo nga adlaw, si Gamaliel nga anak ni Pedazur, nga pangulo sang tribo ni Manase.

Sang ikasiyam nga adlaw, si Abidan nga anak ni Gideoni, nga pangulo sang tribo ni Benjamin.

Sang ikanapulo nga adlaw, si Ahiezer nga anak ni Amishadai, nga pangulo sang tribo ni Dan.

Sang ikaonse nga adlaw, si Pagiel nga anak ni Ocran, nga pangulo sang tribo ni Asher.

Kag sang ikadose nga adlaw, si Ahira nga anak ni Enan, nga pangulo sang tribo ni Naftali.

Ang kada isa sa ila nagdala sang sini nga mga halad: isa ka pilak nga bandehado nga may kabug-aton nga mga isa ka kilo kag tunga, kag isa ka pilak nga yahong nga may kabug-aton nga mga 800 ka gramo suno sa kilohan sang mga pari. Ang kada isa sini ginpuno nila sang maayo nga klase sang harina nga ginmikslahan sang mantika para sa halad nga regalo. Nagdala man ang kada isa sa ila sang isa ka bulawan nga tasa7:12-83 tasa: Indi klaro ang buot silingon sang Hebreo sini. nga may kabug-aton nga mga 120 ka gramo nga puno sang insenso; isa ka torite nga baka, isa ka gulang nga karnero nga lalaki, kag isa ka bataon nga karnero nga lalaki nga isa ka tuig bilang halad nga ginasunog; isa ka lalaki nga kanding bilang halad sa pagpakatinlo; kag duha ka turo nga baka, lima ka gulang nga karnero nga lalaki, lima ka kanding nga lalaki, kag lima ka bataon nga karnero nga lalaki nga isa ka tuig bilang halad nga para sa maayo nga relasyon.

84Amo ini tanan ang mga halad sang dose ka pangulo sang mga Israelinhon para sa pagdedikar sang halaran: dose ka pilak nga bandehado, dose ka pilak nga yahong, kag dose ka bulawan nga tasa.

85Ang kada pilak nga bandehado may kabug-aton nga mga isa ka kilo kag tunga, kag ang kada pilak nga yahong may kabug-aton nga mga 800 ka gramo. Ang kabug-aton nila tanan mga 28 ka kilo suno sa kilohan sang mga pari.

86Ang dose ka bulawan nga tasa nga puno sang insenso may kabug-aton nga mga 120 ka gramo kada isa suno sa kilohan sang mga pari. Ang kabug-aton nila tanan mga 1,440 ka gramo.

87Ang mga sapat nga ginhatag para sa halad nga ginasunog: dose ka torite nga baka, dose ka gulang nga karnero nga lalaki kag dose ka bataon nga karnero nga lalaki nga isa ka tuig ang edad, upod sa sini ang mga halad nga regalo. Ang halad sa pagpakatinlo: dose ka kanding nga lalaki.

88Ang mga sapat nga halad para sa maayo nga relasyon: 24 ka turo nga baka, 60 ka gulang nga karnero nga lalaki, 60 ka kanding nga lalaki, kag 60 ka bataon nga karnero nga lalaki nga isa ka tuig ang edad.

Amo ini tanan ang mga halad sang pagdedikar sang halaran.

89Kon magsulod si Moises sa Tolda nga Ginapakigkitaan sa pagpakighambal sa Ginoo, mabatian niya ang tingog nga nagapakighambal sa iya halin sa tunga sang duha ka kerubin, sa ibabaw sang takop sang Kahon sang Kasuguan. Didto nagapakighambal ang Ginoo kay Moises.