Numeri 34 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 34:1-29

Malire a Dziko la Kanaani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:

3“ ‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere. 4Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni, 5kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.

6“ ‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.

7“ ‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori 8ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi, 9ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.

10“ ‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu. 11Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti. 12Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere.

“ ‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’ ”

13Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka, 14chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo. 15Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”

16Yehova anawuza Mose kuti, 17“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni. 18Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo. 19Mayina awo ndi awa:

Kalebe mwana wa Yefune,

wochokera ku fuko la Yuda,

20Semueli mwana wa Amihudi,

wochokera ku fuko la Simeoni;

21Elidadi mwana wa Kisiloni,

wochokera ku fuko la Benjamini;

22Buki mwana wa Yogili,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;

23Hanieli mwana wa Efodi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;

24Kemueli mwana wa Sifitani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.

25Elizafani mwana wa Parinaki,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;

26Palitieli mwana wa Azani,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,

27Ahihudi mwana wa Selomi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;

28Pedaheli mwana wa Amihudi,

mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”

29Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

La Bible du Semeur

Nombres 34:1-29

Les frontières du pays promis

1L’Eternel parla à Moïse, en disant : 2Ordonne aux Israélites : Quand vous serez entrés dans le pays de Canaan, voici quel territoire vous reviendra en possession : ses frontières sont les suivantes34.2 En approchant du moment d’entrer en Canaan, Israël reçoit des indications précises sur les limites du pays. Celles-ci ne furent atteintes qu’au temps de Salomon (voir Jos 15 ; Ez 47.13-20). : 3la limite méridionale de votre pays partira du désert de Tsîn et longera le pays d’Edom. A l’est, votre frontière sud partira de la mer Morte ; 4elle obliquera au sud vers la montée des Scorpions et passera par Tsîn pour aboutir au sud de Qadesh-Barnéa. Elle ira ensuite vers Hatsar-Addar, et passera à Atsmôn. 5De là, elle se dirigera vers le torrent d’Egypte pour aboutir à la mer. 6La mer Méditerranée34.6 En hébreu, la Grande Mer. constituera votre frontière à l’ouest. 7Au nord, vous ferez aller votre frontière de la mer Méditerranée jusqu’à la montagne de Hor34.7 Une montagne au nord du pays d’Israël, sans doute un sommet du Liban, à ne pas confondre avec la montagne de même nom où mourut Aaron (Nb 20.22 ; 33.37-41) au sud du pays.. 8De là, vous la ferez aller en direction de Lebo-Hamath34.8 Certains traduisent : l’entrée de Hamath. pour aboutir à Tsedad. 9De là, elle repartira en direction de Ziphrôn et atteindra Hatsar-Enân. Ce sera là votre frontière nord. 10A l’est, vous ferez aller votre frontière de Hatsar-Enân à Shepham, 11d’où elle descendra vers Ribla à l’est d’Aïn et suivra les pentes qui bordent la rive orientale du lac de Kinnéreth34.11 Ribla sur l’Oronte (2 R 23.33 ; 25.21) est à 80 kilomètres au sud du Hamath. Le lac mentionné (appelé ici lac de Kinnéreth) est celui de Tibériade, souvent mentionné dans les évangiles. 12jusqu’au Jourdain pour aboutir à la mer Morte. Voilà ce que sera votre pays avec les frontières qui l’entourent.

13Moïse donna les instructions suivantes aux Israélites : C’est là le territoire que vous partagerez par tirage au sort et que l’Eternel a ordonné d’attribuer aux neuf tribus et demie34.13 Voir Nb 26.52-56 ; 33.54 ; Jos 14.1-2.. 14Car la tribu de Ruben et celle de Gad ont déjà reçu leur propriété pour leur tribu, de même que la demi-tribu de Manassé. 15Ces deux tribus et demie ont reçu leur patrimoine foncier de ce côté-ci du Jourdain, en face de Jéricho, à l’est.

Les responsables du partage du pays

16L’Eternel parla encore à Moïse : 17Voici les noms des hommes qui procéderont au partage du pays entre vous : le prêtre Eléazar et Josué, fils de Noun. 18De plus, vous prendrez un chef par tribu pour répartir le pays. 19Voici les noms de ces hommes : Pour la tribu de Juda : Caleb, fils de Yephounné ; 20pour celle de Siméon : Samuel, fils d’Ammihoud ; 21pour celle de Benjamin : Elidad, fils de Kislôn ; 22pour celle de Dan : le chef Bouqqi, fils de Yogli ; 23pour les descendants de Joseph, pour la tribu de Manassé : le chef Hanniel, fils d’Ephod ; 24pour celle d’Ephraïm : le chef Qemouel, fils de Shiphtân ; 25pour celle de Zabulon ; le prince Elitsaphân, fils de Parnak ; 26pour celle d’Issacar : le prince Paltiel, fils d’Azzân ; 27pour celle d’Aser : le chef Ahihoud, fils de Shelomi ; 28pour celle de Nephtali : le chef Pedahel, fils d’Ammihoud. 29Tels sont ceux à qui l’Eternel ordonna de répartir le pays de Canaan entre les Israélites.