Numeri 33 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 33:1-56

Malo omwe Aisraeli Anayima pa Ulendo Wawo

1Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni. 2Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:

3Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona, 4pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.

5Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.

6Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.

7Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.

8Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.

9Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.

10Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.

11Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.

12Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.

13Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.

14Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.

15Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai

16Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.

17Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.

18Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.

19Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.

20Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.

21Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.

22Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.

23Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.

24Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.

25Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.

26Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.

27Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.

28Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.

29Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.

30Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.

31Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.

32Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.

33Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.

34Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.

35Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.

36Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.

37Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu. 38Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto. 39Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.

40Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.

41Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.

42Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.

43Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.

44Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.

45Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.

46Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.

47Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.

48Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko. 49Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.

50Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti, 51“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani, 52mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo. 53Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo. 54Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.

55“ ‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo. 56Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’ ”

New International Version – UK

Numbers 33:1-56

Stages in Israel’s journey

1Here are the stages in the journey of the Israelites when they came out of Egypt by divisions under the leadership of Moses and Aaron. 2At the Lord’s command Moses recorded the stages in their journey. This is their journey by stages:

3The Israelites set out from Rameses on the fifteenth day of the first month, the day after the Passover. They marched out defiantly in full view of all the Egyptians, 4who were burying all their firstborn, whom the Lord had struck down among them; for the Lord had brought judgment on their gods.

5The Israelites left Rameses and camped at Sukkoth.

6They left Sukkoth and camped at Etham, on the edge of the desert.

7They left Etham, turned back to Pi Hahiroth, to the east of Baal Zephon, and camped near Migdol.

8They left Pi Hahiroth33:8 Many manuscripts of the Masoretic Text, Samaritan Pentateuch and Vulgate; most manuscripts of the Masoretic Text left from before Hahiroth and passed through the sea into the desert, and when they had travelled for three days in the Desert of Etham, they camped at Marah.

9They left Marah and went to Elim, where there were twelve springs and seventy palm trees, and they camped there.

10They left Elim and camped by the Red Sea.33:10 Or the Sea of Reeds; also in verse 11

11They left the Red Sea and camped in the Desert of Sin.

12They left the Desert of Sin and camped at Dophkah.

13They left Dophkah and camped at Alush.

14They left Alush and camped at Rephidim, where there was no water for the people to drink.

15They left Rephidim and camped in the Desert of Sinai.

16They left the Desert of Sinai and camped at Kibroth Hattaavah.

17They left Kibroth Hattaavah and camped at Hazeroth.

18They left Hazeroth and camped at Rithmah.

19They left Rithmah and camped at Rimmon Perez.

20They left Rimmon Perez and camped at Libnah.

21They left Libnah and camped at Rissah.

22They left Rissah and camped at Kehelathah.

23They left Kehelathah and camped at Mount Shepher.

24They left Mount Shepher and camped at Haradah.

25They left Haradah and camped at Makheloth.

26They left Makheloth and camped at Tahath.

27They left Tahath and camped at Terah.

28They left Terah and camped at Mithkah.

29They left Mithkah and camped at Hashmonah.

30They left Hashmonah and camped at Moseroth.

31They left Moseroth and camped at Bene Jaakan.

32They left Bene Jaakan and camped at Hor Haggidgad.

33They left Hor Haggidgad and camped at Jotbathah.

34They left Jotbathah and camped at Abronah.

35They left Abronah and camped at Ezion Geber.

36They left Ezion Geber and camped at Kadesh, in the Desert of Zin.

37They left Kadesh and camped at Mount Hor, on the border of Edom. 38At the Lord’s command Aaron the priest went up Mount Hor, where he died on the first day of the fifth month of the fortieth year after the Israelites came out of Egypt. 39Aaron was a hundred and twenty-three years old when he died on Mount Hor.

40The Canaanite king of Arad, who lived in the Negev of Canaan, heard that the Israelites were coming.

41They left Mount Hor and camped at Zalmonah.

42They left Zalmonah and camped at Punon.

43They left Punon and camped at Oboth.

44They left Oboth and camped at Iye Abarim, on the border of Moab.

45They left Iye Abarim and camped at Dibon Gad.

46They left Dibon Gad and camped at Almon Diblathaim.

47They left Almon Diblathaim and camped in the mountains of Abarim, near Nebo.

48They left the mountains of Abarim and camped on the plains of Moab by the Jordan opposite Jericho. 49There on the plains of Moab they camped along the Jordan from Beth Jeshimoth to Abel Shittim.

50On the plains of Moab by the Jordan opposite Jericho the Lord said to Moses, 51‘Speak to the Israelites and say to them: “When you cross the Jordan into Canaan, 52drive out all the inhabitants of the land before you. Destroy all their carved images and their cast idols, and demolish all their high places. 53Take possession of the land and settle in it, for I have given you the land to possess. 54Distribute the land by lot, according to your clans. To a larger group give a larger inheritance, and to a smaller group a smaller one. Whatever falls to them by lot will be theirs. Distribute it according to your ancestral tribes.

55‘ “But if you do not drive out the inhabitants of the land, those you allow to remain will become barbs in your eyes and thorns in your sides. They will give you trouble in the land where you will live. 56And then I will do to you what I plan to do to them.” ’