Numeri 33 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 33:1-56

Malo omwe Aisraeli Anayima pa Ulendo Wawo

1Malo otsatirawa ndi omwe Aisraeli anayima pa maulendo awo atatuluka mʼdziko la Igupto mʼmagulu awo motsogozedwa ndi Mose ndi Aaroni. 2Mose analemba malo amene anayambira maulendo awo molamulidwa ndi Yehova. Maulendo awo ndi malo omwe anayambira ndi awa:

3Aisraeli ananyamuka kuchokera ku Ramesesi pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, itangotha Paska. Iwo anatuluka nayenda molimba mtima Aigupto onse akuona, 4pamene ankayika maliro a ana awo oyamba kubadwa, omwe Yehova anawakantha pakati pawo chifukwa Yehova anaweruza milungu yawo.

5Aisraeli atachoka ku Ramesesi, anamanga misasa yawo ku Sukoti.

6Atachoka ku Sukoti anakamanga misasa yawo ku Etamu, mʼmbali mwa chipululu.

7Ndipo atachoka ku Etamu, anabwerera ku Pihahiroti, kummawa kwa Baala-Zefoni, ndipo anamanga misasa yawo pafupi ndi Migidoli.

8Atachoka ku Pihahiroti anadutsa mʼkati mwa nyanja kupita ku chipululu ndipo atayenda masiku atatu mʼchipululu cha Etamu, anamanga misasa yawo ku Mara.

9Atachoka ku Mara anafika ku Elimu, kumene kunali akasupe a madzi khumi ndi awiri ndi mitengo ya migwalangwa 70 ndipo anamanga misasa yawo kumeneko.

10Atachoka ku Elimu anakamanga misasa yawo mʼmbali mwa Nyanja Yofiira.

11Atachoka ku Nyanja Yofiira anakamanga misasa yawo mʼchipululu cha Sini.

12Atachoka ku chipululu cha Sini anakamanga ku Dofika.

13Atachoka ku Dofika anakamanga misasa yawo ku Alusi.

14Atachoka ku Alusi anakamanga misasa yawo ku Refidimu, kumene kunalibe madzi woti anthu ndi kumwa.

15Atachoka ku Refidimu anakamanga ku chipululu cha Sinai

16Atachoka ku chipululu cha Sinai anakamanga misasa yawo ku Kiburoti-Hataava.

17Atachoka ku Kiburoti-Hataava anakamanga misasa yawo ku Heziroti.

18Atachoka ku Heziroti anakamanga ku Ritima.

19Atachoka ku Ritima anakamanga ku Rimoni-Perezi.

20Atachoka ku Rimoni-Perezi anakamanga ku Libina.

21Atachoka ku Libina anakamanga ku Risa.

22Atachoka ku Risa anakamanga ku Kehelata.

23Atachoka ku Kehelata anakamanga ku phiri la Seferi.

24Atachoka ku phiri la Seferi anakamanga ku Harada.

25Atachoka ku Harada anakamanga ku Mekheloti.

26Atachoka ku Mekheloti anakamanga ku Tahati.

27Atachoka ku Tahati anakamanga ku Tera.

28Atachoka ku Tera anakamanga ku Mitika.

29Atachoka ku Mitika anakamanga ku Hasimona.

30Atachoka ku Hasimona anakamanga ku Moseroti.

31Atachoka ku Moseroti anakamanga ku Beni Yaakani.

32Atachoka ku Beni Yaakani anakamanga ku Hori-Hagidigadi.

33Atachoka ku Hori-Hagidigadi anakamanga ku Yotibata.

34Atachoka ku Yotibata anakamanga ku Abirona.

35Atachoka ku Abirona anakamanga ku Ezioni-Geberi.

36Atachoka ku Ezioni-Geberi anakamanga ku Kadesi, mʼchipululu cha Zini chimene ndi Kadesi.

37Anachoka ku Kadesi ndi kukamanga ku phiri la Hori, mʼmalire mwa dziko la Edomu. 38Molamulidwa ndi Yehova, wansembe Aaroni anakwera ku phiri la Hori kumene anakamwalirira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu, mʼchaka cha makumi anayi, Aisraeli atatuluka mʼdziko la Igupto. 39Aaroni anamwalira pa phiri la Hori ali ndi zaka 123.

40Mfumu ya Akanaani ya ku Aradi yomwe inkakhala ku Negevi kummwera kwa Kanaani, inamva kuti Aisraeli akubwera.

41Atachoka ku phiri la Hori anakamanga ku Zalimoni.

42Atachoka ku Zalimoni anakamanga ku Punoni.

43Atachoka ku Punoni anakamanga ku Oboti.

44Atachoka ku Oboti anakamanga ku Iye-Abarimu.

45Atachoka ku Iye-Abarimu anakamanga ku Diboni Gadi.

46Atachoka ku Diboni Gadi anakamanga ku Alimoni-Dibulataimu.

47Atachoka ku Alimoni-Dibulataimu anakamanga mʼmapiri a Abarimu, pafupi ndi Nebo.

48Atachoka ku mapiri a Abarimu anakamanga ku zigwa za Mowabu mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi Yeriko. 49Ali ku zigwa za Mowabu anamanga mʼmbali mwa Yorodani kuchokera ku Beti-Yesimoti mpaka ku Abeli-Sitimu.

50Pa zigwa za Mowabu, mʼmbali mwa Yorodani moyangʼanana ndi ku Yeriko, Yehova anawuza Mose kuti, 51“Nena kwa Aisraeli kuti, ‘Pamene muwoloka Yorodani kulowa mʼdziko la Kanaani, 52mukathamangitse nzika zonse za mʼdzikomo pamaso panu. Mukawononge mafano awo onse a miyala ndi osula ndi malo awo achipembedzo. 53Mukalande dzikolo ndi kukhalamo chifukwa ndakupatsani dziko limenelo kuti mukhalemo. 54Mukagawane dzikolo pochita maere monga mwa mafuko anu. Kwa omwe ali ambiri, cholowa chambiri, ndipo amene ali ocheperapo, chocheperanso. Chilichonse chimene chidzawagwere iwo mwa maere chidzakhala chawo. Mukaligawane monga mwa mafuko a makolo anu.

55“ ‘Koma ngati simukathamangitsa nzika zimene zili mʼdzikomo, amene mukawalole kukhalamo adzakhala ngati zisonga mʼmaso mwanu ndi ngati minga mʼmbali mwanu. Adzakubweretserani mavuto mʼdziko limene mudzakhalemolo. 56Ndipo pamenepo ndidzachitira inu zomwe ndinaganiza kuwachitira iwowo.’ ”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 33:1-56

從埃及到約旦河

1以下是以色列人在摩西亞倫的領導下離開埃及列隊行軍的路線。 2摩西遵照耶和華的吩咐記錄啟行的地點,以下是他們停留過的地方。

3一月十五日,即逾越節的第二天,埃及人眼睜睜地看著以色列人昂首挺胸地離開了蘭塞4當時埃及人正埋葬他們的長子,耶和華擊殺了他們的長子,並藉此懲罰了他們的眾神明。 5以色列人從蘭塞啟行,至疏割紮營; 6疏割啟行,至曠野邊界的以倘紮營; 7以倘啟行,又折回巴力·洗分對面的比哈·希錄,在密奪附近紮營; 8比哈·希錄啟行,經過紅海到書珥曠野,在伊坦曠野走了三天,至瑪拉紮營; 9瑪拉啟行,至以琳紮營,那裡有十二股水泉和七十棵棕樹; 10以琳啟行,至紅海岸邊紮營; 11從紅海啟行,至曠野紮營; 12曠野啟行,至脫加紮營; 13脫加啟行,至亞錄紮營; 14亞錄啟行,至利非訂紮營,在那裡民眾沒有水喝; 15利非訂啟行,至西奈曠野紮營; 16西奈曠野啟行,至基博羅·哈他瓦紮營; 17基博羅·哈他瓦啟行,至哈洗錄紮營; 18哈洗錄啟行,至利提瑪紮營; 19利提瑪啟行,至臨門·帕烈紮營; 20臨門·帕烈啟行,至立拿紮營; 21立拿啟行,至勒撒紮營; 22勒撒啟行,至基希拉他紮營; 23基希拉他啟行,至沙斐山紮營; 24沙斐山啟行,至哈拉大紮營; 25哈拉大啟行,至瑪吉希錄紮營; 26瑪吉希錄啟行,至他哈紮營; 27他哈啟行,至他拉紮營; 28他拉啟行,至密加紮營; 29密加啟行,至哈摩拿紮營; 30哈摩拿啟行,至摩西錄紮營; 31摩西錄啟行,至比尼·亞干紮營; 32比尼·亞干啟行,至曷·哈吉甲紮營; 33曷·哈吉甲啟行,至約巴他紮營; 34約巴他啟行,至阿博拿紮營; 35阿博拿啟行,至以旬·迦別紮營; 36以旬·迦別啟行,至曠野的加低斯紮營; 37加低斯啟行,至以東邊界的何珥山紮營。

38以色列人離開埃及後的第四十年五月一日,亞倫祭司遵照耶和華的吩咐上了何珥山,並在那裡離世, 39享年一百二十三歲。

40在南地的迦南亞拉得王得知了以色列人要來的消息。

41以色列人從何珥山啟行,至撒摩拿紮營; 42撒摩拿啟行,至普嫩紮營; 43普嫩啟行,至阿伯紮營; 44阿伯啟行,至摩押邊境的以耶·亞巴琳紮營; 45以耶·亞巴琳啟行,至底本·迦得紮營; 46底本·迦得啟行,至亞門·低比拉太音紮營; 47亞門·低比拉太音啟行,至尼波對面的亞巴琳山紮營; 48亞巴琳山啟行,至耶利哥對面、約旦河邊的摩押平原紮營。 49他們沿著約旦河在摩押平原紮營,營地從伯·耶施末一直延伸到亞伯·什亭

50耶和華在耶利哥對面、約旦河邊的摩押平原對摩西說: 51「你告訴以色列人,『你們過約旦河進了迦南以後, 52一定要趕走當地的居民,毀掉他們一切的石像和鑄像,拆毀他們所有的邱壇。 53你們要佔領那片土地,住在那裡,因為我已經把那裡賜給你們作產業了。 54你們要按宗族家系抽籤分配土地,人口多的多分,人口少的少分,抽到哪塊地就得哪塊地。 55如果你們不趕走那裡的居民,留下來的人必成為你們眼裡的刺和肋旁的荊棘,在你們所居之地攪擾你們, 56我也會用預備對付他們的方法來對付你們。』」