Numeri 31 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 31:1-54

Aisraeli Agonjetsa Amidiyani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”

3Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova. 4Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.” 5Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli. 6Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.

7Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense. 8Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori. 9Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense. 10Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse. 11Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe. 12Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.

13Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa. 14Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.

15Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?” 16Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova. 17Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna, 18koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.

19“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu. 20Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”

21Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili: 22Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu 23ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo. 24Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”

Kugawana Zolanda ku Nkhondo

25Yehova anawuza Mose kuti, 26“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo. 27Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse. 28Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa. 29Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova. 30Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.” 31Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.

32Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000, 33Ngʼombe 72,000, 34abulu 61,000, 35ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.

36Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali:

nkhosa 337,500, 37mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;

38ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;

39abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;

40anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.

41Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.

42Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja. 43Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500, 44ngʼombe 36,000, 45abulu 30,500, 46anthu 16,000. 47Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.

48Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose, 49iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa. 50Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”

51Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula. 52Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200. 53Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo. 54Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

民數記 31:1-54

攻打米甸人

1耶和華對摩西說: 2「你要為以色列人向米甸人報仇,之後你將歸到祖先那裡。」 3於是,摩西對民眾說:「你們男子要拿起兵器去攻打米甸,為耶和華報仇。 4以色列的每個支派要派一千人出戰。」 5於是,他們從以色列每個支派選出一千人,武裝了一萬二千軍兵。 6每個支派選出的一千軍兵由摩西派遣出戰,以利亞撒祭司的兒子非尼哈拿著聖所的器具和號角隨行。 7他們照耶和華對摩西的吩咐去攻打米甸人,殺死了米甸的所有男子, 8包括以未利金蘇珥戶珥利巴五個王,還殺了比珥的兒子巴蘭9以色列人擄獲了米甸的婦女、孩子、牛羊和財物, 10將他們的城邑營寨付之一炬, 11帶走了擄掠的人畜等戰利品。 12他們來到耶利哥對面、約旦河邊的摩押平原,把戰利品交給摩西以利亞撒祭司和以色列全體會眾。

13摩西以利亞撒祭司以及所有民眾的首領都到營外迎接他們。 14摩西對回來的千夫長和百夫長發怒, 15說:「你們為什麼讓這些婦女活著? 16就是她們聽了巴蘭的指使在毗珥引誘以色列人背叛耶和華,以致瘟疫降在耶和華的會眾身上。 17現在,你們要殺掉所有的男孩以及與男人發生過關係的女子, 18但可以留下那些處女。 19你們凡殺了人和碰過死人的都要在營外待七天。在第三天和第七天,你們要潔淨自己及擄來的人, 20也要潔淨自己所有的衣服、皮具、山羊毛織的物品和木器。」 21以利亞撒祭司對打仗回來的軍兵說:「以下是耶和華藉摩西頒佈的律例。 22金、銀、銅、鐵、錫、鉛, 23凡耐火之物都要用火來潔淨,還要用除穢水加以潔淨;不耐火之物要用水來潔淨。 24第七天,你們洗完衣服後就潔淨了,可以回營。」

25耶和華對摩西說: 26「你和以利亞撒祭司以及會眾的各族長要統計俘虜和牲畜的數目, 27然後把這些戰利品分成兩份,一份給出征的戰士,一份給會眾。 28要從戰士分得的俘虜、牛、驢和羊群中抽出五百分之一獻給耶和華, 29要把那五百分之一交給以利亞撒祭司獻給耶和華作舉祭。 30要從會眾分得的俘虜和牛、驢、羊等牲畜中抽出五十分之一交給在我聖幕司職的利未人。」 31摩西以利亞撒祭司遵命而行。

32戰士擄獲的戰利品中有六十七萬五千隻羊, 33七萬二千頭牛, 34六萬一千頭驢, 35三萬二千名處女。 36戰士分得的戰利品有三十三萬七千五百隻羊, 37其中六百七十五隻獻給耶和華; 38三萬六千頭牛,其中七十二頭獻給耶和華; 39三萬零五百頭驢,其中六十一頭獻給耶和華; 40一萬六千名處女,其中三十二人獻給耶和華。 41摩西照耶和華的吩咐,把獻給耶和華的舉祭交給以利亞撒祭司。

42以色列會眾分得的那一半戰利品,即摩西從出征之人的戰利品中分出來給他們的, 43有三十三萬七千五百隻羊、 44三萬六千頭牛、 45三萬零五百頭驢、 46一萬六千名處女。 47摩西照耶和華的吩咐,從中抽出五十分之一交給在聖幕裡司職的利未人。

48統領軍隊的千夫長和百夫長來見摩西49說:「僕人們統計了手下出征的戰士,未失一兵一卒。 50現在我們把各自擄獲的臂環、鐲子、圖章戒指、耳環、項鏈等金器都帶來獻給耶和華,作為我們生命的贖價。」 51摩西以利亞撒祭司收了他們所獻的各種金製物品。 52千夫長和百夫長獻給耶和華作舉祭的金子約二百公斤。 53戰士則保留了自己擄獲的財物。 54摩西以利亞撒祭司就把千夫長和百夫長獻的金子帶進會幕,在耶和華面前作以色列人的紀念。