Numeri 29 – CCL & APSD-CEB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 29:1-40

Chikondwerero cha Malipenga

1“ ‘Pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Ili ndi tsiku limene muziliza malipenga. 2Muzipereka mwana wangʼombe wamwamuna mmodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi wopanda chilema monga nsembe zopsereza, fungo lokoma kwa Yehova. 3Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzipereka chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa yayimuna iliyonse muzipereka makilogalamu awiri. 4Pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja muzipereka kilogalamu imodzi. 5Muziperekanso mbuzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu. 6Izi ndi zowonjezera pa nsembe zopsereza za mwezi ndi mwezi komanso za tsiku ndi tsiku pamodzi ndi zopereka za chakudya ndi zopereka za chakumwa potsata malamulo ake. Izi ndi zopereka zotentha pa moto, zoperekedwa kwa Yehova, fungo lokoma.

Tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo

7“ ‘Pa tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiriwu, muzichita msonkhano wopatulika. Muzisala zakudya ndipo musamagwire ntchito. 8Muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza, yotulutsa fungo lokoma lokondweretsa Yehovayo; ngʼombe yayimuna imodzi, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi. Zimenezi zizikhala zopanda chilema. 9Pa ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri; 10kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiriwo. 11Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna kuti izikhala nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe yopepesera machimo ya pa tsiku la mwambo ija, kuwonjezanso pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija, pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi cha chakumwa.

Chikondwerero cha Misasa

12“ ‘Pa tsiku la mwezi wachisanu ndi chiwiri, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. Muzichita madyerero a Yehova masiku asanu ndi awiri. 13Muzipereka nsembe yotentha pa moto, kuti izikhala fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu, nkhosa zazimuna ziwiri, ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 14Pa mwana wangʼombe aliyense mwa ana angʼombe aamuna khumi ndi atatu aja, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. Pa nkhosa iliyonse mwa nkhosa ziwiri zija, mukonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri. 15Pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa aamuna khumi ndi anayiwo, muzipereka chakudya cha kilogalamu imodzi. 16Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhale nsembe yopepesera machimo, kuwonjezera pa nsembe zopsereza za tsiku ndi tsiku zija pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

17“ ‘Pa tsiku lachiwiri muzipereka ana angʼombe aamuna khumi ndi awiri aja, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi aja, zonse zopanda chilema. 18Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 19Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

20“ ‘Pa tsiku lachitatu muzipereka ngʼombe zazimuna khumi ndi imodzi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 21Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka zopereka za chakudya ndi za chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 22Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

23“ ‘Pa tsiku lachinayi muzipereka ngʼombe zazimuna khumi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 24Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 25Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

26“ ‘Pa tsiku lachisanu muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zinayi, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 27Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 28Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

29“ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chimodzi muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi zitatu, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa aamuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 30Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 31Muziperekenso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

32“ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzipereka ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna ziwiri ndi ana ankhosa amuna khumi ndi anayi a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 33Pamodzi ndi ngʼombe zazimuna, nkhosa zazimuna ndi ana ankhosa, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 34Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

35“ ‘Pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzichita msonkhano ndipo musamagwire ntchito iliyonse. 36Muzipereka chopereka chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Yehova, nsembe yopsereza ya ngʼombe imodzi yayimuna, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa amuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, zonse zopanda chilema. 37Pamodzi ndi ngʼombe yayimunayo, nkhosa yayimunayo ndi ana ankhosawo, muzipereka chopereka cha chakudya ndi chakumwa molingana ndi chiwerengero cha nyamazo. 38Muziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ya nsembe yopepesera machimo, powonjezera pa nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pamodzi ndi chopereka chake cha chakudya ndi chakumwa.

39“ ‘Kuwonjezera pa zopereka zimene munalumbirira ndi pa zopereka zanu zaufulu, muzipereka zimenezi kwa Yehova pa masiku osankhika a chikondwerero chanu. Nsembe zanu zachakumwa ndi nsembe zanu zachiyanjano.’ ”

40Mose anawuza Aisraeli zonse zimene Yehova anamulamulira.

Ang Pulong Sa Dios

Numero 29:1-40

Ang mga Halad sa Pista sa Pagpatingog sa mga Trumpeta

(Lev. 23:23-25)

1“Sa unang adlaw sa ikapitong bulan, magtigom kamo aron sa pagsimba sa Ginoo ug ayaw kamo pagtrabaho. Nianang adlawa patingogon ninyo ang mga trumpeta. 2Unya paghalad kamo ug halad nga sinunog diin ang kahumot niini makapalipay sa Ginoo: usa ka toriyong baka, usa ka hamtong nga laking karnero, ug pito ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad, nga walay depekto. 3Lakipan kini sa halad sa pagpasidungog nga maayong klase sa harina nga sinagolan ug mantika—unom ka kilo sa matag toriyong baka, upat ka kilo sa hamtong nga laking karnero, 4ug duha ka kilo sa matag batan-ong karnero. 5Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo aron mahinloan kamo gikan sa inyong mga sala. 6Ihalad ninyo kini dugang sa binulan ug inadlaw-adlaw nga mga halad nga sinunog uban sa mga halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon. Mga halad kini pinaagi sa kalayo, ug ang kahumot niini makapalipay sa Ginoo.

Ang mga Halad sa Adlaw sa Paglukat

(Lev. 23:26-32)

7“Sa ikanapulo nga adlaw niining ikapitong bulan, magtigom kamo aron sa pagsimba sa Ginoo. Kinahanglan nga magpuasa kamo ug dili gayod magtrabaho. 8Unya maghalad kamo ug mga halad nga sinunog diin ang kahumot niini makapalipay sa Ginoo: usa ka toriyong baka, usa ka hamtong nga laking karnero, ug pito ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad. Kining tanan kinahanglan walay depekto. 9Lakipan kini sa halad sa pagpasidungog nga maayong klase sa harina nga sinagolan ug mantika—unom ka kilo sa matag toriyong baka, upat ka kilo sa hamtong nga laking karnero, 10ug duha ka kilo sa matag batan-ong karnero. 11Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa naandang halad sa paghinlo aron maluwas kamo sa inyong mga sala ug sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon.

Ang mga Halad sa Pista sa Pagpatindog sa mga Payag

(Lev. 23:33-43)

12“Sa ika-15 nga adlaw sa mao gihapong bulan, magtigom na usab kamo aron sa pagsimba sa Ginoo ug ayaw gayod kamo pagtrabaho nianang adlawa. Saulogon ninyo kini nga pista alang sa Ginoo sulod sa pito ka adlaw. 13Paghalad kamo ug mga halad nga sinunog diin ang kahumot niini makapalipay sa Ginoo Sa nahaunang adlaw mao kini ang inyong ihalad: 13 ka toriyong baka, 2 ka hamtong nga laking karnero, ug 14 ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad. Kining tanan kinahanglan walay depekto. 14Lakipan kini sa halad sa pagpasidungog nga maayong klase sa harina nga sinagolan ug mantika—unom ka kilo sa matag toriyong baka, upat ka kilo sa matag hamtong nga laking karnero, 15ug duha ka kilo sa matag batan-ong karnero. 16Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon.

17“Sa ikaduhang adlaw, mao kini ang inyong ihalad: 12 ka toriyong baka, 2 ka hamtong nga laking karnero, ug 14 ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad, nga walay depekto. 18Ang matag usa niini, lakipan ninyo sa ensakto nga gidaghanon sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon. 19Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon.

20“Sa ikatulong adlaw, mao kini ang inyong ihalad: 11 ka toriyong baka, 2 ka hamtong nga laking karnero, ug 14 ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad, nga walay depekto. 21Ang matag usa niini, lakipan ninyo sa ensakto nga gidaghanon sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon. 22Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon.

23“Sa ikaupat nga adlaw, mao kini ang inyong ihalad: napulo ka toriyong baka, 2 ka hamtong nga laking karnero, ug 14 ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad, nga walay depekto. 24Ang matag usa niini, lakipan ninyo sa ensakto nga gidaghanon sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon. 25Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon.

26“Sa ikalimang adlaw, mao kini ang inyong ihalad: 9 ka toriyong baka, 2 ka hamtong nga laking karnero, ug 14 ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad, nga walay depekto. 27Ang matag usa niini, lakipan ninyo sa ensakto nga gidaghanon sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon. 28Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon.

29“Sa ikaunom nga adlaw, mao kini ang inyong ihalad: 8 ka toriyong baka, 2 ka hamtong nga laking karnero, ug 14 ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad, nga walay depekto. 30Ang matag usa niini, lakipan ninyo sa ensakto nga gidaghanon sa halad sa pagpasidungog ug sa halad nga ilimnon. 31Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon.

32“Sa ikapito nga adlaw mao kini ang inyong ihalad: 7 ka toriyong baka, 2 ka hamtong nga laking karnero, ug 14 ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad, nga walay depekto. 33Ang matag usa niini, lakipan ninyo sa ensakto nga gidaghanon sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon. 34Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon.

35“Sa ikawalong adlaw, magtigom kamo aron sa pagsimba sa Ginoo ug ayaw gayod kamo pagtrabaho nianang adlawa. 36Paghalad kamo ug halad nga sinunog diin ang kahumot niini makapalipay sa Ginoo: usa ka toriyong baka, usa ka hamtong nga laking karnero, ug pito ka laking karnero nga tagsa ka tuig ang edad, nga walay depekto. 37Ang matag usa niini, lakipan ninyo sa ensakto nga gidaghanon sa halad sa pagpasidungog ug sa mga halad nga ilimnon. 38Maghalad usab kamo ug usa ka laking kanding isip halad sa paghinlo, dugang sa inadlaw-adlaw nga halad nga sinunog uban sa halad sa pagpasidungog ug sa halad nga ilimnon.

39“Dugang sa inyong mga halad sa pagtuman sa inyong panaad ug mga halad nga kinabubut-on, maghalad usab kamo sa Ginoo niining mga halad, sumala sa gitakda ninyo nga mga pista: mga halad nga sinunog, mga halad sa pagpasidungog, mga halad nga ilimnon, ug mga halad alang sa maayong relasyon.”

40Gisulti kining tanan ni Moises ngadto sa mga Israelinhon sumala sa gisugo kaniya sa Ginoo.