Numeri 28 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 28:1-31

Zopereka za Tsiku ndi Tsiku

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’ 3Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema. 4Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo. 5Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi. 6Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova. 7Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova. 8Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’ ”

Zopereka za pa Sabata

9“ ‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta. 10Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’ ”

Zopereka za pa Mwezi

11“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema. 12Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; 13ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova. 14Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka. 15Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.

Paska

16“ ‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova. 17Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri. 18Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse. 19Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema. 20Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse. 21Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja. 22Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu. 23Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa. 24Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa. 25Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.

Madyerero a Masabata

26“ ‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. 27Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova. 28Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri. 29Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi. 30Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu. 31Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

New International Version – UK

Numbers 28:1-31

Daily offerings

1The Lord said to Moses, 2‘Give this command to the Israelites and say to them: “Make sure that you present to me at the appointed time my food offerings, as an aroma pleasing to me.” 3Say to them: “This is the food offering you are to present to the Lord: two lambs a year old without defect, as a regular burnt offering each day. 4Offer one lamb in the morning and the other at twilight, 5together with a grain offering of a tenth of an ephah28:5 That is, probably about 1.6 kilograms; also in verses 13, 21 and 29 of the finest flour mixed with a quarter of a hin28:5 That is, about 1 litre; also in verses 7 and 14 of oil from pressed olives. 6This is the regular burnt offering instituted at Mount Sinai as a pleasing aroma, a food offering presented to the Lord. 7The accompanying drink offering is to be a quarter of a hin of fermented drink with each lamb. Pour out the drink offering to the Lord at the sanctuary. 8Offer the second lamb at twilight, along with the same kind of grain offering and drink offering that you offer in the morning. This is a food offering, an aroma pleasing to the Lord.

Sabbath offerings

9‘ “On the Sabbath day, make an offering of two lambs a year old without defect, together with its drink offering and a grain offering of one-fifth of an ephah28:9 That is, probably about 3.2 kilograms; also in verses 12, 20 and 28 of the finest flour mixed with olive oil. 10This is the burnt offering for every Sabbath, in addition to the regular burnt offering and its drink offering.

Monthly offerings

11‘ “On the first of every month, present to the Lord a burnt offering of two young bulls, one ram and seven male lambs a year old, all without defect. 12With each bull there is to be a grain offering of three-tenths of an ephah28:12 That is, probably about 5 kilograms; also in verses 20 and 28 of the finest flour mixed with oil; with the ram, a grain offering of one-fifth of an ephah of the finest flour mixed with oil; 13and with each lamb, a grain offering of a tenth of an ephah of the finest flour mixed with oil. This is for a burnt offering, a pleasing aroma, a food offering presented to the Lord. 14With each bull there is to be a drink offering of half a hin28:14 That is, about 1.9 litres of wine; with the ram, a third of a hin28:14 That is, about 1.3 litres; and with each lamb, a quarter of a hin. This is the monthly burnt offering to be made at each new moon during the year. 15Besides the regular burnt offering with its drink offering, one male goat is to be presented to the Lord as a sin offering.28:15 Or purification offering; also in verse 22

The Passover

16‘ “On the fourteenth day of the first month the Lord’s Passover is to be held. 17On the fifteenth day of this month there is to be a festival; for seven days eat bread made without yeast. 18On the first day hold a sacred assembly and do not do any of your ordinary work. 19Present to the Lord a food offering consisting of a burnt offering of two young bulls, one ram and seven male lambs a year old, all without defect. 20With each bull offer a grain offering of three-tenths of an ephah of the finest flour mixed with oil; with the ram, one-fifth; 21and with each of the seven lambs, one-tenth. 22Include one male goat as a sin offering to make atonement for you. 23Offer these in addition to the regular morning burnt offering. 24In this way present the food offering every day for seven days as an aroma pleasing to the Lord; it is to be offered in addition to the regular burnt offering and its drink offering. 25On the seventh day hold a sacred assembly and do not do any ordinary work.

The Festival of Weeks

26‘ “On the day of firstfruits, when you present to the Lord an offering of new grain during the Festival of Weeks, hold a sacred assembly and do not do any of your ordinary work. 27Present a burnt offering of two young bulls, one ram and seven male lambs a year old as an aroma pleasing to the Lord. 28With each bull there is to be a grain offering of three-tenths of an ephah of the finest flour mixed with oil; with the ram, one-fifth; 29and with each of the seven lambs, one-tenth. 30Include one male goat to make atonement for you. 31Offer these together with their drink offerings, in addition to the regular burnt offering and its grain offering. Be sure the animals are without defect.