Numeri 25 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 25:1-18

Aisraeli Achita Chigololo

1Aisraeli akukhala ku Sitimu, anayamba kuchita chigololo ndi akazi a ku Mowabu, 2amene ankawayitana ku nsembe za milungu yawo. Anthuwo anadya chakudya chopereka kwa milungu ndi kupembedza milunguyo. 3Motero Aisraeli anapembedza nawo Baala-Peori ndipo Yehova anawapsera mtima kwambiri.

4Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Tenga atsogoleri onse a anthu awa, uwaphe poyera, pamaso pa Yehova kuti mkwiyo waukulu wa Yehova uchoke pa Israeli.”

5Choncho Mose anawuza oweruza a Israeli kuti, “Aliyense wa inu ayenera kupha anthu ake amene anapembedza nawo Baala-Peori.”

6Kenaka mwamuna wina wa ku Israeli anabweretsa ku banja lake mkazi wa Chimidiyani pamaso pa Mose ndi anthu onse a Israeli pamene ankalira pa khomo la tenti ya msonkhano. 7Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni ataona izi, anachoka pa msonkhanowo, natenga mkondo mʼdzanja lake. 8Ndipo anatsatira Mwisraeliyu mpaka mʼtenti yake. Anasolola mkondowo ndi kubaya awiriwo kupyola Mwisraeliyo mpaka mʼthupi la mkaziyo. Pamenepo mliri unaleka pakati pa Aisraeli. 9Pa mliriwo, anthu okwana 24,000 anafa.

10Yehova anawuza Mose kuti, 11“Finehasi mwana wa Eliezara, mwana wa wansembe Aaroni wabweza mkwiyo wanga pa Aisraeli chifukwa sanalole kuti wina aliyense apembedze mulungu wina koma Ine ndekha. Nʼchifukwa chake sindinawawononge mu mkwiyo wanga. 12Tsono muwuze kuti ndikhazikitsa pangano langa la mtendere ndi iye. 13Ndikupangana naye pangano la unsembe wosatha, iyeyo pamodzi ndi zidzukulu zake zonse, chifukwa sanalole kuti anthu awukire Ine Mulungu, ndipo anachita ntchito yopepesera machimo Aisraeli.”

14Dzina la Mwisraeli yemwe anaphedwa ndi mkazi wa Chimidiyani anali Zimuri mwana wa Salu, mtsogoleri wa banja la Simeoni. 15Ndipo dzina la mkazi wa Chimidiyani, yemwe anaphedwayo, linali Kozibi mwana wa Zuri, mtsogoleri wa fuko la ku Midiyaniko.

16Yehova anawuza Mose kuti, 17“Amidiyani ndi adani anu ndipo uwaphe, 18chifukwa ankakuonani inu ngati adani awo pamene anakupusitsani pa nkhani ya ku Peori, ndiponso za mlongo wawo Kozibi, mwana wamkazi wa mtsogoleri wa Amidiyani, mkazi yemwe anaphedwa pamene mliri unabwera chifukwa cha zimene zinachitika ku Peori.”

La Bible du Semeur

Nombres 25:1-19

L’idolâtrie dans les steppes de Moab

1Israël s’établit à Shittim. Là, le peuple commença à se livrer à la débauche avec des filles de Moab25.1 Shittim se trouvait à l’est du Jourdain, en face de Jéricho. Les Moabites, les plus proches voisins d’Israël alors, voulaient leur ruine. C’est pourquoi ils s’étaient alliés aux Madianites (22.4). Selon 31.8, 16 (voir Ap 2.14), c’est sur le conseil de Balaam que les filles moabites invitèrent les jeunes gens israélites à participer à leur culte païen comportant des rites de fertilité, avec leur débauche sexuelle. 2qui les invitèrent aux sacrifices offerts à leurs dieux. Les Israélites participèrent à leurs repas sacrés et se prosternèrent devant leurs dieux. 3Ils adoptèrent ainsi le culte du dieu Baal de Peor25.3 Baal: voir 22.41. Baal de Peor: voir Dt 4.3 ; Os 9.10 ; Ps 106.28., et l’Eternel se mit en colère contre eux. 4L’Eternel dit à Moïse : Prends avec toi tous les chefs du peuple et fais-les pendre en ma présence face au soleil, afin que l’ardeur de ma colère se détourne d’Israël.

5Moïse ordonna aux juges d’Israël25.5 Institués selon Ex 18.19-26. : Que chacun de vous exécute ceux de ses gens qui se sont adonnés au culte du Baal de Peor.

6A ce moment survint un Israélite amenant vers ses compatriotes une fille madianite, sous les yeux de Moïse et devant toute la communauté des Israélites qui pleuraient à l’entrée de la tente de la Rencontre. 7Voyant cela, Phinéas, fils d’Eléazar et petit-fils du prêtre Aaron, se leva du milieu de la communauté, saisit une lance 8et suivit cet Israélite jusque dans la partie arrière de sa tente. Là, il transperça tous les deux, l’homme et la femme, d’un coup en plein ventre. Et le fléau qui sévissait parmi les Israélites cessa. 9Mais il avait déjà fait vingt-quatre mille victimes25.9 Allusion à ce récit dans 1 Co 10.8..

10Alors l’Eternel parla à Moïse en ces termes : 11Phinéas, fils d’Eléazar, petit-fils du prêtre Aaron, a détourné ma colère des Israélites, car il a pris vivement à cœur mes intérêts. Aussi, je n’ai pas exterminé les Israélites dans ma colère de les voir bafouer mon amour pour eux. 12C’est pourquoi, déclare-lui que je conclus avec lui une alliance de paix. 13Cette alliance lui garantira, à lui et à ses descendants, le sacerdoce à perpétuité, parce qu’il a pris vivement à cœur les intérêts de son Dieu, et qu’il a accompli un acte expiatoire pour les Israélites.

14L’Israélite qui avait été tué avec la Madianite s’appelait Zimri, il était fils de Salou et chef d’un groupe familial de la tribu de Siméon. 15La Madianite se nommait Kozbi, c’était une fille de Tsour, un chef de plusieurs familles d’un groupe familial des Madianites.

16L’Eternel parla à Moïse, en ces termes : 17Attaquez les Madianites et battez-les, 18car ils sont devenus vos ennemis en usant de ruse contre vous dans l’affaire de Peor et au moyen de Kozbi, fille d’un de leurs chefs, qui fut mise à mort lors du fléau survenu à cause du Baal de Peor.

Préparatifs en vue de l’entrée dans le pays promis

Le nouveau recensement

Le recensement des douze tribus

19Après ce fléau,