Numeri 14 – CCL & NEN

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 14:1-45

Anthu Awukira

1Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri. 2Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno! 3Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?” 4Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”

5Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo. 6Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo 7ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi. 8Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife, 9koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”

10Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano. 11Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo? 12Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”

13Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo. 14Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku. 15Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati, 16‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’

17“Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti, 18‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’ 19Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”

20Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera. 21Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova, 22palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi, 23palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo. 24Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo. 25Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”

26Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti, 27“Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa. 28Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena: 29Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane. 30Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni. 31Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana. 32Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno. 33Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno. 34Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’ 35Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”

36Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo. 37Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova. 38Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.

39Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri. 40Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”

41Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka! 42Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu 43chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”

44Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa. 45Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.

Kiswahili Contemporary Version (Neno: Bibilia Takatifu)

Hesabu 14:1-45

Watu Wanaasi

114:1 Mwa 27:38; Kut 33:4; Hes 25:6; Kum 1:45; Amu 20:23-26; 2Sam 3:32; Ay 31:29Usiku ule watu wote wa jumuiya walipaza sauti zao na kulia kwa sauti kuu. 214:2 Kut 16:3; 15:24; Ebr 3:16; Hes 11:1; 16:13; 20:4; 21:5Waisraeli wote wakanungʼunika dhidi ya Mose na Aroni, nalo kusanyiko lote wakawaambia, “Laiti tungekuwa tumefia humo nchi ya Misri! Au humu kwenye hili jangwa! 314:3 Kut 5:21; Kum 1:39; Mwa 34:29; Za 109:11; Isa 33:4; Eze 7:21; 25:7; 26:5; Mdo 7:39Kwa nini Bwana anatuleta katika nchi hii ili tufe kwa upanga? Wake zetu na watoto wetu watachukuliwa kama nyara. Je, isingekuwa bora kwetu kurudi Misri?” 414:4 Neh 9:17; Mdo 7:36; Ebr 11:15Wakasemezana wao kwa wao, “Inatupasa kumchagua kiongozi na kurudi Misri.”

514:5 Law 9:24; 19:2; Hes 16:4, 22, 45; 20:6; Yos 5:12; Eze 1:28; 2Sam 14:4; 1Nya 21:16Ndipo Mose na Aroni wakaanguka kifudifudi mbele ya kusanyiko lote la Kiisraeli lililokusanyika hapo. 614:6 Hes 11:28; Mwa 37:29-34; Amu 11:35; 2Sam 13:31; 1Fal 19:1; Ezr 9:3; Es 4:1; Mk 14:63Yoshua mwana wa Nuni na Kalebu mwana wa Yefune, waliokuwa miongoni mwa watu wale waliokwenda kuipeleleza nchi, wakararua nguo zao, 714:7 Hes 13:27; Kum 1:25wakasema na kusanyiko lote la Kiisraeli, wakawaambia, “Nchi tuliyopita katikati yake na kuipeleleza ni nzuri sana sana. 814:8 Kum 1:21; 7:8; 10:15; Za 18:19; 22:8; 37:23; 41:11; 56:9; 147:11; Mit 11:20; Isa 62:4; Mal 2:17; Hes 13:27Ikiwa Bwana anapendezwa nasi, atatuongoza kuingia katika nchi ile, nchi itiririkayo maziwa na asali, naye atatupa nchi hiyo. 914:9 Kum 1:21, 26; 7:18; 9:7; 20:1; Mwa 21:22; 26:24; 2Nya 13:12; 32:7; Za 118:6; Hag 2:4; 1:13; Yer 15:20; 41:18; 42:11; 46:28Ila tu msimwasi Bwana. Wala msiwaogope watu wa nchi hiyo, kwa sababu tutawameza. Ulinzi wao umeondoka, lakini Bwana yupo pamoja nasi. Msiwaogope.”

1014:10 Kut 17:4; 24:16; Law 9:24Lakini kusanyiko lote likazungumza juu ya kuwapiga kwa mawe. Ndipo utukufu wa Bwana ukaonekana katika Hema la Kukutania kwa Waisraeli wote. 1114:11 Kut 3:20; 4:17; 10:1; 23:21; Hes 15:31; 16:30; 1Sam 2:17; Yn 3:25; Eze 31:14; Mal 1:13; Kum 1:32; Za 78:22; 106:24Bwana akamwambia Mose, “Watu hawa watanidharau mpaka lini? Wataendelea kukataa kuniamini mimi mpaka lini, ingawa nimetenda ishara za miujiza miongoni mwao? 1214:12 Kut 5:3; 33:10; Kum 9:14; 29:20; 32:26; Za 109:13Nitawapiga kwa tauni na kuwaangamiza, lakini nitakufanya wewe kuwa taifa kubwa lenye nguvu kuliko wao.”

1314:13 Kut 32:11; Za 106:23Mose akamwambia Bwana, “Ndipo Wamisri watasikia juu ya jambo hili! Kwa uweza wako uliwapandisha watu hawa kutoka miongoni mwao. 1414:14 Kut 13:21; 15:14; 33:16; Hes 5:3; 16:3; Yos 2:9; Kum 5:4; 34:10Nao watawaambia wenyeji wa nchi hii jambo hili. Wao tayari wameshasikia kwamba wewe, Ee Bwana, upo pamoja na watu hawa, na kuwa wewe, Ee Bwana, umeonekana uso kwa uso, nalo wingu lako hukaa juu yao. Tena wewe unawatangulia kwa nguzo ya wingu mchana na kwa nguzo ya moto usiku. 15Ikiwa utawaua watu hawa wote mara moja, mataifa ambayo yamesikia taarifa hii kukuhusu wewe watasema, 1614:16 Hes 11:12; Kut 32:12; Yos 7:7Bwana alishindwa kuwaingiza watu hawa katika nchi aliyowaahidi kwa kiapo; hivyo akawaua jangwani.’

17“Basi sasa nguvu za Bwana na zionekane, sawasawa na vile ulivyosema: 1814:18 Kut 20:5-6; 34:6; Za 145:8; Yon 4:2; Yak 5:11Bwana si mwepesi wa hasira, ni mwingi wa upendo na mwenye kusamehe dhambi na uasi. Lakini haachi kumwadhibu mwenye hatia, huadhibu watoto kwa ajili ya dhambi ya baba zao hata kizazi cha tatu na cha nne.’ 1914:19 Kut 34:9; 1Fal 8:34; Za 85:2; 103:3; 10:6; 65; 78:38Kwa kadiri ya upendo wako mkuu, usamehe dhambi ya watu hawa, kama vile ulivyowasamehe tangu wakati walitoka Misri mpaka sasa.”

2014:20 Kut 34:6; Za 99:8; 106:23; Mik 7:18-20Bwana akajibu, “Nimewasamehe kama ulivyoomba. 2114:21 Hes 14:28; Kum 32:40; Amu 8:19; Rut 3:13; 1Sam 14:39; 19:6; Isa 6:3; 40:5; 49:18; Yer 4:2; Eze 5:11; Law 9:6; Za 72:19; Hab 2:14Hata hivyo, kwa hakika kama niishivyo, na kwa hakika kama utukufu wa Bwana uijazavyo dunia yote, 2214:22 Kut 14:11; 17:7; 32:1; Za 81:7; 1Kor 10:5hakuna hata mmoja wa watu hawa ambao waliuona utukufu wangu na ishara za miujiza niliyotenda huko Misri na huko jangwani, lakini ambaye hakunitii na akanijaribu mara hizi kumi, 2314:23 Kut 33:1; Hes 32:11; Kum 1:34; Ebr 3:18; Za 95:11; 106:26hakuna hata mmoja wao atakayeona nchi niliyowaahidi baba zao kwa kiapo. Hakuna hata mmoja ambaye amenidharau atakayeiona. 2414:24 Hes 13:6; 26:65; 32:12; Kum 1:36; Yos 14:8, 14; Za 25:13; 37:9-11Lakini kwa sababu mtumishi wangu Kalebu ana roho ya tofauti na ananifuata kwa moyo wote, nitamwingiza katika nchi aliyoiendea, nao wazao wake watairithi. 2514:25 Mwa 14:7; 10:18; Kum 1:40; Kut 23:31; Hes 21:4; 1Fal 9:26Kwa kuwa Waamaleki na Wakanaani wanaishi katika mabonde, kesho geukeni mwelekee jangwani kwa kufuata njia iendayo Bahari ya Shamu.”14:25 Yaani Bahari Nyekundu au Bahari ya Mafunjo.

2614:26 Kut 16:12; Kum 1:34-35Bwana akamwambia Mose na Aroni: 2714:27 Kut 16:28; Mt 17:17; Mk 9:19; Kut 16:12; 1Kor 10:10“Jumuiya hii ovu itanungʼunika dhidi yangu hadi lini? Nimesikia malalamiko ya hawa Waisraeli wanaonungʼunika. 2814:28 Hes 33:56; Ebr 3:17Hivyo waambie, ‘Hakika kama niishivyo, asema Bwana, nitawafanyia vitu vilevile nilivyosikia mkisema: 2914:29 Hes 1:45; 26:65; 32:13; 1Kor 10:5; Ebr 3:17; Yud 5; Kut 30:12Kila mmoja wenu mwenye umri wa miaka ishirini au zaidi ambaye alihesabiwa na amenungʼunika dhidi yangu, miili yenu itaanguka katika jangwa hili. 3014:30 Kut 6:8; Kum 32:40; Neh 9:15; Za 106:26; Eze 20:5; 36:7; Hes 13:6; 11:28Hakuna hata mmoja wenu atakayeingia katika nchi niliyoapa kwa mkono ulioinuliwa kuwa makao yenu, isipokuwa Kalebu mwana wa Yefune, na Yoshua mwana wa Nuni. 3114:31 Law 26:43Lakini watoto wenu ambao mlisema watachukuliwa kama mateka, nitawaingiza humo ili waifurahie nchi ambayo ninyi mmeikataa. 3214:32 1Kor 10:5Lakini ninyi, miili yenu itaanguka katika jangwa hili. 3314:33 Kut 16:35; Mdo 13:18; Ebr 3:9Watoto wenu watakuwa wachungaji wa mifugo hapa kwa miaka arobaini, wakiteseka kwa ajili ya kukosa uaminifu kwenu, hadi mwili wa mtu wenu wa mwisho ulale katika jangwa hili. 3414:34 Hes 13:25; 14:32, 33; Za 95:10; Eze 4:6; Za 77:8; Ebr 4:1Kwa miaka arobaini, mwaka mmoja kwa kila siku katika zile siku arobaini mlizoipeleleza nchi, mtateseka kwa ajili ya dhambi zenu, na kujua jinsi ilivyo vibaya kunifanya mimi kuwa adui yenu.’ 3514:35 Hes 23:19Mimi Bwana nimesema, na hakika nitafanya mambo haya kwa jumuiya hii yote ovu, ambayo imefungamana pamoja dhidi yangu. Watakutana na mwisho wao katika jangwa hili; hapa ndipo watafia.”

3614:36 Hes 13:4-16, 32Hivyo watu wale ambao Mose alikuwa amewatuma kuipeleleza nchi, waliorudi na kuifanya jumuiya nzima kunungʼunika dhidi ya Mose kwa kueneza taarifa mbaya kuhusu hiyo nchi: 3714:37 Hes 13:32; 16:49; 25:9; 26:1; 31:16; 1Kor 10:10; Ebr 3:17; Kum 4:3watu hawa waliohusika kueneza taarifa mbaya kuhusu hiyo nchi walipigwa na kuanguka kwa tauni mbele za Bwana. 3814:38 Hes 13:4-16; Yos 14:6Miongoni mwa watu waliokwenda kuipeleleza hiyo nchi, ni Yoshua mwana wa Nuni, na Kalebu mwana wa Yefune peke yao waliosalia.

3914:39 Kut 33:4; Mit 19:3; Mt 8:12; Ebr 12:17Mose alipotoa taarifa hii kwa Waisraeli wote, waliomboleza kwa uchungu. 4014:40 Hes 13:17; Kut 9:27; Kum 1:41Mapema asubuhi siku iliyofuata walipanda juu kuelekea kwenye nchi ya vilima virefu, wakasema, “Tumetenda dhambi. Tutakwea mpaka mahali Bwana alipotuahidi.”

4114:41 2Nya 24:20; Ay 9:4; Isa 59:1, 2; Yer 2:37Lakini Mose akasema, “Kwa nini hamtii amri ya Bwana? Jambo hili halitafanikiwa! 4214:42 Kum 1:42Msipande juu, kwa kuwa Bwana hayupo pamoja nanyi. Mtashindwa na adui zenu, 4314:43 Amu 1:19; 6:16; 3:13; Hes 13:29; Mwa 39:23; Kum 21:8; Yos 6:27; 1Sam 3:19; 18:14; 2Nya 1:1kwa kuwa Waamaleki na Wakanaani watapambana nanyi huko. Kwa sababu mmemwacha Bwana, hatakuwa pamoja nanyi, ninyi mtaanguka kwa upanga.”

4414:44 Kum 1:43; Hes 31:6Hata hivyo, kwa kiburi chao walipanda juu kuelekea nchi ya vilima virefu, ijapokuwa Mose hakutoka kambini wala Sanduku la Agano la Bwana. 4514:45 Hes 21:3; Kum 1:44; Yos 12:14; 15:30; 19:4; Amu 1:17; 1Sam 30:30; 1Nya 4:30Ndipo Waamaleki na Wakanaani walioishi katika hiyo nchi ya vilima wakateremka na kuwashambulia, wakawapiga njia yote hadi Horma.