Numeri 10 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 10:1-36

Malipenga Asiliva

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa. 3Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano. 4Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe. 5Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka. 6Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo. 7Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.

8“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse. 9Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu. 10Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”

Aisraeli Achoka ku Sinai

11Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni. 12Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani. 13Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.

14Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu. 15Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara, 16Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni. 17Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.

18Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri. 19Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai, 20ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi. 21Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.

22Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo. 23Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase. 24Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.

25Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai. 26Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri, 27ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani. 28Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.

29Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”

30Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”

31Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu. 32Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”

33Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo. 34Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.

35Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti,

“Dzukani, Inu Yehova!

Adani anu abalalike;

Odana nanu athawe pamaso panu.

36“Pamene likupumula, ankanena kuti,

“Bwererani, Inu Yehova,

ku chinamtindi cha Aisraeli.”

Korean Living Bible

민수기 10:1-36

두 개의 은나팔

1여호와께서 모세에게 말씀하셨다.

2“너는 은을 두들겨 나팔 두 개를 만 들고 그것을 불어 백성을 소집하며 행진하게 하여라.

3나팔 둘을 길게 불면 모든 백성이 성막 입구 네 앞에 모이게 하고

4나팔을 하나만 불면 10:4 또는 ‘천부장된 족장들’각 집안의 대표자들만 모이게 하라.

5나팔을 짧게 불면 동쪽에 진을 친 지파들이 행진하고

6다시 짧게 불면 남쪽에 진을 친 지파들이 행진하게 하여라. 이와 같이 행진 신호는 나팔을 짧게 불고

7소집 신호는 길게 불도록 하라.

8나팔은 아론의 자손인 제사장들만 불어야 한다. 이것은 너희가 대대로 지켜야 할 규정이다.

9“너희가 약속의 땅에 도착하여 너희를 대적하는 원수들과 싸우러 나갈 때 이 나팔을 불어라. 그러면 너희 하나님 나 여호와가 너희를 기억하고 너희를 원수들에게서 구원해 주겠다.

10또 기쁜 날과 명절과 매월 초하루에 번제물과 화목제물을 드릴 때에도 나팔을 불어라. 그러면 내가 너희를 기억할 것이다. 나는 너희 하나님 여호와이다.”

시내산을 떠나는 이스라엘 백성

11이스라엘 백성이 이집트를 떠나온 지 2년째가 되는 해 2월 20일에 구름이 성막에서 떠오르자

12그들은 시나이 광야에서 출발하여 그 구름이 바란 광야에 멈출 때까지 구름을 따라 행진하였다.

13이것은 여호와께서 모세에게 행진 명령을 내린 후 첫번째 행진이었는데

14이 행렬 선두에는 유다 지파 진영에 속한 자들이 기를 앞세우고 암미나답의 아들 나손이 인솔하는 유다 지파와

15수알의 아들 느다넬이 인솔하는 잇사갈 지파와

16헬론의 아들 엘리압이 인솔하는 스불론 지파가 순서대로 행진하였다.

17그러고 나서 성막이 걷혀지고 게르손 자손과 므라리 자손이 성막을 메고 그 뒤를 따라 출발하였다.

18그 뒤에는 르우벤 지파 진영에 속한 자들이 기를 앞세우고 스데울의 아들 엘리술이 인솔하는 르우벤 지파와

19수리삿대의 아들 슬루미엘이 인솔하는 시므온 지파와

20드우엘의 아들 엘리아삽이 인솔하는 갓 지파가 순서대로 행진하였다.

21그 뒤에는 고핫 자손이 성막의 거룩한 기구들을 메고 행진하였으며 이들이 다음 진영에 도착하기 전에 성막이 세워졌다.

22그 다음은 에브라임 지파 진영에 속한 자들이 기를 앞세우고 암미훗의 아들 엘리사마가 인솔하는 에브라임 지파와

23브다술의 아들 가말리엘이 인솔하는 므낫세 지파와

24기드오니의 아들 아비단이 인솔하는 베냐민 지파가 순서대로 행진하였다.

25그리고 제일 뒤에는 단 지파 진영에 속한 자들이 기를 앞세우고 암미삿대의 아들 아히에셀이 인솔하는 단 지파와

26오그란의 아들 바기엘이 인솔하는 아셀 지파와

27에난의 아들 아히라가 인솔하는 납달리 지파가 순서대로 행진하였다.

28이상은 이스라엘 각 지파가 진영별로 행진한 대열의 순서이다.

29어느 날 모세는 미디안 사람 이드로의 아들인 그의 처남 호밥에게 말하였다. “지금 우리는 약속의 땅으로 가고 있으니 처남도 함께 가세. 우리가 자네를 잘 돌봐 주겠네. 여호와께서는 이스라엘 백성에게 복을 주시겠다고 약속하셨다네.”

30“아니오, 가지 않겠습니다. 나는 10:30 또는 ‘내 고향 내 친척에게로’친척들이 있는 고향으로 돌아가야 합니다.”

31“그러지 말고 함께 가세. 처남은 이 광야 길을 잘 알고 있으니 우리의 좋은 안내자가 될 걸세.

32만일 처남이 우리와 함께 가면 여호와께서 우리에게 주시는 모든 좋은 것을 처남도 함께 누리게 될 것이네.”

33이스라엘 백성은 시내산을 떠나 3일 동안 행진하면서 법궤를 앞세우고 진 칠 곳을 찾았는데

34그들이 행진할 때 낮에는 여호와의 구름이 그들 위에 있었다.

35모세는 법궤가 떠날 때마다 “여호와여, 일어나셔서 주의 원수들을 흩으시고 주를 미워하는 자들이 주 앞에서 도망하게 하소서” 하고 외쳤으며

36법궤가 멈출 때마다 “오! 여호와여, 수백만의 이스라엘 백성에게 돌아오소서” 하였다.