Numeri 10 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 10:1-36

Malipenga Asiliva

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa. 3Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano. 4Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe. 5Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka. 6Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo. 7Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.

8“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse. 9Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu. 10Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”

Aisraeli Achoka ku Sinai

11Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni. 12Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani. 13Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.

14Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu. 15Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara, 16Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni. 17Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.

18Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri. 19Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai, 20ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi. 21Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.

22Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo. 23Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase. 24Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.

25Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai. 26Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri, 27ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani. 28Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.

29Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”

30Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”

31Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu. 32Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”

33Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo. 34Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.

35Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti,

“Dzukani, Inu Yehova!

Adani anu abalalike;

Odana nanu athawe pamaso panu.

36“Pamene likupumula, ankanena kuti,

“Bwererani, Inu Yehova,

ku chinamtindi cha Aisraeli.”

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

民数记 10:1-36

银号

1耶和华对摩西说: 2“你要用银子打造两支号,用来招聚会众和发出拔营的号令。 3吹响两支号时,全体会众要聚集到你那里,即会幕门口。 4如果只吹响一支号,担任首领的以色列各族长要聚集到你那里。 5如果吹响拔营的号令,在东面扎营的就要启行; 6第二次吹响拔营号令时,在南面扎营的就要启行。拔营号令是启行的信号。 7但吹号招聚会众时,不要用拔营号令。 8做祭司的亚伦子孙要负责吹号,这是世代不变的律例。 9当你们在自己的土地上跟敌人作战时,要吹号,你们的上帝耶和华必眷顾你们,救你们脱离敌人。 10在节期和朔日10:10 朔日”即每月初一。这些欢乐的日子献燔祭和平安祭的时候,你们要吹号,好在你们的上帝面前蒙眷顾。我是你们的上帝耶和华。”

离开西奈山

11第二年的二月二十日,云彩从安放约柜的圣幕上升起, 12以色列人就从西奈旷野启行,直到云彩停在巴兰旷野时才停下来。 13这是他们初次照耶和华借摩西的吩咐启行。

14犹大旗下的营队率先出发,率领犹大支派的是亚米拿达的儿子拿顺15率领以萨迦支派的是苏押的儿子拿坦业16率领西布伦支派的是希伦的儿子以利押17然后,圣幕被拆下,革顺米拉利的子孙抬着圣幕出发。 18随后出发的是吕便旗下的营队,率领吕便支派的是示丢珥的儿子以利苏19率领西缅支派的是苏利沙代的儿子示路蔑20率领迦得支派的是丢珥的儿子以利雅萨

21随后出发的是哥辖人,他们抬着圣物前行。在他们到达之前,圣幕应已支好。 22随后出发的是以法莲旗下的营队,率领以法莲支派的是亚米忽的儿子以利沙玛23率领玛拿西支派的是比大苏的儿子迦玛列24率领便雅悯支派的是基多尼的儿子亚比但

25殿后的是旗下的营队,率领支派的是亚米沙代的儿子亚希以谢26率领亚设支派的是俄兰的儿子帕结27率领拿弗他利支派的是以南的儿子亚希拉28这是以色列各营队拔营前行的次序。

29摩西对岳父流珥之子米甸何巴说:“我们就要动身前往耶和华应许给我们的地方,祂曾说要把那地方赐给我们。请你跟我们一起去吧,我们必厚待你,耶和华已经应许要赐福给以色列人。” 30何巴说:“我不去了,我要回到我的家乡和亲族那里。” 31摩西说:“请不要离开我们。你熟悉旷野,可以做我们的向导,告诉我们在哪里扎营。 32如果你跟我们同去,我们一定与你分享耶和华赐给我们的福气。”

33以色列人离开耶和华的山,走了三天的路程,期间耶和华的约柜一直在队伍的前头,为他们寻找安营之地。 34他们拔营前行的时候,白天总有耶和华的云彩在他们上面。 35每当约柜出发的时候,摩西就说:“耶和华啊,求你兴起,击溃你的敌人,使恨你的人逃窜。” 36约柜停下来的时候,他就说:“耶和华啊,求你回到以色列的千万人中。”