Nehemiya 6 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 6:1-19

Adani Apitiriza Kutsutsa ndi Kuopseza Nehemiya

1Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata. 2Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.”

Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko. 3Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?” 4Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.

5Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata. 6Mu kalatamo munali mawu akuti,

“Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo. 7Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”

8Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”

9Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.”

Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”

10Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”

11Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!” 12Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi. 13Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.

14Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”

Kutsiriza kwa Khoma

15Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52. 16Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.

17Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo, 18pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya. 19Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.

New Russian Translation

Неемия 6:1-19

Дальнейшее противодействие строительству стены

1Когда Санбаллату, Товии, арабу Гешему и прочим нашим врагам донесли, что я отстроил стену и в ней не осталось ни одного незаделанного пролома (хотя к тому времени я еще не поставил двери ворот), 2Санбаллат и Гешем послали сказать мне:

– Давай встретимся в одном из селений на равнине Оно.

Но они замышляли причинить мне зло, 3и я послал к ним вестников с таким ответом:

– Я занят важной работой и не могу прийти. Зачем останавливать работу из-за того, чтобы пойти к вам?

4Четыре раза они присылали ко мне с этим посланием, и четыре раза я давал им этот ответ. 5Тогда в пятый раз Санбаллат отправил ко мне с этим же посланием своего слугу. В руке у него было незапечатанное письмо, 6в котором было написано:

«Среди народов ходит слух, и Гешем6:6 Евр.: «Гашму». говорит, что ты и иудеи замышляете восстать, и поэтому ты строишь стену. По этим слухам ты собираешься стать их царем 7и даже назначил пророков, чтобы возвещать о себе в Иерусалиме: „В Иудее есть царь!“ Этот слух дойдет до царя. Итак, приходи, давай вместе посоветуемся».

8Я послал ему ответ: «Нет никакой правды в том, что ты говоришь. Все это ты выдумываешь сам».

9Все они старались запугать нас, думая: «Их руки очень ослабнут, чтобы делать эту работу, и она не будет завершена».

Но я молился:

– Укрепи мои руки.

10Однажды я пришел в дом Шемаи, сына Делаи, внука Мегетавела, который заперся в своем доме. Он сказал:

– Давай встретимся в доме Божьем, внутри храма, и запрем храмовые двери, потому что тебя придут убить, и придут ночью!

11Но я сказал:

– Разве такой человек, как я, может бежать? Может ли такой, как я, пойти в храм, чтобы спасти свою жизнь? Не пойду!

12Я понимал, что Бог не посылал его, и он пророчествовал против меня, потому что его наняли Товия и Санбаллат. 13Его наняли запугать меня, чтобы я согрешил, сделав так, а они бы лишили меня доброго имени и упрекали бы меня.

14Вспомни, Боже мой, Товию и Санбаллата по их делам; вспомни еще и пророчицу Ноадию и прочих пророков, которые пытались меня запугать.

Завершение восстановления стены

15Стена была завершена в двадцать пятый день месяца элула6:15 2 октября 445 г. до н. э., за пятьдесят два дня. 16Когда об этом услышали все наши враги, все окрестные народы испугались6:16 Другое чтение: «увидели». и потеряли свою самоуверенность, потому что поняли, что эта работа была сделана с помощью нашего Бога.

17Еще в те дни знать Иудеи посылала много писем Товии, а письма Товии приходили к ним. 18Ведь многие в Иудее были связаны с ним клятвой, потому что он был зятем Шекании, сына Араха, а его сын Иоханан женился на дочери Мешуллама, сына Берехии. 19Они даже говорили при мне о его добрых делах, а после пересказывали ему то, что я сказал. А Товия присылал письма, чтобы меня запугать.