Nehemiya 5 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 5:1-19

Nehemiya Ateteza Anthu Aumphawi

1Tsono anthu ena ndi akazi awo anayamba kudandaula kwambiri chifukwa cha Ayuda anzawo. 2Ena ankanena kuti, “Ife ndi ana athu aamuna ndi aakazi, tilipo ochuluka kwambiri. Choncho tikufuna tirigu kuti tidye ndi kukhala ndi moyo.”

3Panali ena amene ankanena kuti, “Ife tikuchita kupereka minda yathu, mitengo yathu ya mphesa ndi nyumba zathu ngati chikole kuti tipeze tirigu chifukwa njala yakula.”

4Panalinso ena amene ankanena kuti, “ife tinachita kukongola ndalama zoti tipereke msonkho wa minda ndi mitengo yathu ya mphesa kwa mfumu. 5Ngakhale kuti ndife amodzi ndi abale athuwa, ndipo ngakhalenso ana athu ndi ofanana ndi ana awo, ife tikukakamiza ana athu kuti akhale akapolo. Ena mwa ana athu aakazi atengedwa kale ukapolo. Ife tilibe mphamvu yochitapo kanthu popeza anthu ena anatenga kale minda yathu ndi mitengo yathu ya mphesa.”

6Nditamva madandawulo awo ndi zimene amanenazi ndinapsa mtima kwambiri. 7Nditalingalira bwino ndinatsimikiza zoti ndichitepo kanthu ndipo kenaka ndinawadzudzula anthu olemekezeka ndi akuluakuluwo. Ndinawawuza kuti, “Zoona ndithu inu nʼkumalipiritsana chiwongoladzanja chachikulu anthu apachibale nokhanokha!” Choncho ndinayitanitsa msonkhano waukulu kuti ndiwazenge mlandu 8ndipo ndinati, “Monga zakhaliramu ife tikutha kuwombola abale anthu amene anagulitsidwa ukapolo kwa anthu ena. Kodi tsopano inu mukugulitsanso abale anu kwa anzawo kuti ife tiwumirizidwe kuwawombola?” Iwo anakhala chete, chifukwa sanapeze mawu oti anene.

9Kotero ndinapitiriza kunena kuti, “Zimene mukuchitazi si zabwino. Kodi inu simungakhale ndi moyo woopa Mulungu wathu kuti tipewe kunyoza kwa adani athu, anthu a mitunda inayi? 10Ine ndi abale anga ndiponso antchito anga tikuwakongozanso anthuwa ndalama ndi tirigu. Ndipo tiyeni tilekeretu zolandira chiwongoladzanja! 11Abwezereni lero lomwe minda yawo, mitengo ya mphesa, mitengo ya olivi ndiponso nyumba zawo. Muwabwezerenso chiwongoladzanja cha ndalama, tirigu, vinyo ndi mafuta zimene munatenga.”

12Iwo anayankha kuti, “Ife tidzawabwezera zimenezi popanda kupemphapo kanthu kalikonse kwa iwo. Tidzachita monga mwanena.”

Pambuyo pake ndinayitanitsa ansembe ndipo pamaso pawo ndinawalumbiritsa atsogoleriwo ndi akuluakuluwo kuti adzachitadi zomwe analonjezazo. 13Ndipo inenso ndinakutumula chovala changa ndi kuti, “Chimodzimodzinso Mulungu akutumule munthu wosasunga malonjezano ake. Amulande nyumba yake ndi katundu wake ndi kumusandutsa mʼmphawi!”

Apo msonkhano wonse unati, “Ameni” natamanda Yehova. Ndipo anthu aja anachita monga analonjezera.

14Ndiponso kuyambira nthawi imene anandisankha kuti ndikhale bwanamkubwa wa dziko la Yuda, kuchokera chaka cha makumi awiri mpaka chaka cha 32 muulamuliro wa ufumu wa Aritasasita, ndiye kuti kwa zaka zokwana 12, ine ngakhale abale anga sitinalandire chakudya choyenerera bwanamkubwa. 15Koma abwanamkubwa akale ankasautsa anthu. Iwo ankalanda anthu chakudya ndi vinyo ndi kuwalipiritsanso masekeli asiliva makumi anayi. Ngakhalenso antchito awo amavutitsa anthu kwambiri. Koma ine sindinachite zimenezo chifukwa ndimaopa Mulungu. 16Ndiponso ndinadzipereka kugwira ntchito yomanga khoma la mzinda wa Yerusalemu popanda ngakhale kugulapo munda. Antchito anganso anasonkhana komweko kuti agwire ntchito ndipo sitinafunenso malo ena.

17Kuwonjezera apa, ndinkadyetsa Ayuda, akuluakulu kuphatikizanso anthu amene ankabwera kwa ife kuchokera kwa mitundu ya anthu otizungulira okwanira 150. 18Tsiku lililonse pamaphikidwa ngʼombe imodzi, nkhosa zabwino zisanu ndi imodzi pamodzi ndi nkhuku. Ndipo pakutha pa masiku khumi aliwonse pankakhala matumba achikopa ochuluka a vinyo wa mitundu yonse. Ngakhale zinali choncho, Ine sindinatenge chakudya choperekedwa kwa bwanamkubwa, chifukwa izi zinali zosautsa anthu.

19Kuti zinthu zindiyendere bwino, kumbukirani Yehova Mulungu wanga pa zonse zimene ndachitira anthu awa.

Bibelen på hverdagsdansk

Nehemiasʼ Bog 5:1-19

Nehemias taler de fattiges sag

1Kort efter begyndte nogle mænd og deres koner at klage over, at deres rige landsmænd udnyttede dem. 2Nogle sagde: „Vi har ingen penge, så vi må give vores børn i pant for at få mad.” 3Andre sagde: „Vi har pantsat vores marker, vingårde og huse for at kunne købe korn under hungersnøden.” 4Andre igen sagde: „Vi har måttet belåne vores marker og vingårde for at kunne betale skat til kongen.”

5„Hører vi ikke til samme folk?” protesterede de. „Er vores børn ikke lige så gode som deres? Det er uretfærdigt, at vi skal sælge vores børn som slaver for at kunne overleve. Vi har allerede solgt flere af vores døtre, og vi har ingen mulighed for at købe dem fri, for vores marker og vingårde tilhører pantelånerne.”

6Da jeg hørte det, blev jeg vred, 7og efter at have tænkt over sagen sagde jeg til de rige og fornemme: „Det er forkert af jer at tage pant og renter af jeres landsmænd, når I låner dem penge.” Så sammenkaldte jeg til et folkemøde og henvendte mig til de rige: 8„Vi har gjort alt, hvad vi kunne, for at frikøbe vores landsmænd, der levede som slaver hos et fremmed folk,” sagde jeg. „Men nu gør I jeres egne landsmænd til slaver! Hvor mange gange skal vi købe dem fri?” Der var dødstille. Ingen vidste, hvad de skulle svare. 9Så fortsatte jeg: „I kan ikke være bekendt at opføre jer på den måde! Har I slet ingen ærefrygt for Gud? Er det ikke nok, at vi har fjender, der udefra prøver at komme os til livs? 10Jeg og mine folk har også lånt vores nødstedte landsmænd penge og korn, men uden at kræve renter. Hold op med at tage pant og renter. 11Giv dem deres marker, vingårde, olivenlunde og huse tilbage og refunder dem, hvad I har taget i renter i form af penge, korn, vin og olie.”

12„Vi vil gøre, som du siger,” svarede de. „Vi giver dem deres ejendom tilbage og holder op med at kræve renter.” I præsternes påhør fik jeg dem så til at sværge på, at de ville gøre, som de havde sagt. 13Og mens jeg rystede min kappefold sagde jeg: „De som ikke holder, hvad de har lovet, vil Gud ryste ud fra deres hus og hjem.” „Amen!” råbte hele forsamlingen og takkede Gud. Så gik de i gang med at gøre deres ord til handling.

14I den forbindelse skal det nævnes, at i alle de 12 år, jeg var guvernør over Juda—fra kong Artaxerxes’ 20. til hans 32. regeringsår—modtog hverken jeg selv eller mine embedsmænd nogen løn eller andre ydelser fra Israels folk. 15Denne praksis stod i skærende kontrast til, hvad folket var vant til fra de tidligere guvernører, der havde udnyttet dem ved at kræve mad og vin foruden 40 sølvstykker om dagen. Desuden plejede embedsmændene også at udnytte folket. Men fordi jeg ønskede at adlyde Gud, brød jeg med den praksis. 16I stedet koncentrerede jeg mig om arbejdet på muren og nægtede at skaffe mig fast ejendom. Og alle mine embedsmænd tog del i arbejdet på lige fod med andre. 17Jeg forsørgede ellers 150 judæiske embedsmænd foruden fremmede, der kom på besøg. 18Det daglige forbrug udgjorde en okse, seks førsteklasses får og et stort antal fjerkræ. Desuden købte jeg hver tiende dag en ny forsyning vin. Alligevel undlod jeg at afkræve folket den skat, jeg havde krav på, for de havde det svært nok i forvejen.

19Min Gud, glem ikke, hvad jeg har gjort for dit folk, men velsign mig for det!