Nehemiya 2 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 2:1-20

Aritasasita Atumiza Nehemiya ku Yerusalemu

1Pa mwezi wa Nisani, mʼchaka cha makumi awiri cha ufumu wa Aritasasita, atabwera ndi vinyo pamaso pa mfumu ine ndinatenga vinyoyo ndi kupereka kwa mfumu. Koma ndinali ndisanakhalepo ndi nkhope yachisoni pamaso pake. 2Tsono mfumu inandifunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani nkhope yako ikuoneka yachisoni pamene iwe sukudwala? Ichi si chinthu china koma chisoni cha mu mtima.”

Ine ndinachita mantha kwambiri. 3Ndinawuza mfumu kuti, “Mfumu ikhale ndi moyo wamuyaya! Kodi nkhope yanga ilekerenji kuoneka yachisoni pamene mzinda umene kuli manda a makolo anga, wasanduka bwinja ndipo zipata zake zinawonongedwa ndi moto?”

4Apo mfumu inandifunsa kuti, “Tsono ukufuna kundipempha chiyani?”

Ndipo ine ndinapemphera kwa Mulungu Wakumwamba. 5Ndipo ndinayankha kuti, “Ngati amfumu chingakukondweretseni, ngati mungakomere mtima mtumiki wanune, mundilole kuti ndipite ku Yuda, ku mzinda kumene kuli manda a makolo anga kuti ndikawumangenso.”

6Tsono mfumu, mfumukazi itakhala pambali pake, anandifunsa kuti, “Kodi kumeneko ukakhalako masiku angati ndipo udzabwera liti?” Ndinayiwuza mfumu nthawi yake ndipo inandilola kuti ndipite.

7Ndipo ndinatinso kwa mfumu, “Ngati zikondweretse mfumu, mundipatse makalata oti ndikapereke kwa abwanamkubwa a ku chigawo cha Patsidya pa Yufurate, kuti akandilole kudutsa mwamtendere mpaka nditakafika ku Yuda. 8Mundipatsenso kalata yokapereka kwa Asafu woyangʼanira nkhalango ya mfumu, kuti akandipatse mitengo yokapangira mitanda ya zipata za nsanja yoteteza Nyumba ya Mulungu, mitanda ya khoma la mzinda ndi ya nyumba yokhalamo ine.” Mfumu indipatse zomwe ndinapempha popeza Yehova wokoma mtima anali nane. 9Choncho ndinanyamuka ulendo wanga ndipo ndinafika kwa abwanamkubwa a chigawo cha Patsidya pa Yufurate ndipo ndinawapatsa makalata a mfumu. Mfumu nʼkuti itatumiza akulu ankhondo ndi okwera pa akavalo kuti atsagane nane.

10Sanibalati wa ku Horoni ndi Tobiya wa ku Amoni atamva zimenezi, iwo anayipidwa kwambiri kuti wina wabwera kudzachitira zabwino Aisraeli.

Nehemiya Ayendera Makoma a Yerusalemu

11Ndinafika ku Yerusalemu, ndipo ndinakhala kumeneko masiku atatu. 12Sindinawuze munthu aliyense za zimene Yehova anayika mu mtima mwanga kuti ndichitire mzinda wa Yerusalemu. Choncho ndinanyamuka usiku pamodzi ndi anthu ena owerengeka. Ndinalibe bulu wina aliyense kupatula amene ndinakwerapo.

13Ndinatuluka usiku podzera ku Chipata cha ku Chigwa ndi kuyenda kupita ku Chitsime cha Chirombo Chamʼmadzi mpaka ku Chipata cha Zinyalala. Ndinayangʼana makoma a Yerusalemu, amene anagwetsedwa, ndi zipata zake, zimene zinawonongedwa ndi moto. 14Kenaka ndinapita ku Chipata cha Kasupe ndi ku Dziwe la Mfumu. Koma panalibe malo okwanira akuti bulu wanga adutse. 15Kotero usikuwo ndinapita ku chigwa, ndikuyangʼana khomalo. Pomaliza ndinabwerera ndi kukalowanso mu mzinda kudzera ku Chipata cha ku Chigwa. 16Akuluakulu sanadziwe kumene ndinapita kapena zimene ndimachita, chifukwa pa nthawiyi nʼkuti ndisananene kalikonse kwa Ayuda kapena ansembe, anthu olemekezeka kapena akuluakulu, kapena wina aliyense amene anali woyenera kugwira ntchitoyi.

17Ndinawawuza kuti, “Inu mukuona mavuto amene tili nawo. Mukuona kuti mzinda wa Yerusalemu wasanduka bwinja ndipo zipata zake zatenthedwa ndi moto. Tsono tiyeni timangenso makoma a Yerusalemu ndipo sitidzachitanso manyazi.” 18Ndinawawuza za mmene Yehova Mulungu wanga anandichitira zabwino ndiponso mawu amene mfumu inandiwuza.

Tsono anati, “Tiyeni tiyambenso kumanga.” Kotero analimbitsana mtima kuti ayambenso ntchito yabwinoyi.

19Koma Sanibalati wa ku Horoni, Tobiya wa ku Amoni ndi Gesemu Mwarabu atamva zimenezi, anatiseka ndi kutinyoza. Iwo anafunsa kuti, “Kodi muti ndi chiyani chimene mukuchitachi? Kodi mufuna kuwukira mfumu?”

20Koma ndinawayankha kuti, “Mulungu Wakumwamba atithandiza kuti zinthu zitiyendere bwino. Ife antchito ake tiyambapo kumanga. Koma inu mulibe gawo lanu muno mu Yerusalemu. Mulibe chokuyenerezani kulandira malo ano. Mulibenso chilichonse muno chokumbutsa za inu.”

New Serbian Translation

Књига Немијина 2:1-20

Артаксеркс шаље Немију у Јерусалим

1Било је то месеца нисана2,1 Март/април. двадесете године цара Артаксеркса. Пред њим је било вино и ја сам узео то вино и дао га цару. И никада раније нисам био тужан пред њим. 2Цар ми рече: „Зашто ти је лице тужно? Да ниси болестан? То није ништа него нека туга срца.“

А ја сам се јако уплашио 3и рекао цару: „Нека је цар жив довека! Како да ми лице не буде жалосно када је опустошен град где су гробови мојих предака, а врата су му огњем спаљена?“

4Рече ми цар: „Дакле, шта желиш?“

А ја сам се помолио Богу небеском 5и одговорио цару: „Ако цар нађе за добро и ако му је по вољи твој слуга пред тобом, онда ме пошаљи у Јуду, у град где су гробови мојих предака и ја ћу да га обновим.“

6Цар ме је – док је царица седела поред њега – питао: „Докле ћеш бити на путу и када ћеш да се вратиш?“ Цару је то било по вољи, па ме је послао, а ја сам му рекао за време.

7Још сам казао цару: „Ако је цару по вољи, нека ми да писма за управитеље подручја преко реке, како би ме пустили да прођем док не дођем у Јуду. 8И писмо за Асафа, чувара цареве шуме, да би ми дао дрва, како би се направиле греде за врата утврђења, које припада Дому, за градски зид и за кућу у којој ћу бити.“ Цар ми их је дао јер је добра рука мога Бога била нада мном. 9Тако сам отишао управитељима подручја преко реке и дао им царева писма. Цар је још са мном послао војне заповеднике и коњанике.

10Али када су то чули Санавалат Ороњанин и Товија, слуга Амонац, било им је веома мрско што је дошао неко да тражи добро за израиљски народ.

Немија проверава зидине Јерусалима

11Дошао сам у Јерусалим и био тамо три дана. 12Устао сам ноћу, ја и неколицина људи са мном, али никоме нисам казао шта ми је мој Бог ставио у срце да урадим за Јерусалим. А од животиња ништа није било уз мене осим живинчета на коме сам јахао.

13Изашао сам на Долинска врата, ноћу, наспрам Змајевог извора и Гнојних врата. Проверавао сам зидове Јерусалима. Били су порушени, а његова врата спаљена огњем. 14Прошао сам до Изворских врата и до Царевог језера, али тамо није било места да прође живинче испод мене. 15Пењао сам се уз поток, ноћу, и проверавао зид, а онда сам се окренуо назад ка Долинским вратима и вратио се. 16Достојанственици нису знали где сам отишао и шта сам радио. Наиме, никог од Јевреја, свештеника, главара и достојанственика, који су радили на подухвату, нисам обавестио до сада.

17И тада сам им казао: „Ви видите невољу у којој смо: да је Јерусалим опустошен, да су му врата огњем спалили. Дођите, хајде да обновимо јерусалимски зид и не будемо опет на срамоту!“ 18Испричао сам им о доброј руци мога Бога, која је била нада мном, о царевим речима које ми је рекао.

А они су рекли: „Устанимо и зидајмо!“ Тако су се охрабрили за добро дело.

19Али то су чули Санавалат Ороњанин, Товија, слуга Амонац и Гисем Арапин, ругали су нам се и гледали нас с презиром. Казали су: „Шта је то што радите? Буните ли се против цара?!“

20Ја сам им узвратио и казао им: „Бог небески ће нам дати да успемо. И ми, његове слуге, ћемо устати и зидати. А вама не припада ни део ни право ни спомен у Јерусалиму.“