Nehemiya 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nehemiya 1:1-11

Pemphero la Nehemiya

1Awa ndi mawu a Nehemiya mwana wa Hakaliya:

Pa mwezi wa Kisilevi, chaka cha makumi awiri, pamene ndinali mu mzinda wa Susa, 2Hanani mmodzi mwa abale anga, anabwera ndi anthu ena kuchokera ku Yuda, ndipo ine ndinawafunsa za Ayuda otsala amene sanatengedwe ukapolo, ndiponso za mzinda wa Yerusalemu.

3Anandiyankha kuti, “Amene sanatengedwe ukapolo aja ali pa mavuto aakulu ndipo ali ndi manyazi. Khoma la Yerusalemu ndilogamukagamuka ndipo zipata zake zinatenthedwa ndi moto.”

4Nditamva zimenezi, ndinakhala pansi ndi kuyamba kulira. Ndinalira kwa masiku angapo. Ndinkasala zakudya ndi kumapemphera pamaso pa Mulungu Wakumwamba. 5Ndinkati:

“Inu Yehova, Mulungu wakumwamba, Mulungu wamkulu ndi woopsa. Mumasunga pangano ndi kuonetsa chikondi chosasinthika kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu. 6Tcherani khutu lanu ndi kutsekula maso anu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune limene ndikupemphera usana ndi usiku pamaso panu kupempherera Aisraeli, atumiki anu. Ndikuvomereza machimo a Aisraeli amene tinakuchimwirani. Ndithu, ine ndi banja la makolo anga tinakuchimwirani. 7Ife tinakuchitirani zoyipa zambiri. Sitinamvere mawu anu, malamulo ndi malangizo anu amene munapereka kwa mtumiki wanu Mose.

8“Kumbukirani mawu amene munawuza mtumiki wanu Mose akuti, ‘Ngati mukhala osakhulupirika, ndidzakubalalitsani pakati pa mitundu ina. 9Koma mukabwerera kwa Ine, mukamvera malamulo anga ndi kuwatsatadi, ndiye kuti ngakhale anthu anu atabalalika kutali chotani, Ine ndidzawasonkhanitsa kuchokera kumeneko ndi kubwera nawo ku malo amene ndinasankha kuti azidzayitanira dzina langa.’

10“Iwo ndi atumiki anu ndi anthu anu, amene munawawombola ndi mphamvu yanu yayikulu ndi dzanja lanu lamphamvu. 11Inu Ambuye tcherani khutu lanu kuti mumve pemphero la mtumiki wanune ndiponso pemphero la atumiki anu amene amakondwera kuchitira ulemu dzina lanu. Lolani kuti mtumiki wanune zinthu zindiyendere bwino lero ndi kuti mfumu indichitire chifundo.”

Nthawi imeneyi nʼkuti ndili woperekera zakumwa kwa mfumu.

New Russian Translation

Неемия 1:1-11

Молитва Неемии об Иерусалиме

1Слова Неемии, сына Хахалии:

В месяце кислеве, в двадцатом году1:1 Поздней осенью 446 г. до н. э. правления царя Артаксеркса1:1 Артаксеркс I Лонгиман (Долгорукий) правил Персидской империей с 464 по 424 гг. до н. э., когда я находился в крепости города Сузы, 2Ханани – один из моих братьев, пришел из Иудеи с некоторыми другими людьми, и я расспросил их об уцелевших жителях Иудеи, которые вернулись из плена, и об Иерусалиме.

3Они сказали мне:

– Те, кто прошел через плен и вернулся в провинцию1:3 Или: «Те, кто остался в провинции и не пошел в плен»., сейчас в большой беде и бесчестии. Стена Иерусалима разрушена, а его ворота сожжены.

4Услышав это, я сел и заплакал. Несколько дней я скорбел, постился и молился пред Богом небесным. 5Я говорил:

– Господи, Боже небес, Бог великий и грозный, хранящий завет и милость к тем, кто любит Его и слушается Его повелений, 6да будут уши Твои внимательны и глаза Твои открыты, чтобы услышать молитву Твоего слуги, которой я молюсь перед Тобой день и ночь за Твоих слуг, народ Израиля. Я открыто признаюсь в грехах, которыми мы, израильтяне, включая меня и дом моего отца, согрешили против Тебя. 7Мы поступали перед Тобой нечестиво. Мы не слушались повелений, уставов и законов, которые Ты дал Своему слуге Моисею.

8Вспомни повеление, которое Ты дал Своему слуге Моисею, сказав: «Если вы нарушите верность, Я рассею вас среди народов, 9но если вы вернетесь ко Мне и станете слушаться Моих повелений, то даже если ваши изгнанники будут находиться на краю земли, Я соберу их оттуда и приведу на место, которое Я избрал обителью для Моего имени».

10Они – Твои слуги и Твой народ, который Ты искупил Своей великой силой и могучей рукой. 11Владыка, да будут уши Твои внимательны к молитве Твоего слуги и к молитве Твоих слуг, которые любят чтить Твое имя. Дай сегодня Твоему слуге успех, даровав ему расположение этого человека.

Я был виночерпием1:11 Виночерпий был одним из самых важных лиц при дворе, которому царь доверял свою жизнь. царя.