Mlaliki 5 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 5:1-20

Lemekeza Mulungu

1Uzisamala mayendedwe ako pamene ukupita ku nyumba ya Mulungu. Upite pafupi kuti ukamvetsere mʼmalo mopereka nsembe ya zitsiru zimene sizizindikira kuti zikuchita zolakwa.

2Usamafulumire kuyankhula,

usafulumire mu mtima mwako

kunena chilichonse pamaso pa Mulungu.

Mulungu ali kumwamba

ndipo iwe uli pa dziko lapansi,

choncho mawu ako akhale ochepa.

3Kuchuluka kwa mavuto mu mtima kumabweretsa maloto oyipa,

ndipo kuchuluka kwa mawu kumadzetsa uchitsiru.

4Pamene ulumbira kwa Mulungu usachedwe kukwaniritsa chimene walumbiracho. Iye sakondweretsedwa ndi chitsiru; kwaniritsa lumbiro lako. 5Kuli bwino kusalumbira kusiyana ndi kulumbira koma osakwaniritsa lumbirolo. 6Pakamwa pako pasakuchimwitse. Ndipo usanene kwa mthenga wa mʼNyumba ya Mulungu kuti, “Ndinalakwitsa polumbira.” Chifukwa chiyani ukufuna Mulungu akwiye ndi mawu ako ndiponso ntchito ya manja ako? 7Maloto ochuluka ndi mawu ochuluka ndi zinthu zopandapake. Kotero lemekeza Mulungu.

Chuma Nʼchopandapake

8Ngati uwona anthu osauka akuzunzika mʼdziko, ndiponso anthu ena akupsinja anzawo ndi kuwalanda ufulu wawo, usadabwe ndi zinthu zimenezi; pakuti woyangʼanira ali naye wina womuyangʼanira wamkulu, ndipo pamwamba pa awiriwa pali ena akuluakulu owaposa. 9Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.

10Aliyense amene amakonda ndalama sakhutitsidwa ndi ndalamazo;

aliyense amene amakonda chuma sakhutitsidwa ndi zimene amapeza.

Izinso ndi zopandapake.

11Chuma chikachuluka

akudya nawo chumacho amachulukanso.

Nanga mwini wake amapindulapo chiyani

kuposa kumangochiyangʼana ndi maso ake?

12Wantchito amagona tulo tabwino

ngakhale adye pangʼono kapena kudya kwambiri,

koma munthu wolemera, chuma

sichimulola kuti agone.

13Ine ndinaona choyipa chomvetsa chisoni pansi pano:

chuma chokundikidwa chikupweteka mwini wake yemwe,

14kapena chuma chowonongedwa pa nthawi yatsoka,

kotero kuti pamene wabereka mwana

alibe kanthu koti amusiyire.

15Munthu anabadwa wamaliseche kuchokera mʼmimba mwa amayi ake,

ndipo monga iye anabadwira, adzapitanso choncho.

Pa zonse zimene iye anakhetsera thukuta

palibe nʼchimodzi chomwe chimene adzatenge mʼmanja mwake.

16Izinso ndi zoyipa kwambiri:

munthu adzapita monga momwe anabwerera,

ndipo iye amapindula chiyani,

pakuti amagwira ntchito yolemetsa yopanda phindu?

17Masiku ake onse ndi odzaza ndi mdima,

kukhumudwa kwakukulu, masautso ndi nkhawa.

18Tsono ndinazindikira kuti nʼchabwino ndi choyenera kuti munthu azidya ndi kumwa, ndi kukhutitsidwa ndi ntchito yake yolemetsa imene amayigwira pansi pano pa nthawi yake yochepa imene Mulungu amamupatsa, poti ichi ndiye chake. 19Komatu pamene Mulungu apereka chuma kwa munthu aliyense ndi zinthu zina, ndi kulola kuti akondwere ndi chumacho, munthuyo alandire chumacho ndi kusangalala ndi ntchito yake, imene ndi mphatso yochokera kwa Mulungu. 20Munthu wotereyu saganizirapo za masiku a moyo wake, chifukwa Mulungu amamutanganidwitsa ndi chisangalalo cha mu mtima mwake.

Священное Писание

Размышления 5:1-19

1Подумай, прежде чем что-то сказать,

не торопись произнести слово перед Всевышним.

Всевышний на небе,

а ты на земле,

так будь же немногословен.

2И как снятся беспокойные сны при множестве забот,

так и речь глупца рождается при множестве слов.

3Когда даёшь обет Всевышнему, не замедли исполнить его. Ему не угодны глупцы; исполни то, что обещал. 4Лучше не давать обещания, чем дать и не исполнить. 5Не позволяй устам своим ввести тебя в грех. И не говори посланнику5:5 Этот посланник, скорее всего, священнослужитель, пришедший из храма за обещанным. Однако слово, стоящее в оригинале, можно перевести и как «ангел».: «Моё обещание было ошибкой». Зачем тебе, чтобы Всевышний прогневался на слова твои и уничтожил дело рук твоих? 6Пустота во множестве сновидений, как и в многословии, поэтому бойся Всевышнего!

Богатство – пусто

7Если ты увидишь, что в какой-то местности притесняют бедного и не соблюдается правосудие и справедливость, то не удивляйся этому, потому что над одним правителем стоит другой, который наблюдает за ним, а над ними есть ещё более высокое начальство. 8Но всё же лучше для страны, чтобы у неё был царь, заботящийся о земле5:8 Или: «Каждый получает прибыль от земли, и даже царь извлекает из неё свою пользу»..

9Кто любит деньги,

тому их никогда не хватает,

и кто любит богатство,

никогда не будет доволен своим доходом.

И это тоже пустое.

10Когда увеличивается имущество,

увеличивается и число нахлебников.

В чём польза его владельцу,

кроме как смотреть на него?

11Сон работника сладок,

много ли он съел или мало.

Но объевшийся богач

всё ворочается в своей кровати.

12И видел я ужасное зло под солнцем:

человек зря копил богатство –

13оно было потеряно из-за неудачной сделки,

а теперь ему нечего оставить своему сыну.

14Нагим человек выходит из утробы матери,

и каким он пришёл, таким и уходит.

Он ничего не возьмёт от труда своего,

не унесёт с собой и горсти.

15И это тоже ужасное зло:

каким человек пришёл, таким и уходит,

и какая польза ему,

что он трудится на ветер?

16Все дни его жизни проходят во тьме,

в большом разочаровании, огорчении и гневе.

17Затем я понял, что хорошо и правильно для человека есть и пить и находить наслаждение в труде своём под солнцем в течение немногих дней жизни, что дал ему Всевышний, ведь такова его доля. 18Более того, если Всевышний даёт кому-либо богатство, имущество и возможность пользоваться ими, получить свою долю и наслаждаться своим трудом, то это дар Всевышнего. 19Редко такой человек размышляет о своей жизни, потому что Всевышний наполняет радостью сердце его.