Miyambo 9 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 9:1-18

Za Nzeru ndi Uchitsiru

1Nzeru inamanga nyumba yake;

inayimika nsanamira zake zisanu ndi ziwiri.

2Inapha ziweto zake ndipo yasakaniza vinyo wake;

inasakaniza vinyo wake ndi kuyala tebulo lake.

3Nzeruyo inatuma adzakazi ake,

kuti akakhale pamwamba penipeni pa mzinda ndi kukalengeza kuti,

4“Aliyense amene ali munthu wamba, abwere kuno!”

Kwa onse opanda nzeru inkanena kuti,

5“Bwerani, dzadyeni chakudya changa

ndipo dzamweni vinyo amene ndakonza.

6Lekani zopusa zanu kuti mukhale ndi moyo;

yendani njira ya nzeru yomvetsa zinthu.”

7Aliyense amene amayesa kukonza munthu wonyoza amadziputira minyozo;

aliyense amene amadzudzula munthu woyipa amadetsa mbiri yake.

8Usadzudzule munthu wonyoza kuti angadzadane nawe;

dzudzula munthu wanzeru ndipo adzakukonda.

9Ukalangiza munthu wanzeru ndiye adzapitirira kukhala wanzeru;

ukaphunzitsa munthu wolungama ndiye adzawonjezera kuphunzira kwake.

10Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru;

kudziwa Woyerayo ndiko kukhala womvetsa bwino zinthu.

11Chifukwa cha ine nzeru, masiku ako adzachuluka,

ndipo zaka za moyo wako zidzawonjezeredwa.

12Ngati ndiwe wanzeru, nzeru yakoyo idzakupindulitsa;

ngati ndiwe wonyoza ena, udzavutika wekha.

13Uchitsiru ndi mkazi waphokoso,

wopulikira ndiponso wosadziwa zinthu.

14Iye amakhala pa mpando, pa khomo la nyumba yake,

pamalo aatali a mu mzinda,

15kuti aziyitana anthu ongodutsa,

amene akunka nayenda njira zawo.

16Amati, “Onse amene ndi anthu wamba abwere kuno,”

ndipo kwa wopanda nzeru amati,

17“Madzi akuba ndiye amatsekemera;

chakudya chodya mobisa ndi chokoma!”

18Koma amunawo sadziwa kuti akufa ali kale komweko,

ndi kuti alendo ake alowa kale mʼmanda akuya.

Luganda Contemporary Bible

Engero 9:1-18

Empagi z’Amagezi Omusanvu

19:1 Bef 2:20-22; 1Pe 2:5Amagezi gazimbye ennyumba yaago,

gagizimbidde ku mpagi musanvu.

29:2 Luk 14:16-23Gategese ennyama yaago ne wayini9:2 Wayini yatabulwangamu ebyakaloosa aka mooli, yeeyongere okuwoomerera. waago;

gategese ekijjulo.

39:3 a Nge 8:1-3 b nny 14Gatumye abawala abaweereza bakoowoolere

mu bifo ebigulumivu nti,

49:4 Nge 6:32“Buli atalina kutegeera akyameko wano!”

Eri abo abatalina magezi gabagamba nti,

59:5 Is 55:1“Mujje mulye ku mmere yange

era munywe ne ku nvinnyo gwe ntabudde.

69:6 Nge 8:35Mulekeraawo obutaba na kutegeera mubeere balamu,

era mutambulire mu kkubo ly’okumanya.”

79:7 Nge 23:9Oyo anenya omunyoomi ayolekera kuvumwa,

n’oyo abuulirira omukozi w’ebibi yeeretera kuvumibwa.

89:8 a Nge 15:12 b Zab 141:5Tonenyanga munyoomi, aleme okukukyawa, naye

nenya ow’amagezi naye anaakwagalanga.

99:9 Nge 1:5, 7Yigirizanga ow’amagezi naye aneeyongeranga okuba n’amagezi,

yigirizanga omutuukirivu, aneeyongerangako okuyiga.

109:10 Yob 28:28; Nge 1:7“Mu kutya Mukama amagezi mwe gasookera,

era n’okumanya oyo Omutukuvu Katonda, kwe kutegeera.

119:11 Nge 3:16; 10:27Ku lwange oliwangaala emyaka mingi nnyo,

era olyongerwako emyaka.

12Bw’obeera omugezi, amagezi go gakuyamba,

naye bw’onyooma amagezi weerumya wekka.”

139:13 a Nge 7:11 b Nge 5:6Omukazi omusirusiru aleekaana,

taba na mpisa era taba na magezi!

149:14 nny 3Era atuula mu mulyango gw’ennyumba ye,

ne ku ntebe mu bifo eby’ekibuga ebisinga obugulumivu,

15ng’akoowoola abo abayitawo,

ababa batambula amakubo gaabwe abali ku byabwe.

16Abagamba nti, “Buli alina okumanya okutono ajje muno.”

Era eri oyo atalina kutegeera agamba nti,

179:17 Nge 20:17“Amazzi amabbe nga gawooma!

emmere eriibwa mu kyama ng’ewooma!”

189:18 Nge 2:18; 7:26-27Naye oyo agwa mu kitimba kye tamanya nti nnyumba yakuzikirira,

era nti abagenyi be bali mu buziba obw’emagombe.