Miyambo 31 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 31:1-31

Mawu a Mfumu Lemueli

1Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:

2Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga?

Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?

3Usapereke mphamvu yako kwa akazi.

Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.

4Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu,

mafumu sayenera kumwa vinyo.

Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa

5kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko,

nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.

6Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa,

vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;

7amwe kuti ayiwale umphawi wawo

asakumbukirenso kuvutika kwawo.

8Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha.

Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.

9Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo.

Uwateteze amphawi ndi osauka.

Mathero: Mkazi Wangwiro

10Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani?

Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.

11Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira

ndipo mwamunayo sasowa phindu.

12Masiku onse a moyo wake

mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.

13Iye amafunafuna ubweya ndi thonje;

amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.

14Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda,

amakatenga chakudya chake kutali.

15Iye amadzuka kusanache kwenikweni;

ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya

ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.

16Iye amalingalira za munda ndi kuwugula;

ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.

17Iye amavala zilimbe

nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.

18Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu,

choncho nyale yake sizima usiku wonse.

19Iye amadzilukira thonje

ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.

20Iye amachitira chifundo anthu osauka

ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.

21Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu;

pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.

22Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake;

amavala zovala zabafuta ndi zapepo.

23Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda,

ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.

24Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa;

amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.

25Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake;

ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.

26Iye amayankhula mwanzeru,

amaphunzitsa anthu mwachikondi.

27Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake

ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.

28Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala;

ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,

29“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana

koma iwe umawaposa onsewa.”

30Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa;

koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.

31Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita

ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

箴言 31:1-31

利慕伊勒王的箴言

1以下是利慕伊勒王的箴言,

是他母亲给他的教诲:

2我儿,我亲生的骨肉,

我许愿得来的孩子啊,

我该怎样教导你呢?

3不要在女人身上耗废精力,

不要迷恋那些能毁灭王的人。

4利慕伊勒啊,

君王不可喝酒,

不可喝酒,

首领不宜喝烈酒,

5免得喝酒后忘记律例,

不为困苦人伸张正义。

6把烈酒给灭亡的人,

把淡酒给忧伤的人,

7让他们喝了忘掉贫穷,

不再记得自己的痛苦。

8要为不能自辩者说话,

为一切不幸的人申冤。

9你要发言,秉公审判,

为贫穷困苦者主持公道。

贤德的妻子

10谁能找到贤德之妻?

她的价值远胜过珠宝。

11她丈夫信赖她,

什么也不缺乏。

12她一生对丈夫有益无损。

13她寻找羊毛和细麻,

愉快地亲手做衣。

14她好像商船,

从远方运来粮食。

15天未亮她就起床,

为全家预备食物,

分派女仆做家事。

16她选中田地便买下来,

亲手赚钱栽种葡萄园。

17她精力充沛,

双臂有力。

18她深谙经营之道,

她的灯彻夜不熄。

19她手拿卷线杆,

手握纺线锤。

20她乐于周济穷人,

伸手帮助困苦者。

21她不因下雪而为家人担心,

因为全家都穿着朱红暖衣。

22她为自己缝制绣花毯,

用细麻和紫布做衣服。

23她丈夫在城门口与当地长老同坐,

受人尊重。

24她缝制细麻衣裳出售,

又制作腰带卖给商人。

25她充满力量和尊荣,

她以笑颜迎接未来。

26她说的话带着智慧,

她的训言充满慈爱。

27她料理一切家务,

从不偷懒吃闲饭。

28她的儿女肃立,

为她祝福,

她的丈夫也称赞她,

29说:“世上贤德的女子很多,

唯有你无与伦比。”

30艳丽是虚假的,

美貌是短暂的,

唯有敬畏耶和华的女子配得称赞。

31愿她享受自己的劳动成果,

愿她的事迹使她在城门口受称赞。