Miyambo 25 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 25:1-28

Miyambo Ina ya Solomoni

1Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.

2Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu;

ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.

3Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi,

ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.

4Chotsa zoyipa mʼsiliva

ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.

5Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu;

ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.

6Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu,

ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;

7paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,”

kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa.

Chimene wachiona ndi maso ako,

8usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu

nanga udzachita chiyani pa mapeto pake

ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?

9Kamba mlandu ndi mnansi wako,

koma osawulula chinsinsi cha munthu wina

10kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi

ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.

11Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera

ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.

12Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide

kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.

13Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola

kwa anthu amene amutuma;

iye amaziziritsa mtima bwana wake.

14Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka

ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.

15Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu,

ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.

16Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira,

kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.

17Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako

ukawirikiza kupita, udzadana naye.

18Munthu wochitira mnzake umboni wonama,

ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.

19Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto,

kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.

20Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni

kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira

kapena kuthira mchere pa chilonda.

21Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye;

ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.

22Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake,

ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.

23Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula,

chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.

24Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga

kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.

25Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali

ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.

26Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa

ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.

27Sibwino kudya uchi wambiri,

sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.

28Munthu amene samatha kudziretsa

ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

Nova Versão Internacional

Provérbios 25:1-28

Outros Provérbios de Salomão

1Estes são outros provérbios de Salomão, compilados pelos servos de Ezequias, rei de Judá:

2A glória de Deus é ocultar certas coisas;

tentar descobri-las é a glória dos reis.

3Assim como o céu é elevado e a terra é profunda,

também o coração dos reis é insondável.

4Quando se retira a escória da prata,

nesta se tem material para o25.4 Ou aí surge um vaso da parte do ourives;

5quando os ímpios são retirados da presença do rei,

a justiça firma o seu trono.

6Não se engrandeça na presença do rei

e não reivindique lugar entre os homens importantes;

7é melhor que o rei lhe diga: “Suba para cá!”,

do que ter que humilhá-lo diante de uma autoridade.

O que você viu com os olhos

8não leve precipitadamente ao tribunal,

pois o que você fará se o seu próximo o desacreditar?

9Procure resolver sua causa diretamente com o seu próximo

e não revele o segredo de outra pessoa,

10caso contrário, quem o ouvir poderá recriminá-lo,

e você jamais perderá sua má reputação.

11A palavra proferida no tempo certo

é como frutas de ouro incrustadas numa escultura25.11 Ou moldura de prata.

12Como brinco de ouro e enfeite de ouro fino

é a repreensão dada com sabedoria a quem se dispõe a ouvir.

13Como o frescor da neve na época da colheita

é o mensageiro de confiança

para aqueles que o enviam;

ele revigora o ânimo de seus senhores.

14Como nuvens e ventos sem chuva

é aquele que se gaba de presentes que não deu.

15Com muita paciência pode-se convencer a autoridade,

e a língua branda quebra até ossos25.15 Ou vence a resistência.

16Se você encontrar mel, coma apenas o suficiente,

para que não fique enjoado e vomite.

17Não faça visitas frequentes à casa do seu vizinho

para que ele não se canse de você e passe a odiá-lo.

18Como um pedaço de pau, uma espada ou uma flecha aguda

é o que dá falso testemunho contra o seu próximo.

19Como dente estragado ou pé deslocado

é a confiança no25.19 Ou do hipócrita na hora da dificuldade.

20Como tirar a própria roupa num dia de frio,

ou derramar vinagre numa ferida

é cantar com o coração entristecido.

21Se o seu inimigo tiver fome, dê-lhe de comer;

se tiver sede, dê-lhe de beber.

22Fazendo isso, você amontoará brasas vivas sobre a cabeça dele,

e o Senhor recompensará você.

23Como o vento norte traz chuva,

assim a língua fingida traz o olhar irado.

24Melhor é viver num canto sob o telhado do que repartir a casa

com uma mulher briguenta.

25Como água fresca para a garganta sedenta

é a boa notícia que chega de uma terra distante.

26Como fonte contaminada ou nascente poluída,

assim é o justo que fraqueja diante do ímpio.

27Comer mel demais não é bom,

nem é honroso buscar a própria honra.

28Como a cidade com seus muros derrubados,

assim é quem não sabe dominar-se.