Miyambo 23 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 23:1-35

1Ngati ukhala pansi kuti udye pamodzi ndi wolamulira,

uyangʼane bwino zimene zili pamaso pako,

2ngati ndiwe munthu wadyera

udziletse kuti usaonetse dyera lakolo.

3Usasirire zakudya zake,

pakuti zimenezo ndi zakudya zachinyengo.

4Usadzitopetse wekha ndi kufuna chuma,

ukhale ndi nzeru ya kudziretsa.

5Ukangoti wachipeza chumacho uwona posachedwa kuti palibepo.

Chumacho chimachita ngati chamera mapiko mwadzidzidzi

ndi kuwuluka kunka kumwamba ngati chiwombankhanga.

6Usadye chakudya cha munthu waumbombo,

usalakalake zakudya zake zokoma;

7paja iye ndi munthu amene

nthawi zonse amaganizira za mtengo wake

ngakhale amati kwa iwe, “Idya ndi kumwa,”

koma sakondweretsedwa nawe.

8Udzasanza zimene wadyazo

ndipo mawu ako woyamikira adzapita pachabe.

9Usayankhule munthu wopusa akumva,

pakuti adzanyoza mawu ako anzeru.

10Usasunthe mwala wa mʼmalire akalekale

kapena kulowerera mʼminda ya ana amasiye,

11paja Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;

iye adzawateteza pa milandu yawo kutsutsana nawe.

12Mtima wako uzikhala pa malangizo

ndipo makutu ako azimvetsera mawu a chidziwitso.

13Usaleke kumulangiza mwana;

ngati umulanga ndi chikwapu sadzafa.

14Ukamukwapula ndi tsatsa

udzapulumutsa moyo wake.

15Mwana wanga, ngati mtima wako ukhala wanzeru,

inenso mtima wanga udzakondwera.

16Mtima wanga udzakondwera

pamene ndidzakumva ukuyankhula zolungama.

17Mtima wako usachite nsanje ndi anthu ochimwa,

koma uziopa Yehova tsiku ndi tsiku.

18Ndithu za mʼtsogolo zilipo

ndipo chiyembekezo chakocho sichidzalephereka.

19Tamvera mwana wanga, ndipo ukhale wanzeru,

mtima wako uwuyendetse mʼnjira yabwino.

20Usakhale pakati pa anthu amene amaledzera

kapena pakati pa anthu amene amadya nyama mwadyera.

21Paja anthu oledzera ndi adyera amadzakhala amphawi

ndipo aulesi adzavala sanza.

22Mvera abambo ako amene anakubala,

usanyoze amayi ako pamene akalamba.

23Gula choonadi ndipo usachigulitse;

ugulenso nzeru, mwambo ndiponso kumvetsa zinthu bwino.

24Abambo a munthu wolungama ali ndi chimwemwe chachikulu;

Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.

25Abambo ndi amayi ako asangalale;

amene anakubereka akondwere!

26Mwana wanga, undikhulupirire

ndipo maso ako apenyetsetse njira zanga.

27Paja mkazi wachiwerewere ali ngati dzenje lozama;

ndipo mkazi woyendayenda ali ngati chitsime chopapatiza.

28Amabisala ngati mbala yachifwamba,

ndipo amuna amakhala osakhulupirika chifukwa cha iyeyu.

29Ndani ali ndi tsoka? Ndani ali ndi chisoni?

Ndani ali pa mkangano? Ndani ali ndi madandawulo?

Ndani ali ndi zipsera zosadziwika uko zachokera? Ndani ali ndi maso ofiira?

30Ndi amene amakhalitsa pa mowa,

amene amapita nalawa vinyo osakanizidwa.

31Usatengeke mtima ndi kufiira kwa vinyo,

pamene akuwira mʼchikho

pamene akumweka bwino!

32Potsiriza pake amaluma ngati njoka,

ndipo amajompha ngati mphiri.

33Maso ako adzaona zinthu zachilendo

ndipo maganizo ndi mawu ako adzakhala osokonekera.

34Udzakhala ngati munthu amene ali gone pakati pa nyanja,

kapena ngati munthu wogona pa msonga ya mlongoti ya ngalawa.

35Iwe udzanena kuti, “Anandimenya, koma sindinapwetekedwe!

Andimenya koma sindinamve kanthu!

Kodi ndidzuka nthawi yanji?

Ndiye ndifunefunenso vinyo wina.”

Hoffnung für Alle

Sprüche 23:1-35

6.

1Wenn du mit einem mächtigen Herrn am Tisch sitzt, dann bedenke, wen du vor dir hast! 2Beherrsche dich, selbst wenn du heißhungrig bist! 3Stürze dich nicht auf seine Leckerbissen, denn wenn du meinst, sie seien dir zu Ehren aufgetischt, täuschst du dich selbst23,3 Wörtlich: denn sie sind eine trügerische Speise..

7.

4Versuche nicht, mit aller Gewalt reich zu werden; sei klug genug, darauf zu verzichten! 5Schneller, als ein Adler fliegen kann, ist dein Geld plötzlich weg – wie gewonnen, so zerronnen!

8.

6Iss nicht mit einem Geizhals, sei nicht begierig nach seinen Leckerbissen, 7denn er ist falsch und berechnend. »Iss und trink nur!«, fordert er dich auf, aber in Wirklichkeit gönnt er dir nichts. 8Sobald du es merkst, kommt dir das Essen wieder hoch; dann waren all deine freundlichen Worte umsonst!

9.

9Versuche nicht, einem Dummkopf etwas zu erklären; er wird deinen guten Rat ohnehin nur verachten!

10.

10Versetze keine alten Grenzsteine, mache den Waisen niemals ihr Eigentum streitig! 11Denn in Gott haben sie einen starken Beschützer, er selbst wird gegen dich auftreten und ihnen Recht verschaffen.

11.

12Sei offen für Ermahnung und hör genau zu, wenn du etwas lernen kannst!

12.

13Erspare deinem Kind die harte Strafe nicht! Ein paar Hiebe werden es nicht umbringen. 14Im Gegenteil: Du rettest sein Leben damit!

13.

15Mein Sohn, wenn du weise bist, dann freue ich mich darüber. 16Wenn deine Worte zeigen, was Gutes in dir steckt, bin ich überglücklich.

14.

17Beneide nicht die Menschen, die Schuld auf sich laden; sondern setze stets alles daran, dem Herrn mit Ehrfurcht zu begegnen! 18Dann hast du eine sichere Zukunft, und deine Hoffnung wird nicht enttäuscht.

15.

19Hör gut zu, mein Sohn, und werde weise! Bemühe dich, auf dem rechten Weg zu bleiben! 20Halte dich fern von den Weinsäufern und maßlosen Schlemmern! 21Auf sie wartet die Armut; denn wer bloß isst, trinkt und schläft, hat bald nichts als Lumpen am Leib.

16.

22Hör auf deinen Vater und deine Mutter, denn sie haben dir das Leben geschenkt! Verachte sie auch dann nicht, wenn sie alt geworden sind!

23Bemühe dich um Wahrheit, egal was es kostet. Wenn du Weisheit, Selbstbeherrschung und Einsicht erworben hast, dann gib sie nie wieder auf!

24Der Vater eines zuverlässigen Sohnes hat allen Grund zur Freude. Wie froh macht doch ein kluger Sohn! 25Darum sorge dafür, dass deine Eltern stolz auf dich sind. Deine Mutter, die dich geboren hat, soll sich glücklich schätzen!

17.

26Mein Sohn, vertraue dich mir an und nimm dir mein Leben zum Vorbild! 27Hüte dich vor Huren und Ehebrecherinnen, denn sie sind so gefährlich wie ein tiefer Brunnen – schon mancher hat sich durch sie in den Tod gestürzt. 28Wie Räuber lauern sie auf neue Opfer und verführen viele zur Untreue.

18.

29Bei wem sieht man Kummer und Klage? Bei wem Streit und Gejammer? Wer hat Wunden durch grundlose Schlägereien, wer hat trübe Augen? 30Wer noch spät beim Wein sitzt und jede neue Sorte ausprobiert. 31Lass dich nicht vom Wein verlocken, wenn er so rötlich schimmert, wenn er im Glas funkelt und so glatt die Kehle hinuntergleitet! 32Denn zuletzt wirkt er wie der Biss einer giftigen Schlange. 33Deine Augen sehen seltsame Dinge, deine Gedanken und Gefühle wirbeln durcheinander. 34Es geht dir wie einem Seekranken auf hoher See – du fühlst dich wie im Mastkorb eines schaukelnden Schiffes. 35»Man muss mich geschlagen haben«, sagst du, »aber es hat mir nicht wehgetan; ich bin verprügelt worden, aber ich habe nichts davon gemerkt! Wann wache ich endlich aus meinem Rausch auf? Ich brauche wieder ein Glas Wein!«