Miyambo 2 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 2:1-22

Ubwino Wanzeru

1Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga

ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,

2ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru

ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;

3ngati upempha kuti uzindikire zinthu

inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,

4ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva

ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,

5ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova;

ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.

6Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru,

ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.

7Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo.

Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,

8pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama.

Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.

9Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo,

kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.

10Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako,

kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.

11Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga;

kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.

12Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa,

kwa anthu amabodza,

13amene amasiya njira zolungama

namayenda mʼnjira zamdima,

14amene amakondwera pochita zoyipa

namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.

15Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota,

ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.

16Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo;

kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,

17amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake

ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.

18Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa;

njira zake zimamufikitsa ku manda.

19Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera

kapena kupezanso njira zamoyo.

20Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino,

uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.

21Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko

ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;

22Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo,

ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Мудрые изречения 2:1-22

Достоинства мудрости

1Сын мой, если ты примешь мои слова

и повеления мои сохранишь в сердце,

2обратив своё ухо к мудрости

и склонив своё сердце к пониманию,

3если будешь взывать о разуме

и призывать понимание,

4если будешь искать его, как серебра,

и разыскивать, словно клад,

5то поймёшь, что такое страх перед Вечным,

и обретёшь познание Всевышнего.

6Потому что Вечный даёт мудрость,

и из уст Его – знание и понимание.

7Он бережёт победу для праведных;

щит Он для живущих непорочно.

8Он хранит стези справедливых

и оберегает путь верных Ему.

9Тогда ты поймёшь, что такое праведность,

справедливость и честность – всякий добрый путь.

10Мудрость войдёт в твоё сердце,

и знание будет приятно твоей душе.

11Рассудительность защитит тебя,

и понимание тебя сохранит.

12Мудрость спасёт тебя от пути злодеев,

от тех, чьи слова превратны,

13кто оставляет стези прямые,

чтобы ходить по путям тьмы;

14от тех, кто веселится, делая зло,

и радуется извращённости зла,

15чьи дороги кривы,

и кто плутает по своим путям.

16Мудрость спасёт тебя от чужой жены,

от жены другого с её обольщающими словами,

17которая оставила того, кто был ей супругом в юности,

и забыла союз, что заключила пред Всевышним.

18Дом её ведёт к смерти,

и пути её – к духам умерших.

19Никто из вошедших к ней не возвращается

и уже не ступит на путь жизни.

20Поэтому ходи по пути добрых

и держись дороги праведников,

21ведь праведные будут жить на земле,

и непорочные останутся на ней;

22а нечестивые будут истреблены с земли,

и неверные будут искоренены.