Miyambo 18 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 18:1-24

1Munthu wokonda kukhala yekha amafunafuna zomukomera yekha;

iye amatsutsana ndi malangizo onse anzeru.

2Chitsiru chilibe chidwi chomvetsa zinthu,

koma chimakondwera ndi kuyankhula maganizo ake okha.

3Kuyipa mtima kukabwera, manyozonso amabwera.

Manyazi amabwera pamodzi ndi kunyozeka.

4Mawu a munthu ali ngati madzi akuya,

kasupe wa nzeru ndiye mtsinje wotumphuka.

5Si kwabwino kukondera munthu woyipa pa milandu;

kapena kupondereza munthu wosalakwa.

6Mawu a chitsiru amautsa mkangano;

pakamwa pake pamayitana mkwapulo.

7Pakamwa pa chitsiru ndipo pamabweretsa chiwonongeko chake,

ndipo milomo yake ili ngati msampha wa moyo wake.

8Mawu a miseche ali ngati chakudya chokoma;

amalowa mʼmimba mwa munthu.

9Munthu waulesi pa ntchito yake

ali pachibale ndi munthu amene amawononga zinthu.

10Dzina la Yehova lili ngati nsanja yolimba;

wolungama amathawiramo napulumuka.

11Chuma cha anthu olemera chili ngati mzinda wake wolimba;

chili ngati khoma lalitali limene amaganiza kuti limutchinjiriza.

12Chiwonongeko chisanafike, mtima wa munthu umakhala wonyada,

koma ulemu umatsatira kudzichepetsa.

13Ukayankha usanamvetse bwino nkhani,

umenewo ndi uchitsiru ndipo umachita manyazi.

14Mtima wa munthu utha kupirira pa matenda,

koma munthu akataya mtima ndani angathe kumulimbitsanso.

15Munthu wanzeru amawonjezera nzeru zina;

amafunafuna kudziwa bwino zinthu.

16Mphatso ya munthu imamutsekulira njira

yomufikitsa pamaso pa anthu akuluakulu.

17Amene amayamba kufotokoza mlandu wake amaoneka ngati wolungama ndiye

mpaka mnzake atabwera ndi kumufunsa bwino.

18Kuchita maere kumathetsa mikangano;

amalekanitsa okangana amphamvu.

19Mʼbale amene wamuthandiza amakhala ngati mzinda wolimba,

koma kukangana naye kumatsekereza thandizo.

20Munthu amapeza bwino malingana ndi zoyankhula zake.

Adzakhuta ndi zipatso za pakamwa pake.

21Mawu ako angathe kukuphetsa kapena kukukhalitsa moyo.

Wokonda kuyankhulayankhula adzadya zipatso zake.

22Wapeza mkazi wapeza chinthu chabwino

ndipo Yehova amamukomera mtima.

23Munthu wosauka amapempha

koma munthu wolemera amayankha mwaukali.

24Pali abwenzi amene chibwenzi chawo nʼchapamaso,

koma pali bwenzi limene limakukangamira kuposa mʼbale wako.

La Bible du Semeur

Proverbes 18:1-24

1L’original suit son bon plaisir :

il s’insurgera contre tout ce qui est raisonnable.

2L’insensé n’aime pas réfléchir,

il ne demande qu’à faire étalage de son opinion.

3Le méchant apporte avec lui le mépris :

une action déshonorante est suivie de l’opprobre.

4Les paroles humaines sont comme des eaux profondes ;

la source de la sagesse est un torrent qui déborde18.4 Ce verset semble opposer notre répugnance à nous livrer (voir le secret des « eaux profondes » en 20.5) à la franchise vivifiante des sages..

5Il n’est pas bien de favoriser le méchant

et de léser le juste dans le jugement.

6Les propos de l’insensé suscitent des querelles,

et ses discours lui attirent les coups.

7La bouche de l’insensé cause sa ruine,

et ses lèvres sont un piège pour sa vie.

8Les médisances sont comme des friandises :

elles descendent jusqu’au tréfonds de l’être.

9Qui se relâche dans son travail

est frère de celui qui détruit.

10L’Eternel est comme un donjon bien fortifié :

le juste y accourt et il y est en sécurité.

11La fortune du riche lui tient lieu de place forte,

il s’imagine qu’ils sont un rempart inaccessible.

12Quand l’orgueil remplit le cœur d’un homme, sa ruine est proche.

Avant d’être honoré, il faut savoir être humble18.12 Voir 15.33..

13Qui répond avant d’avoir écouté

manifeste sa sottise et se couvre de confusion.

14Un bon moral permet de supporter la maladie,

mais si le moral est abattu, qui le relèvera ?

15L’homme intelligent acquiert la connaissance,

et l’oreille des sages est tendue vers elle.

16Les cadeaux ouvrent les chemins

et font arriver jusqu’en présence des gens importants18.16 Voir 17.8..

17Qui plaide sa cause en premier paraît toujours avoir raison,

vient la partie adverse, et l’on examine ce qu’il a dit.

18Le sort met fin aux contestations

et tranche même entre des puissants.

19Un frère que l’on a offensé est plus inaccessible qu’une ville fortifiée,

et des dissensions sont comme les verrous d’un palais.

20Chacun goûtera à satiété les fruits de ses paroles

et se rassasiera de ce que ses lèvres ont produit.

21La mort et la vie sont au pouvoir de la langue :

qui aime se répandre en paroles mangera les fruits qu’elles auront produits.

22Qui trouve une épouse trouve le bonheur :

c’est une faveur que l’Eternel lui a accordée.

23Le pauvre parle en suppliant,

mais le riche répond durement.

24Qui a beaucoup de compagnons les a pour son malheur,

mais un véritable ami est plus attaché qu’un frère.