Miyambo 11 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 11:1-31

1Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa,

koma amakondwera ndi muyeso woyenera.

2Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi,

koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.

3Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera,

koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.

4Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

5Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo,

koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.

6Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa,

koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.

7Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso.

Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.

8Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto,

koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.

9Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake,

koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.

10Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera,

ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.

11Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima,

koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.

12Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru,

koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.

13Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi;

koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.

14Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa;

koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.

15Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto,

koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.

16Mkazi wodekha amalandira ulemu,

koma amuna ankhanza amangopata chuma.

17Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino

koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.

18Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu,

koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.

19Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo,

koma wothamangira zoyipa adzafa.

20Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota

koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.

21Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa,

koma anthu olungama adzapulumuka.

22Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba,

ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.

23Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha,

koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.

24Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe;

wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.

25Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera;

iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.

26Anthu amatemberera womana anzake chakudya,

koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.

27Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo,

koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.

28Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota,

koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.

29Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto,

ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.

30Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo,

ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.

31Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi,

kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

箴言 11:1-31

1耶和华憎恶骗人的天平,

喜爱公平的砝码。

2傲慢带来羞辱,

谦卑者有智慧。

3正直人靠诚实引导,

奸诈者被奸诈毁灭。

4在降怒之日,财富毫无益处,

唯有公义能救人免于死亡。

5纯全人行义走坦途,

恶人作恶致沉沦。

6正直人被义行所救,

奸诈者被私欲所掳。

7恶人一死,他的希望就破灭,

他对财势的冀望转眼成空。

8义人脱离患难,

恶人落入苦难。

9不敬虔的张口败坏邻舍,

义人却因知识获得拯救。

10义人亨通,全城快乐;

恶人灭亡,人人欢呼。

11城因正直人的祝福而兴盛,

因恶人的口舌而倾覆。

12无知者轻视邻舍,

明哲人保持缄默。

13嚼舌者泄露秘密,

忠信者守口如瓶。

14缺乏智谋,国必败亡;

谋士众多,战无不胜。

15为他人作保,必受亏损;

厌恶当保人,得享平安。

16贤淑的女子得到尊荣,

残暴的男子得到资财。

17仁慈的人造福自己,

残酷的人惹祸上身。

18恶人赚来的转眼成空,

播种公义的必获奖赏。

19坚持行义,必得生命;

追逐罪恶,终必灭亡。

20心术不正的人令耶和华憎恶,

纯全无过的人蒙耶和华喜爱。

21恶人终必落入法网,

义人的子孙必得拯救。

22女子貌美无内涵,

如同猪鼻挂金环。

23义人的愿望结出善果,

恶人的希望招致烈怒。

24有人乐善好施,反倒越来越富;

有人一毛不拔,反而越来越穷。

25慷慨好施的必得昌盛,

恩待他人的必蒙恩待。

26囤粮不卖,惹人咒诅;

乐意卖粮,必蒙祝福。

27寻求良善得恩惠,

追求罪恶遭祸患。

28倚仗财势者必衰败,

义人必兴旺如绿叶。

29祸害自家,必一无所有,

愚人必做智者的仆役。

30义人结果如生命之树,

智者深得人心。

31看啊!义人在世上尚且遭报11:31 义人在世上尚且遭报”七十士译本为“义人尚且难以得救”,参见彼得前书4:18

更何况罪人和恶人呢?