Miyambo 10 – CCL & HTB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 10:1-32

Miyambo ya Solomoni

1Miyambo ya Solomoni:

Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,

koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.

2Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

3Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala;

koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.

4Wochita zinthu mwaulesi amasauka,

koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.

5Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru,

koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.

6Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.

7Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso,

koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.

8Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo,

koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.

9Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka;

koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.

10Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto,

koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.

11Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.

12Udani umawutsa mikangano,

koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

13Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu,

koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.

14Anzeru amasunga chidziwitso

koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.

15Chuma cha munthu wolemera

ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.

16Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama,

koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.

17Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo,

koma wonyoza chidzudzulo amasochera.

18Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama,

ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.

19Mawu akachuluka zolakwa sizisowa,

koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.

20Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri,

koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.

21Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri;

koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.

22Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma,

ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.

23Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa,

koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.

24Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira;

chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.

25Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa,

koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.

26Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso,

ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.

27Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo;

koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.

28Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe,

koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.

29Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino,

koma wochita zoyipa adzawonongeka.

30Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake

koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.

31Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru,

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula,

koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

Het Boek

Spreuken 10:1-32

1De spreuken van Salomo.

Een verstandige zoon is een genoegen voor zijn ouders, maar een dwaze zoon doet hun verdriet.

2Oneerlijk verkregen vermogen levert niets op, maar zijn oprechtheid redt een mens van de dood.

3De Here zorgt dat een rechtvaardig mens geen honger lijdt, maar de goddeloze neemt Hij alles af.

4Iemand die zich niet ten volle inzet, wordt arm. Maar wie zich inspant, wordt rijk.

5Wie in de zomer zijn oogst binnenhaalt, is een verstandige zoon. Maar de zoon die in de oogsttijd slaapt, maakt zichzelf te schande.

6Rechtvaardige mensen worden gezegend, goddelozen worden door hun eigen onrecht tot zwijgen gebracht.

7De nagedachtenis van een rechtvaardige brengt zegen voort, maar van de naam van de goddeloze blijft niets over.

8Een wijs mens neemt Gods geboden aan, maar de dwaze prater loopt in de val.

9Wie oprecht leeft, leidt een zeker bestaan, maar wie verkeerde wegen bewandelt, wordt ontdekt en ontmaskerd.

10Een slinkse boosdoener bezorgt anderen verdriet en een dwaze prater loopt zijn ondergang tegemoet.

11De woorden van een rechtvaardige zijn een bemoediging, maar goddelozen worden door hun eigen onrecht tot zwijgen gebracht.

12Haat leidt tot onrust en ruzies, de liefde bedekt echter al het menselijk falen.

13Op de lippen van een verstandig mens ligt wijsheid, de onverstandige verdient alleen maar straf.

14Een wijs mens verzamelt steeds meer inzicht, maar de woorden van een dwaas kunnen voortdurend onheil aanrichten.

15De rijke vertrouwt volledig op zijn bezit, terwijl arme mensen niets hebben.

16Alles wat een rechtvaardige doet, bezorgt hem voordeel. Wat de goddeloze verdient, leidt tot zijn ondergang.

17Wie wijze lessen ter harte neemt, loopt op de weg van het leven, maar wie ze in de wind slaat, brengt anderen op een dwaalspoor.

18Wie heimelijk zijn naaste haat, is schijnheilig in zijn spreken. Wie roddelt, is een zot.

19Iemand die zijn tong niet in bedwang heeft, zondigt met zijn woorden. Iemand die nadenkt voor hij spreekt, is bedachtzaam en verstandig.

20De woorden van een rechtvaardige zijn goud waard, die van een goddeloze zijn waardeloos.

21Van de woorden van een rechtvaardig mens kunnen velen leren, maar dwazen sterven door gebrek aan inzicht.

22Alleen de zegen van de Here maakt een mens rijk, niet zijn eigen zwoegen.

23Zoals een boosdoener genoegen heeft in misdaden, verheugt een verstandig mens zich in wijsheid.

24Waar de goddeloze bang voor is, gebeurt nog ook. Maar God geeft de rechtvaardigen waar zij naar verlangen.

25Verzwolgen door een wervelwind zal de goddeloze verdwijnen, de rechtvaardige staat echter op een sterk fundament.

26Wat azijn is voor de mond en scherpe rook voor de ogen, is een lui mens voor zijn werkgever.

27Eerbiedig ontzag voor de Here verlengt uw leven, terwijl de goddelozen jong zullen sterven.

28De hoop van de rechtvaardigen gaat gepaard met blijdschap, maar de toekomstverwachting van de goddelozen valt in duigen.

29De oprechte mens put kracht uit wat de Here doet, maar voor de boosdoener leidt dat tot zijn ondergang.

30De rechtvaardige mens zal tot in eeuwigheid niet aan het wankelen worden gebracht, maar van de goddelozen blijft niets over.

31De woorden van een rechtvaardige zijn vol wijsheid, maar de leugenaar wordt vernietigd.

32De rechtvaardige zal het goede zeggen, maar een goddeloze spreekt alleen slechtheid.