Mika 4 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 4:1-13

Phiri la Yehova

1Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa

kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse.

Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,

ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.

2Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova,

ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.

Iye adzatiphunzitsa njira zake,

ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”

Malangizo adzachokera ku Ziyoni,

mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.

3Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri

ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe.

Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu

ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.

Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,

kapena kuphunziranso za nkhondo.

4Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa

ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu,

ndipo palibe amene adzawachititse mantha,

pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.

5Mitundu yonse ya anthu

itha kutsatira milungu yawo;

ife tidzayenda mʼnjira za Yehova

Mulungu wathu mpaka muyaya.

Cholinga cha Yehova

6“Tsiku limenelo, Yehova akuti,

“ndidzasonkhanitsa olumala;

ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa

ndiponso amene ndinawalanga.

7Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala.

Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu.

Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova

kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.

8Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga,

iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni,

ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe;

ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”

9Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula,

kodi ulibe mfumu?

Kodi phungu wako wawonongedwa,

kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?

10Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,

ngati mayi pa nthawi yake yobereka,

pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda

ndi kugona kunja kwa mzindawo.

Udzapita ku Babuloni;

kumeneko udzapulumutsidwa,

kumeneko Yehova adzakuwombola

mʼmanja mwa adani ako.

11Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu

yasonkhana kulimbana nawe.

Iwo akuti, “Tiyeni timudetse,

maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”

12Koma iwo sakudziwa

maganizo a Yehova;

iwo sakuzindikira cholinga chake,

Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.

13“Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,

pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo;

ndidzakupatsa ziboda zamkuwa

ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.”

Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova,

chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.

Hoffnung für Alle

Micha 4:1-14

Gott verspricht ein Reich des Friedens

(Kapitel 4–5)

Jerusalem, der Mittelpunkt eines neuen Reiches

1Am Ende der Zeit wird der Berg, auf dem der Tempel des Herrn steht, alle anderen Berge und Hügel weit überragen. Menschen aller Nationen strömen dann herbei. 2Viele Völker ziehen los und rufen einander zu: »Kommt, wir wollen auf den Berg des Herrn steigen, zum Tempel des Gottes Israels! Dort wird er uns seinen Weg zeigen, und wir werden lernen, so zu leben, wie er es will.« Denn vom Berg Zion aus wird der Herr seine Weisungen geben, dort in Jerusalem wird er der ganzen Welt seinen Willen verkünden. 3Gott selbst schlichtet den Streit zwischen den Völkern, und den mächtigen Nationen in weiter Ferne spricht er Recht. Dann schmieden sie ihre Schwerter zu Pflugscharen um und ihre Speere zu Winzermessern. Kein Volk wird mehr das andere angreifen; niemand lernt mehr, Krieg zu führen.4,3 Vgl. Jesaja 2,2‒4. 4Jeder kann ungestört unter seinem Feigenbaum und in seinem Weingarten sitzen, ohne dass ihn jemand aufschreckt. Das verspricht der Herr, der allmächtige Gott!

5Noch dient jedes Volk seinem eigenen Gott, wir Israeliten aber folgen für immer dem Herrn, unserem Gott.

6So spricht der Herr: »Es kommt der Tag, da werde ich mein Volk, das ich so schwer bestraft habe, wieder in seine Heimat bringen, so wie ein Hirte seine Schafe zurückholt, die vertrieben und verletzt wurden. 7Ja, ich sorge dafür, dass die Verletzten überleben und die Schwachen wieder zu einem mächtigen Volk werden! Dann werde ich, der Herr, ihr König sein und für alle Zeiten auf dem Berg Zion herrschen. 8Du Festung auf dem Hügel von Jerusalem, in dir wird einst wieder ein König wohnen, so wie es früher war; von dir aus wird er wie ein Hirte über das Volk wachen.«

Noch ist Jerusalem bedroht

9Warum schreist du so laut, Jerusalem? Ist denn kein König mehr in der Stadt? Sind etwa alle deine Ratgeber umgekommen? Warum windest du dich vor Schmerzen wie eine Frau in den Wehen?

10Ja, du hast allen Grund zu schreien und dich vor Schmerzen zu krümmen! Denn du wirst aus deinen schützenden Mauern vertrieben und musst draußen auf den Feldern hausen; bis nach Babylon wird man dich verschleppen. Dort wirst du schließlich Rettung finden, dort wird dich der Herr aus der Gewalt deiner Feinde erlösen.

11Doch jetzt, Jerusalem, haben dich Soldaten aus vielen Völkern umzingelt. »Lasst uns die Stadt auf dem Berg Zion entweihen und uns an ihrem Untergang weiden!«, rufen sie einander zu. 12Aber sie ahnen ja nicht, was der Herr vorhat: Er will sie hier versammeln, wie man Garben zum Dreschen bereitlegt.

13Gott befiehlt: »Komm, Jerusalem, drisch auf sie ein! Ich mache dich so stark wie einen Stier mit Hörnern aus Eisen und Hufen aus Bronze. Du wirst die vielen Völker zermalmen und wirst alles, was sie auf ihren Raubzügen erbeutet haben, dann mir weihen. Ja, alle ihre Schätze sollen einmal mir, dem Herrn der ganzen Welt, gehören!«

Hoffnung auf den Befreier Israels

14Ritzt euch vor Trauer die Haut blutig, ihr Menschen in der belagerten Stadt! Feindliche Soldaten werden euch einkesseln und dem Herrscher Israels mit dem Stock ins Gesicht schlagen.