Mika 1 – CCL & NIVUK

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 1:1-16

1Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.

2Tamverani, inu anthu a mitundu yonse,

mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo,

pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani,

Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.

Chiweruzo cha Samariya ndi Yerusalemu

3Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake;

Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.

4Mapiri akusungunuka pansi pake,

ndipo zigwa zikugawikana

ngati phula pa moto,

ngati madzi ochokera mʼphiri.

5Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo,

chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli.

Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani?

Kodi si Samariya?

Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati?

Kodi si Yerusalemu?

6“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja,

malo odzalamo mphesa.

Miyala yake ndidzayitaya ku chigwa

ndipo ndidzafukula maziko ake.

7Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya;

mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto;

ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake.

Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere,

mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”

Kulira ndi Kumva Chisoni

8Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni;

ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche.

Ndidzafuwula ngati nkhandwe

ndi kulira ngati kadzidzi.

9Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika;

chafika ku Yuda.

Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga,

mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.

10Musanene zimenezi ku Gati;

musalire nʼkomwe.

Mugubuduzike mu fumbi

ku Beti-Leafura.

11Inu anthu okhala ku Safiro,

muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi.

Iwo amene akukhala ku Zanaani

sadzatuluka.

Beti-Ezeli akulira mwachisoni;

chitetezo chake chakuchokerani.

12Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu,

akuyembekezera thandizo,

chifukwa Yehova wabweretsa tsoka,

lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.

13Inu anthu okhala ku Lakisi

mangani akavalo ku magaleta.

Inu amene munayamba kuchimwitsa

mwana wamkazi wa Ziyoni,

pakuti zolakwa za Israeli

zinapezeka pakati panu.

14Chifukwa chake perekani mphatso zolawirana

ndi a ku Moreseti Gati.

Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunama

kwa mafumu a Israeli.

15Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu

okhala mu Maresa.

Ulemerero wa Israeli udzafika

ku Adulamu.

16Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukulirira

ana anu amene mumawakonda;

mudzichititse dazi ngati dembo,

pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.

New International Version – UK

Micah 1:1-16

1The word of the Lord that came to Micah of Moresheth during the reigns of Jotham, Ahaz and Hezekiah, kings of Judah – the vision he saw concerning Samaria and Jerusalem.

2Hear, you peoples, all of you,

listen, earth and all who live in it,

that the Sovereign Lord may bear witness against you,

the Lord from his holy temple.

Judgment against Samaria and Jerusalem

3Look! The Lord is coming from his dwelling-place;

he comes down and treads on the heights of the earth.

4The mountains melt beneath him

and the valleys split apart,

like wax before the fire,

like water rushing down a slope.

5All this is because of Jacob’s transgression,

because of the sins of the people of Israel.

What is Jacob’s transgression?

Is it not Samaria?

What is Judah’s high place?

Is it not Jerusalem?

6‘Therefore I will make Samaria a heap of rubble,

a place for planting vineyards.

I will pour her stones into the valley

and lay bare her foundations.

7All her idols will be broken to pieces;

all her temple gifts will be burned with fire;

I will destroy all her images.

Since she gathered her gifts from the wages of prostitutes,

as the wages of prostitutes they will again be used.’

Weeping and mourning

8Because of this I will weep and wail;

I will go about barefoot and naked.

I will howl like a jackal

and moan like an owl.

9For Samaria’s plague is incurable;

it has spread to Judah.

It has reached the very gate of my people,

even to Jerusalem itself.

10Tell it not in Gath1:10 Gath sounds like the Hebrew for tell.;

weep not at all.

In Beth Ophrah1:10 Beth Ophrah means house of dust.

roll in the dust.

11Pass by naked and in shame,

you who live in Shaphir.1:11 Shaphir means pleasant.

Those who live in Zaanan1:11 Zaanan sounds like the Hebrew for come out.

will not come out.

Beth Ezel is in mourning;

it no longer protects you.

12Those who live in Maroth1:12 Maroth sounds like the Hebrew for bitter. writhe in pain,

waiting for relief,

because disaster has come from the Lord,

even to the gate of Jerusalem.

13You who live in Lachish,

harness fast horses to the chariot.

You are where the sin of Daughter Zion began,

for the transgressions of Israel were found in you.

14Therefore you will give parting gifts

to Moresheth Gath.

The town of Akzib1:14 Akzib means deception. will prove deceptive

to the kings of Israel.

15I will bring a conqueror against you

who live in Mareshah.1:15 Mareshah sounds like the Hebrew for conqueror.

The nobles of Israel

will flee to Adullam.

16Shave your head in mourning

for the children in whom you delight;

make yourself as bald as the vulture,

for they will go from you into exile.