Mateyu 6 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 6:1-34

Zopereka Zachifundo

1“Samalani kuti musachite ntchito zanu zolungama pamaso pa anthu kuti akuoneni. Popeza ngati mutero simudzalandira mphotho yochokera kwa Atate anu akumwamba.

2“Pamene mupereka zachifundo, musachite modzionetsera monga amachita achiphamaso mʼmasunagoge ndi pa misewu kuti atamidwe ndi anthu. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwowo alandiriratu mphotho yawo yonse. 3Koma pamene mupereka zachifundo, dzanja lanu lamanzere lisadziwe chimene dzanja lanu lamanja likuchita, 4kotero kuti kupereka kwanu kukhale mwachinsinsi. Ndipo Atate anu amene amaona zochitika mwachinsinsi, adzakupatsani mphotho.

Za Kupemphera

5“Pamene mupemphera, musakhale ngati achiphamaso, chifukwa iwo amakonda kupemphera choyimirira mʼmasunagoge ndi pa mphambano za mʼmisewu kuti anthu awaone. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwo alandiriratu mphotho yawo yonse. 6Koma pamene mupemphera, lowani mʼchipinda chanu chamʼkati, ndi kutseka chitseko ndipo mupemphere kwa Atate anu amene saoneka. Ndipo Atate anu, amene amaona zochitika mseri, adzakupatsani mphotho. 7Ndipo pamene mukupemphera, musamabwerezabwereza monga akunja, pakuti iwo amaganiza kuti adzamveka chifukwa chochulutsa mawu. 8Musakhale ngati iwo chifukwa Atate anu amadziwa zimene musowa musanapemphe.

9“Chifukwa chake pempherani motere:

“ ‘Atate athu akumwamba,

dzina lanu lilemekezedwe,

10Ufumu wanu ubwere,

chifuniro chanu chichitike

pansi pano monga kumwamba.

11Mutipatse chakudya chathu chalero.

12Mutikhululukire mangawa athu,

monga ifenso tawakhululukira amangawa athu.

13Ndipo musatitengere kokatiyesa;

koma mutipulumutse kwa woyipayo.’

14Ngati inu mukhululukira anthu pamene akuchimwirani, Atate anu akumwamba adzakukhululukirani. 15Koma ngati inu simukhululukira anthu zolakwa zawo, Atate anunso sadzakukhululukirani machimo anu.

Kusala Kudya

16“Pamene mukusala kudya, musaonetse nkhope yachisoni monga achita achiphamaso, pakuti iwo amasintha nkhope zawo kuonetsa anthu kuti akusala kudya. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwo alandiriratu mphotho yawo yonse. 17Koma pamene ukusala kudya, samba mʼmaso nudzole mafuta kumutu, 18kuti usaonekere kwa anthu kuti ukusala kudya koma kwa Atate ako ali mseri; ndipo Atate ako amene amaona za mseri adzakupatsa mphotho.

Za Chuma cha Kumwamba

19“Musadziwunjikire chuma pa dziko lapansi, pamene njenjete ndi dzimbiri zimawononga ndi pamene mbala zimathyola ndi kuba. 20Koma mudziwunjikire chuma kumwamba kumene njenjete ndi dzimbiri siziwononga ndipo mbala sizithyola ndi kuba. 21Pakuti kumene kuli chuma chako, mtima wako udzakhala komweko.

Diso Nyale ya Thupi

22“Diso ndi nyale ya thupi. Ngati maso ako ali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mʼkuwala. 23Koma ngati maso ako sali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mu mdima. Koma ngati kuwala kuli mwa iwe ndi mdima, ndiye kuti mdimawo ndi waukulu bwanji!

24“Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri. Pakuti pena adzamuda mmodzi ndi kukonda winayo kapena adzagwira ntchito mokhulupirika kwa mmodzi, nadzanyoza winayo. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa chuma pa nthawi imodzi.

Musade Nkhawa

25“Nʼchifukwa chake ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu kuti mudzadya chiyani kapena mudzamwa chiyani; kapenanso za thupi lanu kuti mudzavala chiyani. Kodi moyo suposa chakudya? Kodi thupi siliposa zovala? 26Onani mbalame zamlengalenga sizifesa kapena kukolola kapena kusunga mʼnkhokwe komabe Atate anu akumwamba amazidyetsa. Kodi inu simuziposa kwambiri? 27Kodi ndani wa inu podandaula angathe kuwonjeza ora limodzi pa moyo wake?

28“Ndipo bwanji inu mudera nkhawa za zovala? Onani makulidwe a maluwa akutchire. Sagwira ntchito kapena kuwomba nsalu. 29Ndikukuwuzani kuti angakhale Solomoni mu ulemerero wake sanavale mofanana ndi limodzi la maluwa amenewa. 30Ngati umu ndi mmene Mulungu avekera udzu wa kutchire umene ulipo lero ndipo mawa uponyedwa ku moto, kodi sadzakuvekani koposa? Aa! Inu a chikhulupiriro chochepa! 31Chifukwa chake musadere nkhawa ndi kuti, ‘Tidzadya chiyani?’ kapena ‘Tidzamwa chiyani?’ kapena ‘Tidzavala chiyani?’ 32Pakuti anthu akunja amazifuna zinthu zonsezi ndipo Atate anu akumwamba adziwa kuti musowa zimenezi. 33Koma muyambe mwafuna ufumu wake ndi chilungamo chake ndipo zinthu zonsezi zidzapatsidwa kwa inu. 34Chifukwa chake musadere nkhawa ndi za mawa, popeza tsiku lililonse lili ndi zovuta zake zokwanira.

Knijga O Kristu

Matej 6:1-34

O pomaganju onima koji su u potrebi

1“Pazite! Nemojte svoja dobra djela činiti javno da vam se drugi dive jer onda nećete primiti plaću od svojega nebeskog Oca.

2Zato kada daješ milodar, ne trubi pred sobom kao što to u sinagogama i na ulicama čine licemjeri da ih ljudi hvale. Zaista vam kažem, drugu nagradu osim te neće dobiti.6:2, 5 i 16 U grčkome: oni su već primili svoju plaću. 3Naprotiv, kada daješ milodar, neka tvoja ljevica ne zna što radi desnica. 4Udijeli svoj milodar potajno pa će te tvoj Otac, koji vidi i u tajnosti, nagraditi.”

O molitvi

(Mk 11:25; Lk 11:2-4)

5“I kada se molite, ne budite poput licemjera koji se vole moliti u sinagogama i po uličnim raskrižjima da ih ljudi vide. Zaista vam kažem, drugu nagradu osim te neće dobiti. 6Ti, naprotiv, kada se moliš, uđi nekamo gdje ćeš biti sam, zatvori za sobom vrata te se pomoli Ocu u tajnosti, a tvoj će te Otac, koji vidi u tajnosti, nagraditi. 7Kad se molite, ne nabrajajte isprazne riječi kao pogani, koji misle da će biti uslišani zbog svojega nabrajanja. 8Ne činite kao oni jer vaš Otac dobro zna što vam je potrebno i prije nego što ga zamolite. 9Zato se vi molite ovako:

‘Oče naš na nebu, neka se štuje tvoje sveto ime.

10Neka dođe tvoje kraljevstvo.

Neka se tvoja volja provodi

na zemlji kao i na nebu.

11Kruh naš svagdašnji daj nam danas

12i oprosti nam naše grijehe kao što i mi opraštamo onima koji griješe protiv nas.

13I ne dopusti da podlegnemo kušnji,

nego nas izbavi od Zloga.’6:13 U nekim rukopisima stoji još: Jer tvoji su kraljevstvo, sila i slava zauvijek. Amen.

14Jer ako oprostite ljudima njihove pogreške, i vaš će nebeski Otac vama oprostiti. 15Ali ne oprostite li vi drugima njihovih pogrešaka, ni vaš Otac neće vama oprostiti vaše grijehe.

O postu

16Kad postite, ne mrštite se kao licemjeri, koji izobliče lice kako bi ljudi opazili da poste. Zaista vam kažem, drugu nagradu osim te neće dobiti. 17Ali ti se, kada postiš, lijepo uredi 18da tvoj post ne zapaze ljudi, nego samo tvoj Otac koji je u tajnosti. I tvoj će ti Otac, koji vidi u tajnosti, uzvratiti.”

O novcu i imetku

(Lk 11:34-36; 12:33-34; 16:13)

19“Ne zgrćite sebi blago ovdje na zemlji, gdje ga mogu izgristi moljci ili može zahrđati, gdje lopovi provaljuju i kradu. 20Stječite sebi blago na nebu, gdje ga ne mogu izgristi moljci ni hrđa, gdje lopovi ne provaljuju i ne kradu. 21Jer gdje ti je blago, ondje će ti biti i srce.

22Oko je poput svjetiljke tijelu. Ne budete li odviše brinuli za materijalna dobra jasno ćete vidjeti u životu, 23ali ako za njih budete previše brinuli vid će vam biti zasjenjen i duboka će vam tama ispuniti život.

Ne može se služiti Bogu i bogatstvu

24Nitko ne može služiti dvojici gospodara. Ili će jednoga mrziti, a drugoga voljeti ili će jednome biti odan, a drugoga prezirati. Ne možete služiti i Bogu i bogatstvu.

Ne brinite se!

(Lk 12:22-31)

25Zato vam kažem: Ne brinite se tjeskobno kako ćete preživjeti, što ćete jesti ili piti, ni u što ćete obući svoje tijelo! Nije li život vredniji od hrane, a tijelo od odjeće? 26Pogledajte ptice nebeske! Niti siju, niti žanju, niti sabiru u žitnice jer ih hrani vaš nebeski Otac. A niste li vi mnogo vredniji od njih? 27Može li tko od vas sebi brigama produžiti život barem i za jedan dan?

28Zašto se onda brinuti za odjeću? Pogledajte samo poljske ljiljane! Niti se muče niti predu. 29A kažem vam da se ni kralj Salomon u svoj svojoj raskoši nije zaodjenuo kao jedan od njih. 30Pa ako Bog tako odijeva poljsku travu koja danas jest, a već se sutra baca u peć, zar se neće još i više brinuti za vas, malovjerni? 31Ne brinite se tjeskobno i ne govorite: ‘Što ćemo jesti?’, ‘Što ćemo piti?’ ili ‘U što ćemo se obući?’ 32jer tako čine nevjernici. Vaš nebeski Otac zna da vam je sve to potrebno. 33Stoga najprije tražite Božje kraljevstvo i njegovu pravednost, pa će vam se i to nadodati.

34Ne brinite se zato tjeskobno za sutra jer će ono donijeti nove brige. Današnja vam je muka dovoljna za danas.”