Mateyu 23 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 23:1-39

Yesu Adzudzula Aphunzitsi Amalamulo ndi Afarisi

1Pamenepo Yesu anati kwa magulu a anthu ndi ophunzira ake: 2“Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi amakhala pa mpando wa Mose. 3Choncho muziwamvera ndi kuchita chilichonse chimene akuwuzani. Koma musachite zimene amachita, popeza sachita zimene amaphunzitsa. 4Amamanga akatundu olemera nawayika pa mapewa a anthu, koma iwo eni safuna kuwanyamula.

5“Ntchito zawo amachita ndi cholinga chakuti anthu awaone. Amadzimangirira timaphukusi tikulutikulu ta Mawu a Mulungu pa mphumi ndi pa mkono komanso amatalikitsa mphonje za mikanjo yawo. 6Amakonda malo aulemu pa maphwando ndi malo ofunika kwambiri mʼmasunagoge. 7Amakondwera ndi kupatsidwa moni mʼmisika ndi kutchulidwa kuti ‘Aphunzitsi.’

8“Koma inu simuyenera kutchulidwa ‘Aphunzitsi,’ popeza muli naye Mbuye mmodzi ndipo inu nonse ndinu abale. 9Ndipo musamatchule wina aliyense pansi pano kuti ‘Atate,’ pakuti muli ndi Atate mmodzi, ndipo ali kumwamba. 10Komanso musamatchedwenso ‘Mtsogoleri,’ pakuti muli naye Mtsogoleri mmodzi amene ndi Khristu. 11Wamkulu pakati panu adzakhala wokutumikirani. 12Pakuti aliyense amene adzikuza adzachepetsedwa, ndipo aliyense amene adzichepetsa adzakuzidwa.

Tsoka kwa Aphunzitsi Amalamulo ndi Afarisi

13“Tsoka kwa inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumatseka pa khomo la kumwamba kuti anthu asalowemo. Eni akenu simulowamo komanso simulola kuti ena amene akufuna kulowa kuti alowe. 14Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumawadyera akazi amasiye chuma chawo, kwinaku nʼkumanamizira kunena mapemphero ataliatali. Chifukwa cha zimenezi Mulungu adzakulangani koposa.

15“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu.

16“Tsoka kwa inu, atsogoleri akhungu! Mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula Nyumba ya Mulungu, zilibe kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula ndalama zagolide za mʼNyumbayo, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’ 17Inu akhungu opusa! Chopambana nʼchiyani: ndalama zagolide, kapena Nyumba imene imayeretsa golideyo? 18Ndiponso mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula guwa lansembe, sizitanthauza kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula mphatso ya paguwa lansembe, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’ 19Inu anthu akhungu! Chopambana nʼchiyani: mphatso, kapena guwa limene limayeretsa mphatsoyo? 20Chifukwa chake, iye amene alumbira kutchula guwa alumbira pa ilo ndi pa chilichonse chili pamenepo. 21Ndipo iye wolumbira potchula Nyumba ya Mulungu alumbira pa Nyumbayo ndi pa Iye amene amakhala mʼmenemo. 22Ndipo iye wolumbira kutchula kumwamba alumbira kutchula mpando waufumu wa Mulungu ndi pa Iye wokhalapo.

23“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumapereka chakhumi cha timbewu tonunkhira ndi cha timbewu tokometsera chakudya. Koma mwasiya zofunikira kwambiri za mʼmalamulo monga chilungamo, chifundo ndi kukhulupirika. Muyenera kuchita zomalizirazi komanso osasiya zoyambazo. 24Atsogoleri akhungu inu! Mumachotsa kantchentche mu chakumwa chanu koma mumameza ngamira.

25“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumayeretsa kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkatimo mwadzaza ndi dyera ndi kusadziretsa. 26Afarisi akhungu! Poyamba tsukani mʼkati mwa chikho ndi mbale, ndipo kunja kwake kudzakhalanso koyera.

27“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Muli ngati ziliza pa manda zowala kunja zimene zimaoneka zokongola koma mʼkatimo mwadzaza mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zina zonse. 28Chimodzimodzinso, kunja mumaoneka kwa anthu kuti ndinu olungama koma mʼkatimo ndinu odzaza ndi chinyengo ndi zoyipa zina.

29“Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumamanga ziliza za aneneri ndi kukongoletsa manda a olungama. 30Ndipo mumati, ‘Ngati tikanakhala mʼmasiku a makolo athu sitikanakhetsa nawo magazi a aneneri.’ 31Potero mukutsimikiza kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri. 32Dzazani inu muyeso wa uchimo wa makolo anu!

33“Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? 34Choncho ndi kutumizirani aneneri ndi anthu anzeru ndi aphunzitsi. Ena a iwo mudzawapha ndi kuwapachika; ena mudzawakwapula mʼmasunagoge anu ndi kuwafunafuna kuchokera mudzi wina kufikira wina. 35Ndipo magazi onse a olungama amene anakhetsedwa pansi pano, kuyambira magazi a Abele, olungama kufikira Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, adzakhala pa inu. 36Zoonadi, ndikuwuzani kuti zonsezi zidzafika pa mʼbado uno.

37“Haa! Yerusalemu, Yerusalemu, iwe amene umapha aneneri ndi kugenda miyala amene atumidwa kwa iwe, kawirikawiri ndimafuna kusonkhanitsa ana ako, monga nkhuku imasonkhanitsira ana ake pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune. 38Taona, nyumba yako yasiyidwa ya bwinja. 39Chifukwa chake ndikuwuza kuti simudzandionanso kufikira pamene mudzati, ‘Wodala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye.’ ”

Knijga O Kristu

Matej 23:1-39

Isus opominje vjerske poglavare

(Mk 12:38-39; Lk 11:39-52; 20:45-46)

1Tada Isus reče mnoštvu i svojim učenicima: 2“Pismoznanci i farizeji službeni su tumači Svetoga pisma.23:2 U grčkome: su zasjeli na Mojsijevu stolicu. 3Zato činite i slušajte sve što vam kažu, ali nemojte slijediti njihov primjer jer oni sami ne čine ono što druge poučavaju. 4Tlače vas teškim teretom vjerskih zahtjeva, a ni prstom ne žele maknuti da vam taj teret pomognu nositi.

5Sve što čine, čine zato da ih ljudi vide. Trude se da ono što na sebi nose u znak pobožnosti—kutijice sa stihovima iz Svetoga pisma na čelu ili oko ruke te rese na odjeći—bude što veće i što duže. 6Na gozbama vole sjediti na pročelju stola, a u sinagogama na počasnome mjestu. 7Godi im kad ih ljudi pozdravljaju na javnim mjestima i kad ih zovu ‘Učitelju’.23:7 U grčkome: Rabbi.

8Vi nikome nemojte dopustiti da vas zove učiteljem jer imate samo jednoga učitelja, a svi ste vi ravnopravna braća i sestre.23:8 U grčkome: svi ste vi braća. 9I ne zovite nikoga ovdje na zemlji Ocem jer imate samo jednoga Oca—onoga na nebesima. 10I ne dajte da vas tko naziva vođom jer imate samo jednoga vođu: Krista. 11Tko je najveći među vama, neka vam bude sluga! 12Tko sebe uzvisuje, bit će ponižen, a ponizni će biti uzvišeni.

13Teško vama, pismoznanci i farizeji! Licemjeri! Zatvarate pred ljudima vrata u nebesko kraljevstvo. Sami ne ulazite u njega, a ne dopuštate da uđu ni oni koji bi htjeli.23:13 U nekim je rukopisima dodan i 14. stih: Teško vama, pismoznanci i farizeji! Bestidno lišavate udovice njihovih dobara, a prikrivate se dugim molitvama u javnosti. Zato ćete vam kazna biti veća.

15Teško vama, pismoznanci i farizeji! Licemjeri! Obilazite morem i kopnom da biste pridobili jednog sljedbenika, a kad vam postane sljedbenikom, učinite od njega sina paklenoga dvostruko gorega nego što ste i sami!

16Teško vama! Slijepi vođe! Tvrdite: ‘Zakune li se tko Hramom, to ne vrijedi. Ali zakune li se hramskim zlatom, onda ga zakletva obvezuje.’ 17Slijepe budale! Pa što je veće—zlato ili Hram koji posvećuje zlato? 18I još kažete: ‘Zakune li se tko žrtvenikom, to ne vrijedi. Ali zakune li se darom koji je na njemu, zakletva ga obvezuje.’ 19Slijepci! Što je veće? Žrtveni dar ili žrtvenik koji ga posvećuje? 20Tko se zakune žrtvenikom, kune se njime i svime što je na njemu. 21A tko se zakune Hramom, kune se njime i Onime koji u njemu prebiva. 22Tko se zakune nebom, kune se Božjim prijestoljem i Bogom koji na njemu sjedi.

23Teško vama, pismoznanci i farizeji! Licemjeri! Jer revno namirujete čak i desetinu metvice, i kopra, i kima, a zanemarujete ono najvažnije u Zakonu: pravednost, milosrđe i vjernost. Treba davati desetinu, ali ne smijete zanemarivati važnije stvari.23:23 U grčkome: Ovo je trebalo činiti, a ono ne propuštati. 24Slijepi vođe! Procjeđujete vodu da ne biste s njom popili i komarca, a kadri ste, ne opazivši, progutati i cijelu devu!

25Teško vama, pismoznanci i farizeji! Licemjeri! Toliko se trudite očistiti svoju čašu i zdjelu izvana, a napunili ste ih svojim grabežom i pohlepom. 26Slijepi farizeju! Očisti najprije ono što je u čaši, pa će i izvana biti čista.

27Teško vama, pismoznanci i farizeji! Vi ste poput obijeljenih grobova. Izvana izgledaju lijepo, a iznutra su prepuni mrtvačkih kostiju i svakojake prljavštine! 28Tako i vi ljudima izvana izgledate pravednima, a iznutra ste prepuni licemjerja i bezakonja.

29Teško vama, pismoznanci i farizeji! Licemjeri! Vi prorocima gradite grobnice i pravednicima kitite spomenike 30pa kažete: ‘Da smo živjeli u doba svojih otaca, ne bismo sudjelovali u prolijevanju proročke krvi.’ 31Tako sami protiv sebe svjedočite da ste sinovi onih koji su ubijali proroke. 32Dovršite, dakle, to što su oni započeli!23:32 U grčkome: Dopunite mjeru svojih otaca!

33Zmije! Leglo zmijsko! Kako ćete izbjeći osudi pakla? 34Šaljem vam, evo, proroke, mudrace i pismoznance. Neke ćete od njih ubiti i raspeti, druge bičevati po sinagogama i progoniti od grada do grada 35tako da na vas padne sva pravedna krv prolivena na zemlji, od krvi pravednog Abela pa do krvi Zaharije, sina Barahijina, kojega ste ubili između Hrama i žrtvenika. 36Zaista vam kažem, sva će ta krv pasti na ovaj naraštaj!”

Isus tuži nad Jeruzalemom

(Lk 13:34-35)

37“Jeruzaleme, Jeruzaleme, koji ubijaš proroke i kamenuješ Božje poslanike! Koliko sam puta htio okupiti tvoju djecu kao što kvočka skuplja piliće pod krila, ali niste htjeli! 38A sada će ti, eto, kuća biti napuštena. 39I kažem vam, nećete me više vidjeti sve dok ne uzviknete: ‘Blagoslovljen koji dolazi u ime Gospodnje!’”23:39 Vidjetii Psalam 118:26.