Mateyu 19 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 19:1-30

Za Kuthetsa Ukwati

1Yesu atatsiriza kunena zinthu zimenezi, anachoka ku Galileya ndi kupita ku chigawo cha Yudeya mbali ina ya mtsinje wa Yorodani. 2Magulu akulu a anthu anamutsatira Iye, ndipo iwo anachiritsidwa pomwepo.

3Afarisi ena anabwera kwa Iye kudzamuyesa. Anamufunsa Iye nati, “Kodi ndikololedwa kuti mwamuna amuleke mkazi wake pa chifukwa china chilichonse?”

4Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge kuti pachiyambi Mulungu analenga iwo, ‘mwamuna ndi mkazi?’ 5Ndipo anati, ‘Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.’ 6Motero salinso awiri ayi koma mmodzi. Nʼchifukwa chake chimene Mulungu wachimanga pamodzi munthu wina asachilekanitse.”

7Ndipo iwo anamufunsa nati, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mose analamula kuti mwamuna azipatsa mkazi wake kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa?”

8Yesu anayankha kuti, “Mose anakulolezani kuti muzisudzula akazi anu chifukwa cha kuwuma mitima kwanu. Koma sizinali chotere kuyambira pachiyambi. 9Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake, osati chifukwa cha chiwerewere nakakwatira mkazi wina, achita chigololo.”

10Ophunzira ake anati kwa Iye, “Ngati umu ndi mmene zilili pa mwamuna ndi mkazi, kuli bwino kusakwatira.”

11Yesu anayankha kuti, “Si aliyense amene angavomere chiphunzitso ichi, koma kwa okhawo amene achimvetsetsa. 12Pakuti ena ndi akuti sangakwatire chifukwa anabadwa motero, ena ali motero chifukwa chofulidwa ndi anthu ndipo ena anawukana ukwati chifukwa cha ufumu wakumwamba. Iye amene angalandire ichi alandire.”

Yesu Adalitsa Ana

13Pamenepo anabwera nawo ana kwa Yesu kuti awasanjike manja ndi kuwapempherera. Koma ophunzira ake anadzudzula amene anabweretsa anawo.

14Yesu anati, “Lolani ana abwere kwa Ine, ndipo musawaletse pakuti ufumu wakumwamba ndi wa iwo onga anawa.” 15Atasanjika manja ake pa anawo, anachokapo.

Mnyamata Wolemera ndi Ufumu wa Mulungu

16Taonani mnyamata wina anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Aphunzitsi, ndi chinthu chiti chabwino chimene ndiyenera kuchita kuti ndipeze moyo wosatha?”

17Yesu anayankha kuti, “Ukundifunsiranji Ine za chinthu chimene ndi chabwino? Pali mmodzi yekha amene ndi wabwino. Ngati ukufuna kulowa mʼmoyo wosatha mvera malamulo.”

18Mnyamatayo anamufunsa kuti, “Ndi ati?”

Yesu anayankha kuti, “Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni onama, 19lemekeza abambo ako ndi amayi ako ndipo konda mnansi wako monga iwe mwini.”

20Mnyamatayo anati, “Zonsezi ndimazisunga, nanga chatsala ndi chiyani?”

21Yesu anayankha kuti, “Ngati ukufuna kukhala wangwiro, pita kagulitse katundu wako ndi kupereka kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ukakachita zimenezi, ukabwere udzanditsate Ine.”

22Mnyamatayo atamva zimenezi, anachoka mokhumudwa, chifukwa anali ndi chuma chambiri.

23Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti nʼkovuta kuti olemera akalowe mu ufumu wakumwamba. 24Komanso ndikuwuzani kuti, nʼkwapafupi kuti ngamira idzere pa kabowo ka zingano kusiyana ndi kuti wolemera akalowe mu ufumu wa Mulungu.”

25Ophunzira atamva zimenezi, anadabwa kwambiri ndipo anamufunsa kuti, “Nanga angapulumuke ndani?”

26Yesu anawayangʼana iwo nati, “Ndi anthu, izi nʼzosatheka, koma ndi Mulungu zinthu zonse zimatheka.”

27Petro anamuyankha Iye kuti, “Ife tinasiya zonse ndi kukutsatirani Inu! Nanga tsono ife tidzalandira chiyani?”

28Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti pa nthawi yokonzanso zinthu zonse, pamene Mwana wa Munthu adzakhala pa mpando wake waufumu mu ulemerero wake kumwamba, inu amene mwanditsata Ine mudzakhalanso pa mipando khumi ndi iwiri yaufumu, kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli. 29Ndipo aliyense amene wasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena bambo kapena mayi kapena mkazi, kapena ana, kapena minda chifukwa cha Ine adzalandira madalitso ochuluka ndi kulandiranso moyo wosatha. 30Koma ambiri amene ali oyambirira adzakhala omalizira, ndipo ambiri amene ndi omalizira adzakhala oyambirira.”

Slovo na cestu

Matouš 19:1-30

Ježíš učí o manželství a rozvodu

1Po tomto hovoru Ježíš odešel do Judska za Jordánem.

2Mnoho lidí šlo za ním a on uzdravoval nemocné. 3Přišli za ním i farizejové a chtěli ho vyprovokovat k nějakému výroku, který by mohli použít proti němu. „Může se člověk rozvést z jakéhokoliv důvodu?“ zeptali se.

4-6On odpověděl: „Nečetli jste v Písmu, že když na počátku Bůh stvořil muže a ženu, ustanovil: Muž opustí své rodiče, připojí se ke své ženě a stanou se jednou bytostí? Nikdo nemá právo rozdělit to, co Bůh spojil.“

7Oni však namítali: „Proč tedy Mojžíš řekl, že muž může propustit manželku jednoduše tím, že jí dá rozlukový lístek?“

8Ježíš odpověděl: „Toto ustanovení Mojžíšova zákona je ústupkem vaší tvrdosti a nesnášenlivosti. Původní Boží úmysl to však nikdy nebyl. 9Já vám říkám, že kdo se rozvádí z jiného důvodu, než je cizoložství jeho partnera, a uzavírá nový sňatek, dopouští se sám cizoložství.“

10Učedníci mu řekli: „Když mohou nastat takové těžkosti mezi mužem a ženou, pak je lepší se neženit.“ 11On odpověděl: „Tak jednoduché to není. Je zde nutné porozumět Boží vůli. 12Jsou tři důvody proto, aby člověk zůstal svobodný: když je k manželství od narození nezpůsobilý, když mu v uzavření sňatku zabránili lidé, nebo když se manželství zřekne dobrovolně pro plnou službu Boží věci. Rozumíte tomu?“

Ježíš žehná malým dětem

13Potom k Ježíšovi nosili malé děti, aby jim žehnal a modlil se za ně. Učedníci však domlouvali těm, kteří děti přivedli, aby Ježíše neobtěžovali. 14On jim ale řekl: „Nechte je, ať jdou ke mně, a nebraňte jim. Jejich místo je u mne.“ 15Kladl na ně ruce a žehnal jim. Pak odtud odešel.

Ježíš mluví s bohatým mužem

16Za Ježíšem přišel jeden mladý člověk a ptal se ho: „Mistře, jakými dobrými skutky mohu získat věčný život?“

17Ježíš mu na to řekl: „Snažíš se být dobrý? To se chceš vyrovnat Bohu, který jediný je skutečně dobrý! Plň jeho přikázání a budeš věčně živ.“

18„Která to jsou?“ zeptal se mladý muž.

Ježíš odpověděl: „Nezabiješ, nezcizoložíš, nebudeš krást, lhát, 19budeš ctít svoje rodiče, své bližní budeš milovat jako sebe!“

20Mladík na to řekl: „To všechno jsem vždycky dodržoval. Co mi ještě chybí?“

21Ježíš odpověděl: „Chceš-li být dokonalý, jdi a prodej celý svůj majetek a peníze rozdej chudým, a tak budeš mít poklad v nebi. Pak se vrať a staň se mým učedníkem.“

22Mladík zesmutněl a zklamaně odešel. Měl totiž velký majetek. 23Ježíš pak řekl svým učedníkům: „Pro zámožného člověka je velmi nesnadné postavit se na Boží stranu. 24Kdybych to měl k něčemu přirovnat, pak snáze projde velbloud uchem jehly, nežli bohatý branou Božího království.“ 25Učedníky to překvapilo a ptali se: „Kdo tedy vůbec může být spasen?“

26Ježíš se na ně zadíval a řekl: „V lidských silách to není, ale Bůh dokáže všechno.“

27Petr se ozval a řekl: „My jsme se vzdali všeho a jdeme za tebou. Co nás čeká?“

28Ježíš odpověděl: „Ujišťuji vás, že až přijdu, abych stvořil nový svět, nad kterým budu panovat v plné slávě, pak vás dvanáct, kteří mne následujete, posadím po svém boku jako soudce celého Izraele. 29A každému, kdo se vzdá domova, bratrů, sester, otce, matky, manželky, dětí nebo majetku proto, aby šel za mnou, všechno mu mnohokrát vynahradím a bude mít podíl na věčném životě. 30Mnozí první budou poslední a poslední budou první.