Mateyu 12 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 12:1-50

Yesu Mbuye wa Sabata

1Pa nthawi imeneyo Yesu anadutsa pakati pa minda ya tirigu pa tsiku la Sabata. Ophunzira ake anamva njala nayamba kuthyola ngala za tirigu nʼkumadya. 2Afarisi ataona zimenezi anati kwa Iye, “Taonani! Ophunzira anu akuchita zosaloledwa pa tsiku la Sabata.”

3Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge zimene anachita Davide pamene iye ndi anzake anamva njala? 4Analowa mʼNyumba ya Mulungu, ndipo iye ndi anzakewo anadya buledi wopatulika amene sikunali kololedwa kwa iwo kudya koma ansembe okha. 5Kodi simunawerenge mʼmalamulo kuti pa Sabata ansembe mʼNyumba ya Mulungu amaphwanya lamulo la Sabata komabe sawayesa olakwa? 6Ine ndikuwuzani kuti wamkulu kuposa Nyumba ya Mulunguyo ali pano. 7Ngati mukanadziwa zomwe mawu awa atanthauza, ‘Ine ndifuna chifundo osati nsembe,’ inu simukanatsutsa osalakwa. 8Pakuti Mwana wa Munthu ndiye Mbuye wa Sabata.”

Yesu Achiritsa Munthu Wolumala Dzanja

9Atachoka kumeneko anakalowa mʼsunagoge mwawo. 10Ndipo mʼmenemo munali munthu wolumala dzanja. Pofuna chifukwa chokamunenezera, iwo anamufunsa Yesu kuti, “Kodi nʼkololedwa kuchiritsa munthu tsiku la Sabata?”

11Iye anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu ali ndi nkhosa nigwera mʼdzenje tsiku la Sabata, kodi simudzayigwira ndi kuyitulutsa kunja? 12Nanga munthu sali oposa nkhosa kwambiri! Chifukwa chake nʼkololedwa kuchita zabwino pa Sabata.”

13Pamenepo Yesu anati kwa munthuyo, “Wongola dzanja lako.” Iye analiwongola ndipo linakhala monga linalili kale. 14Koma Afarisi anatuluka kunja ndi kukonza njira yoti amuphere.

Mtumiki Wosankhidwa ndi Mulungu

15Podziwa zimenezi, Yesu anachoka kumalo amenewo. Ambiri anamutsata Iye ndipo anachiritsira odwala awo onse 16nawachenjeza kuti asamuwulule kuti yani. 17Uku kunali kukwaniritsa zimene zinayankhulidwa kudzera mwa mneneri Yesaya kuti,

18“Taonani mnyamata wanga amene ndinamusankha,

Wokondedwa wanga, amene moyo wanga ukondwera naye.

Pa Iye ndidzayika Mzimu wanga,

ndipo Iye adzalalikira chiweruzo kwa akunja.

19Sadzalimbana, sadzafuwula,

ngakhale mmodzi sadzamva mawu ake mʼmakwalala.

20Bango lophwanyika sadzalithyola,

ndi nyale yofuka sadzayizimitsa,

kufikira Iye adzatumiza chiweruziro chikagonjetse.

21Ndipo akunja adzakhulupirira dzina lake.”

Mwano wa Afarisi

22Pomwepo anthu anabwera naye kwa Yesu munthu wogwidwa ndi chiwanda amene anali wosaona ndi wosamva ndipo Yesu anamuchiritsa kotero kuti atatha anayamba kumva ndi kuona. 23Anthu onse anadabwa ndipo anati, “Kodi uyu ndi kukhala mwana wa Davide?”

24Koma Afarisi atamva zimenezi, anati, “Uyu amatulutsa ziwanda ndi mphamvu ya Belezebabu mkulu wa ziwandazo.”

25Yesu anadziwa maganizo awo ndipo anawawuza kuti, “Ufumu uliwonse ukagawanika mwa iwo udzawonongeka ndi mzinda uliwonse kapena banja likagawanika, mwa izo zokha sizidzayima. 26Ngati Satana atulutsa Satana, iye adzigawa yekha. Nanga ufumu wake ungayime bwanji? 27Ndipo ngati Ine nditulutsa ziwanda ndi Belezebule, anthu anu amatulutsa ziwandazo ndi chiyani? Potero tsono adzakhala oweruza anu. 28Koma ngati Ine ndimatulutsa ziwanda ndi Mzimu wa Mulungu, pamenepo ufumu wa Mulungu wafika pa inu.

29“Kapenanso wina aliyense angathe bwanji kulowa mʼnyumba ya munthu wamphamvu ndi kunyamulamo zinthu zake, sipokhapo atayamba wamanga munthu wa mphamvuyo? Pamenepo iye akhoza kuba mʼnyumbamo.

30“Iye amene sali ndi Ine atsutsana nane ndipo iye amene sasonkhanitsa pamodzi ndi Ine amamwaza. 31Ndipo potero Ine ndikuwuzani inu, tchimo lililonse ndi cha mwano chilichonse zidzakhululukidwa kwa anthu koma chamwano cha pa Mzimu Woyera, sichidzakhululukidwa. 32Aliyense amene anena mawu otsutsana ndi Mwana wa Munthu adzakhululukidwa koma aliyense wonena motsutsana ndi Mzimu Woyera sadzakhululukidwa mu mʼbado uno kapena umene ukubwerawo.

Mtengo ndi Zipatso Zake

33“Mtengo wabwino umabala zipatso zabwino ndipo mtengo woyipa umabalanso zipatso zoyipa, pajatu mtengo umadziwika ndi zipatso zake. 34Ana anjoka inu, woyipa inu, mungathe bwanji kuyankhula kanthu kalikonse kabwino? Pakuti pakamwa pamayankhula zosefuka kuchokera mu mtima. 35Munthu wabwino amatulutsa zinthu zabwino zomwe zili mumtima mwake ndipo munthu woyipa amatulutsanso zinthu zoyipa zomwe zili mwa iye. 36Ine ndikukuwuzani kuti pa tsiku la chiweruziro munthu adzazengedwa mlandu chifukwa cha mawu aliwonse wopanda pake amene anayankhula. 37Pakuti ndi mawu anu mudzapezeka osalakwa ndiponso ndi mawu anu mudzapezeka olakwa.”

Chizindikiro cha Yona

38Pamenepo ena mwa Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo anati kwa Iye, “Aphunzitsi, tikufuna tione chizindikiro chodabwitsa kuchokera kwa Inu.”

39Iye anayankha kuti, “Mʼbado woyipa ndi wachigololo ufunsa za chizindikiro chodabwitsa! Koma ndi chimodzi chomwe sichidzapatsidwa kwa inu kupatula chizindikiro cha mneneri Yona. 40Pakuti monga Yona anali mʼmimba mwa nsomba yayikulu masiku atatu, usana ndi usiku, momwemonso Mwana wa Munthu adzakhala masiku atatu, usana ndi usiku, mʼkati mwa nthaka. 41Anthu a ku Ninive adzayimirira pachiweruzo ndi mʼbado uwu ndi kuwutsutsa pakuti iwo analapa Yona atalalikira ndipo tsopano wamkulu kuposa Yona ali pano. 42Mfumu yayikazi yakummwera idzayimirira pa tsiku lachiweruzo ndi mʼbado uwu ndipo idzawutsutsa pakuti inachokera kumathero a dziko lapansi kudzamva nzeru za Solomoni, ndipo pano pali woposa Solomoni.

Za Mzimu Woyipa

43“Pamene mzimu woyipa utuluka mwa munthu, umadutsa malo wopanda madzi kufunafuna malo opumulira ndipo suwapeza. 44Pamenepo umati, ‘Ndidzabwerera ku nyumba yanga komwe ndinatuluka.’ Pamene ufika, upeza mopanda kanthu, mosesedwa ndi mokonzedwa bwino. 45Kenaka umapita kukatenga mizimu ina isanu ndi iwiri yoyipa kwambiri kuposa uwowo ndipo imapita ndi kukakhala mʼmenemo. Choncho khalidwe lotsiriza la munthu uyu limakhala loyipa kwambiri kuposa loyambalo. Umo ndi mmene zidzakhalire ndi mʼbado oyipawu.”

Amayi ndi Abale Ake a Yesu

46Pamene Yesu anali kuyankhulabe ndi gulu la anthu, amayi ndi abale ake anayimirira kunja, akufuna kuyankhulana naye. 47Wina anamuwuza Iye kuti, “Amayi ndi abale anu ayima kunjaku akufuna kuyankhulana nanu.”

48Iye anayankha kuti, “Amayi anga ndani ndipo abale anga ndi ndani?” 49Ndipo akuloza ophunzira ake, Iye anati, “Awa ndiwo amayi anga ndi abale anga. 50Pakuti aliyense amene achita chifuniro cha Atate anga akumwamba ndiye mʼbale wanga, mlongo wanga ndi amayi anga.”

King James Version

Matthew 12:1-50

1At that time Jesus went on the sabbath day through the corn; and his disciples were an hungred, and began to pluck the ears of corn, and to eat. 2But when the Pharisees saw it, they said unto him, Behold, thy disciples do that which is not lawful to do upon the sabbath day. 3But he said unto them, Have ye not read what David did, when he was an hungred, and they that were with him; 4How he entered into the house of God, and did eat the shewbread, which was not lawful for him to eat, neither for them which were with him, but only for the priests? 5Or have ye not read in the law, how that on the sabbath days the priests in the temple profane the sabbath, and are blameless? 6But I say unto you, That in this place is one greater than the temple. 7But if ye had known what this meaneth, I will have mercy, and not sacrifice, ye would not have condemned the guiltless. 8For the Son of man is Lord even of the sabbath day. 9And when he was departed thence, he went into their synagogue:

10¶ And, behold, there was a man which had his hand withered. And they asked him, saying, Is it lawful to heal on the sabbath days? that they might accuse him. 11And he said unto them, What man shall there be among you, that shall have one sheep, and if it fall into a pit on the sabbath day, will he not lay hold on it, and lift it out? 12How much then is a man better than a sheep? Wherefore it is lawful to do well on the sabbath days. 13Then saith he to the man, Stretch forth thine hand. And he stretched it forth; and it was restored whole, like as the other.

14¶ Then the Pharisees went out, and held a council against him, how they might destroy him. 15But when Jesus knew it, he withdrew himself from thence: and great multitudes followed him, and he healed them all; 16And charged them that they should not make him known: 17That it might be fulfilled which was spoken by Esaias the prophet, saying, 18Behold my servant, whom I have chosen; my beloved, in whom my soul is well pleased: I will put my spirit upon him, and he shall shew judgment to the Gentiles. 19He shall not strive, nor cry; neither shall any man hear his voice in the streets. 20A bruised reed shall he not break, and smoking flax shall he not quench, till he send forth judgment unto victory. 21And in his name shall the Gentiles trust.

22¶ Then was brought unto him one possessed with a devil, blind, and dumb: and he healed him, insomuch that the blind and dumb both spake and saw. 23And all the people were amazed, and said, Is not this the son of David? 24But when the Pharisees heard it, they said, This fellow doth not cast out devils, but by Beelzebub the prince of the devils. 25And Jesus knew their thoughts, and said unto them, Every kingdom divided against itself is brought to desolation; and every city or house divided against itself shall not stand: 26And if Satan cast out Satan, he is divided against himself; how shall then his kingdom stand? 27And if I by Beelzebub cast out devils, by whom do your children cast them out? therefore they shall be your judges. 28But if I cast out devils by the Spirit of God, then the kingdom of God is come unto you. 29Or else how can one enter into a strong man’s house, and spoil his goods, except he first bind the strong man? and then he will spoil his house. 30He that is not with me is against me; and he that gathereth not with me scattereth abroad.

31¶ Wherefore I say unto you, All manner of sin and blasphemy shall be forgiven unto men: but the blasphemy against the Holy Ghost shall not be forgiven unto men. 32And whosoever speaketh a word against the Son of man, it shall be forgiven him: but whosoever speaketh against the Holy Ghost, it shall not be forgiven him, neither in this world, neither in the world to come. 33Either make the tree good, and his fruit good; or else make the tree corrupt, and his fruit corrupt: for the tree is known by his fruit. 34O generation of vipers, how can ye, being evil, speak good things? for out of the abundance of the heart the mouth speaketh. 35A good man out of the good treasure of the heart bringeth forth good things: and an evil man out of the evil treasure bringeth forth evil things. 36But I say unto you, That every idle word that men shall speak, they shall give account thereof in the day of judgment. 37For by thy words thou shalt be justified, and by thy words thou shalt be condemned.

38¶ Then certain of the scribes and of the Pharisees answered, saying, Master, we would see a sign from thee. 39But he answered and said unto them, An evil and adulterous generation seeketh after a sign; and there shall no sign be given to it, but the sign of the prophet Jonas: 40For as Jonas was three days and three nights in the whale’s belly; so shall the Son of man be three days and three nights in the heart of the earth. 41The men of Nineveh shall rise in judgment with this generation, and shall condemn it: because they repented at the preaching of Jonas; and, behold, a greater than Jonas is here. 42The queen of the south shall rise up in the judgment with this generation, and shall condemn it: for she came from the uttermost parts of the earth to hear the wisdom of Solomon; and, behold, a greater than Solomon is here. 43When the unclean spirit is gone out of a man, he walketh through dry places, seeking rest, and findeth none. 44Then he saith, I will return into my house from whence I came out; and when he is come, he findeth it empty, swept, and garnished. 45Then goeth he, and taketh with himself seven other spirits more wicked than himself, and they enter in and dwell there: and the last state of that man is worse than the first. Even so shall it be also unto this wicked generation.

46¶ While he yet talked to the people, behold, his mother and his brethren stood without, desiring to speak with him. 47Then one said unto him, Behold, thy mother and thy brethren stand without, desiring to speak with thee. 48But he answered and said unto him that told him, Who is my mother? and who are my brethren? 49And he stretched forth his hand toward his disciples, and said, Behold my mother and my brethren! 50For whosoever shall do the will of my Father which is in heaven, the same is my brother, and sister, and mother.