Mateyu 1 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 1:1-25

Makolo a Yesu Khristu Monga mwa Thupi

1Buku lofotokoza za mʼbado wa Yesu Khristu mwana wa Davide, mwana wa Abrahamu:

2Abrahamu anabereka Isake,

Isake anabereka Yakobo,

Yakobo anabereka Yuda ndi abale ake.

3Yuda anabereka Perezi ndi Zara, amene amayi awo anali Tamara.

Perezi anabereka Hezironi,

Hezironi anabereka Aramu.

4Aramu anabereka Aminadabu,

Aminadabu anabereka Naasoni,

Naasoni anabereka Salimoni.

5Salimoni anabereka Bowazi amene amayi ake anali Rahabe,

Bowazi anabereka Obedi amene amayi ake anali Rute,

Obedi anabereka Yese.

6Yese anabereka Mfumu Davide.

Ndipo Davide anabereka Solomoni, amene amayi ake anali mkazi wa Uriya.

7Solomoni anabereka Rehabiamu,

Rehabiamu anabereka Abiya,

Abiya anabereka Asa,

8Asa anabereka Yehosafati,

Yehosafati anabereka Yoramu,

Yoramu anabereka Uziya.

9Uziya anabereka Yotamu,

Yotamu anabereka Ahazi,

Ahazi anabereka Hezekiya.

10Hezekiya anabereka Manase,

Manase anabereka Amoni,

Amoni anabereka Yosiya.

11Yosiya anali atabala Yekoniya ndi abale ake pamene Ayuda anatengedwa ukapolo kupita ku Babuloni.

12Ali ku ukapolo ku Babuloni,

Yekoniya anabereka Salatieli,

Salatieli anabereka Zerubabeli.

13Zerubabeli anabereka Abiudi,

Abiudi anabereka Eliakimu,

Eliakimu anabereka Azoro.

14Azoro anabereka Zadoki,

Zadoki anabereka Akimu,

Akimu anabereka Eliudi.

15Eliudi anabereka Eliezara,

Eliezara anabereka Matani,

Matani anabereka Yakobo.

16Yakobo anabereka Yosefe, mwamuna wa Mariya. Mariyayu ndiye anabereka Yesu wotchedwa Khristu.

17Kuyambira pa Abrahamu mpaka pa Davide, pali mibado khumi ndi inayi. Ndipo kuyambira pa Davide mpaka pamene Ayuda anatengedwa kupita ku ukapolo ku Babuloni, pali mibado khumi ndi inayi. Ndiponso kuyambira nthawi ya ukapolo ku Babuloni mpaka pamene Khristu anabadwa, palinso mibado khumi ndi inayi.

Kubadwa kwa Yesu Khristu

18Kubadwa kwa Yesu Khristu kunali motere: Amayi ake, Mariya, anapalidwa ubwenzi ndi Yosefe, koma asanagone malo amodzi, anapezeka ali woyembekezera mwana mwa mphamvu ya Mzimu Woyera. 19Popeza Yosefe mwamuna wake anali munthu wolungama, sanafune kumuchititsa manyazi pomuleka poyera. Choncho anaganiza zomuleka mosaonetsera.

20Koma akuganiza zimenezi, taonani, mngelo wa Ambuye anamuonekera mʼmaloto nati, “Yosefe mwana wa Davide, usaope kumutenga Mariya kukhala mkazi wako, chifukwa mwana akuyembekezerayo ndi wochokera kwa Mzimu Woyera. 21Ndipo adzabala mwana wamwamuna, udzamutcha dzina lake Yesu; pakuti Iyeyo adzapulumutsa anthu ake ku machimo awo.”

22Zonsezi zinachitika kukwaniritsa zimene Ambuye ananena mwa mneneri kuti, 23“Onani namwali adzakhala woyembekezera ndipo adzabala mwana wamwamuna, ndipo mwanayo adzamutcha Imanueli,” kutanthauza kuti, “Mulungu ali nafe.”

24Yosefe atadzuka, anachita zomwe mngelo wa Ambuye uja anamulamulira. Iye anamutenga Mariya kukhala mkazi wake. 25Koma sanagone malo amodzi mpaka mwanayo atabadwa ndipo anamutcha dzina lake Yesu.

New International Version

Matthew 1:1-25

The Genealogy of Jesus the Messiah

1This is the genealogy1:1 Or is an account of the origin of Jesus the Messiah1:1 Or Jesus Christ. Messiah (Hebrew) and Christ (Greek) both mean Anointed One; also in verse 18. the son of David, the son of Abraham:

2Abraham was the father of Isaac,

Isaac the father of Jacob,

Jacob the father of Judah and his brothers,

3Judah the father of Perez and Zerah, whose mother was Tamar,

Perez the father of Hezron,

Hezron the father of Ram,

4Ram the father of Amminadab,

Amminadab the father of Nahshon,

Nahshon the father of Salmon,

5Salmon the father of Boaz, whose mother was Rahab,

Boaz the father of Obed, whose mother was Ruth,

Obed the father of Jesse,

6and Jesse the father of King David.

David was the father of Solomon, whose mother had been Uriah’s wife,

7Solomon the father of Rehoboam,

Rehoboam the father of Abijah,

Abijah the father of Asa,

8Asa the father of Jehoshaphat,

Jehoshaphat the father of Jehoram,

Jehoram the father of Uzziah,

9Uzziah the father of Jotham,

Jotham the father of Ahaz,

Ahaz the father of Hezekiah,

10Hezekiah the father of Manasseh,

Manasseh the father of Amon,

Amon the father of Josiah,

11and Josiah the father of Jeconiah1:11 That is, Jehoiachin; also in verse 12 and his brothers at the time of the exile to Babylon.

12After the exile to Babylon:

Jeconiah was the father of Shealtiel,

Shealtiel the father of Zerubbabel,

13Zerubbabel the father of Abihud,

Abihud the father of Eliakim,

Eliakim the father of Azor,

14Azor the father of Zadok,

Zadok the father of Akim,

Akim the father of Elihud,

15Elihud the father of Eleazar,

Eleazar the father of Matthan,

Matthan the father of Jacob,

16and Jacob the father of Joseph, the husband of Mary, and Mary was the mother of Jesus who is called the Messiah.

17Thus there were fourteen generations in all from Abraham to David, fourteen from David to the exile to Babylon, and fourteen from the exile to the Messiah.

Joseph Accepts Jesus as His Son

18This is how the birth of Jesus the Messiah came about1:18 Or The origin of Jesus the Messiah was like this: His mother Mary was pledged to be married to Joseph, but before they came together, she was found to be pregnant through the Holy Spirit. 19Because Joseph her husband was faithful to the law, and yet1:19 Or was a righteous man and did not want to expose her to public disgrace, he had in mind to divorce her quietly.

20But after he had considered this, an angel of the Lord appeared to him in a dream and said, “Joseph son of David, do not be afraid to take Mary home as your wife, because what is conceived in her is from the Holy Spirit. 21She will give birth to a son, and you are to give him the name Jesus,1:21 Jesus is the Greek form of Joshua, which means the Lord saves. because he will save his people from their sins.”

22All this took place to fulfill what the Lord had said through the prophet: 23“The virgin will conceive and give birth to a son, and they will call him Immanuel”1:23 Isaiah 7:14 (which means “God with us”).

24When Joseph woke up, he did what the angel of the Lord had commanded him and took Mary home as his wife. 25But he did not consummate their marriage until she gave birth to a son. And he gave him the name Jesus.