Salimo 99
1Yehova akulamulira,
mitundu ya anthu injenjemere;
Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,
dziko lapansi ligwedezeke.
2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;
Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.
3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,
Iye ndi woyera.
4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo
Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;
mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.
5Kwezani Yehova Mulungu wathu
ndipo mulambireni pa mapazi ake;
Iye ndi woyera.
6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,
Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;
iwo anayitana Yehova
ndipo Iyeyo anawayankha.
7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;
iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.
8Inu Yehova Mulungu wathu,
munawayankha iwo;
Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,
ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.
9Kwezani Yehova Mulungu wathu
ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,
pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.
第 99 篇
上帝是聖潔的君王
1耶和華掌權,萬民當戰抖;
祂坐在基路伯天使之上,
大地當戰抖。
2耶和華在錫安偉大無比,
超越萬邦。
3萬國要讚美你偉大而可畏的名,
你是聖潔的。
4你是大能的君王,
喜愛正義,維護公平,
在雅各家秉公行義。
5要尊崇我們的上帝耶和華,
俯伏在祂腳凳前敬拜,
祂是聖潔的。
6祂的祭司中有摩西和亞倫,
呼求祂的人中有撒母耳。
他們求告耶和華,
祂就應允他們。
7祂在雲柱中向他們說話,
他們遵守祂賜下的法度和律例。
8耶和華,我們的上帝啊,
你應允了他們,
向他們顯明你是赦罪的上帝,
但也懲罰他們的罪惡。
9要尊崇我們的上帝耶和華,
在祂的聖山上敬拜祂,
因為我們的上帝耶和華是聖潔的。