Masalimo 99 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 99:1-9

Salimo 99

1Yehova akulamulira,

mitundu ya anthu injenjemere;

Iye wakhala pa mpando wake waufumu, pakati pa akerubi,

dziko lapansi ligwedezeke.

2Mʼziyoni wamkulu ndi Yehova;

Iye ndi wokwezeka pamwamba pa mitundu yonse ya anthu.

3Anthu atamande dzina lanu lalikulu ndi loopsa kwambiri,

Iye ndi woyera.

4Mfumu yamphamvu, iyo imakonda chilungamo

Inu mwakhazikitsa khalidwe losakondera;

mwachita zolungama ndi zoyenera mwa Yakobo.

5Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mulambireni pa mapazi ake;

Iye ndi woyera.

6Mose ndi Aaroni anali ena mwa ansembe ake,

Samueli anali pamodzi ndi iwo amene anayitana pa dzina lake;

iwo anayitana Yehova

ndipo Iyeyo anawayankha.

7Iye anayankhula nawo kuchokera mʼchipilala cha mtambo;

iwo anasunga malamulo ake ndi zophunzitsa zomwe anawapatsa.

8Inu Yehova Mulungu wathu,

munawayankha iwo;

Inu kwa Israeli munali Mulungu wokhululuka,

ngakhale munawalanga pa zochita zawo zoyipa.

9Kwezani Yehova Mulungu wathu

ndipo mumulambire pa phiri lake loyera,

pakuti Yehova Mulungu wathu ndi woyera.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 99:1-9

第 99 篇

上帝是聖潔的君王

1耶和華掌權,萬民當戰抖;

祂坐在基路伯天使之上,

大地當戰抖。

2耶和華在錫安偉大無比,

超越萬邦。

3萬國要讚美你偉大而可畏的名,

你是聖潔的。

4你是大能的君王,

喜愛正義,維護公平,

雅各家秉公行義。

5要尊崇我們的上帝耶和華,

俯伏在祂腳凳前敬拜,

祂是聖潔的。

6祂的祭司中有摩西亞倫

呼求祂的人中有撒母耳

他們求告耶和華,

祂就應允他們。

7祂在雲柱中向他們說話,

他們遵守祂賜下的法度和律例。

8耶和華,我們的上帝啊,

你應允了他們,

向他們顯明你是赦罪的上帝,

但也懲罰他們的罪惡。

9要尊崇我們的上帝耶和華,

在祂的聖山上敬拜祂,

因為我們的上帝耶和華是聖潔的。