Masalimo 95 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 95:1-11

Salimo 95

1Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,

tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu

2Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko

ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.

3Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,

mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.

4Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,

ndipo msonga za mapiri ndi zake.

5Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,

ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.

6Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,

tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;

7pakuti Iye ndiye Mulungu wathu

ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,

ndi nkhosa za mʼdzanja lake.

Lero ngati inu mumva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,

monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.

9Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,

ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.

10Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;

ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera

ndipo sanadziwe njira zanga.”

11Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,

“Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 95:1-11

Salmo 95

1Venid, cantemos con júbilo al Señor;

aclamemos a la roca de nuestra salvación.

2Lleguemos ante él con acción de gracias,

aclamémoslo con cánticos.

3Porque el Señor es el gran Dios,

el gran Rey sobre todos los dioses.

4En sus manos están los abismos de la tierra;

suyas son las cumbres de los montes.

5Suyo es el mar, porque él lo hizo;

con sus manos formó la tierra firme.

6Venid, postrémonos reverentes,

doblemos la rodilla

ante el Señor nuestro Hacedor.

7Porque él es nuestro Dios

y nosotros somos el pueblo de su prado;

¡somos un rebaño bajo su cuidado!

Si oís hoy su voz,

8no endurezcáis el corazón, como en Meribá,95:8 En hebreo, Meribá significa altercado.

como aquel día en Masá,95:8 En hebreo, Masá significa prueba o provocación. en el desierto,

9cuando vuestros antepasados me tentaron,

cuando me pusieron a prueba,

a pesar de haber visto mis obras.

10Cuarenta años estuve enojado

con aquella generación,

y dije: «Son un pueblo mal encaminado

que no reconoce mis senderos».

11Así que, en mi enojo, hice este juramento:

«Jamás entrarán en mi reposo».