Masalimo 86 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 86:1-17

Salimo 86

Pemphero la Davide.

1Ndimvereni Yehova ndipo mundiyankhe,

pakuti ndine wosauka ndi wosowa.

2Yangʼanirani moyo wanga, pakuti ndine wodzipereka kwa Inu.

Inu ndinu Mulungu wanga;

pulumutsani mtumiki wanu amene amadalira Inu.

Inu ndinu Mulungu wanga.

3Mundichitire chifundo, Inu Ambuye,

pakuti ndikuyitana Inu tsiku lonse.

4Bweretsani chimwemwe kwa mtumiki wanu, Ambuye,

pakuti ndimadalira Inu.

5Inu Ambuye, ndinu wokhululuka ndi wabwino,

wodzaza ndi chikondi kwa onse amene amayitana Inu.

6Yehova imvani pemphero langa;

mvetserani kulira kwanga kofuna chifundo.

7Pa tsiku la mavuto anga ndidzayitana Inu,

pakuti Inu mudzandiyankha.

8Pakati pa milungu palibe wina wofanana nanu Ambuye;

palibe ntchito zolingana ndi ntchito zanu.

9Mitundu yonse ya anthu imene munayipanga

idzabwera ndi kudzalambira pamaso panu Ambuye;

iwo adzabweretsa ulemerero pa dzina lanu.

10Pakuti ndinu wamkulu ndipo mumachita zodabwitsa;

Inu nokha ndiye Mulungu.

11Ndiphunzitseni njira yanu Yehova,

ndipo ndidzayenda mʼchoonadi chanu;

patseni mtima wosagawikana

kuti ndilemekeze dzina lanu.

12Ndidzakutamandani Ambuye Mulungu wanga, ndi mtima wanga wonse;

ndidzalemekeza dzina lanu kwamuyaya.

13Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu kwa ine;

mwandipulumutsa ku malo ozama a manda.

14Inu Mulungu wanga, anthu odzikuza akundithira nkhondo;

anthu ankhanza akufuna kundipha,

amene salabadira za Inu.

15Koma Ambuye ndinu Mulungu wachifundo ndi wokoma mtima,

wosakwiya msanga, wodzaza ndi chikondi ndi wokhulupirika.

16Tembenukirani kwa ine ndipo ndichitireni chifundo;

perekani mphamvu zanu kwa mtumiki wanu

ndipo pulumutsani mwana wa mdzakazi wanu.

17Mundionetse chizindikiro cha ubwino wanu

kuti adani achione ndi kuchititsidwa manyazi,

pakuti Yehova mwandithandiza ndi kunditonthoza.

Hoffnung für Alle

Psalm 86:1-17

Gib mir ein Zeichen deiner Güte!

1Ein Gebet von David.

Höre mich, o Herr, und antworte mir,

denn ich bin hilflos und auf dich angewiesen!

2Rette mein Leben – ich gehöre doch zu dir!

Hilf mir, denn auf dich setze ich mein Vertrauen!

Du bist mein Gott, dem ich diene.

3Den ganzen Tag rufe ich nach dir;

hab doch Erbarmen mit mir, Herr!

4Schenke mir wieder neue Freude,

nach dir sehne ich mich!

5Du, Herr, bist gut und zum Vergeben bereit,

unermesslich ist deine Gnade für alle, die zu dir beten.

6Höre, Herr, mein Gebet,

ich flehe zu dir!

7Ich weiß weder aus noch ein.

Darum schreie ich zu dir, und du wirst mich erhören.

8Kein anderer Gott ist wie du, Herr;

niemand kann tun, was du tust!

9Du hast alle Völker geschaffen.

Sie werden zu dir kommen und dich anbeten,

sie werden deinen Namen rühmen und ehren.

10Denn du bist groß und vollbringst Wunder,

nur du bist Gott, du allein!

11Herr, zeige mir deinen Weg,

ich will dir treu sein und tun, was du sagst.

Gib mir nur dies eine Verlangen:

dir mit Ehrfurcht zu begegnen!

12Von ganzem Herzen will ich dir danken, Herr, mein Gott;

für alle Zeiten will ich deinen Namen preisen.

13Denn deine Liebe zu mir ist unfassbar groß!

Du hast mich dem sicheren Tod entrissen.

14Hochmütige Menschen fallen über mich her.

Sie tun sich zusammen und schrecken vor keiner Gewalttat zurück,

ja, sie trachten mir nach dem Leben.

Du, Herr, bist ihnen völlig gleichgültig!

15Aber du bist ein gnädiger und barmherziger Gott.

Deine Geduld ist groß, deine Liebe und Treue kennen kein Ende.

16Darum wende dich mir zu und hab Erbarmen!

Gib mir deine Kraft und rette mich! Dir bin ich treu ergeben.

17Herr, gib mir ein sichtbares Zeichen deiner Güte!

Dann werden alle, die mich hassen, sich schämen,

weil du mir geholfen und mich getröstet hast!