Masalimo 83 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 83:1-18

Salimo 83

Nyimbo. Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu musakhale chete;

musangoti phee, Mulungu musangoti duu.

2Onani adani anu akuchita chiwawa,

amene amadana nanu autsa mitu yawo.

3Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;

Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.

4Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu

kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

5Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;

Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:

6Matenti a Edomu ndi Aismaeli,

Mowabu ndi Ahagiri,

7Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,

Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.

8Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo

kupereka mphamvu kwa ana a Loti.

Sela

9Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,

monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.

10Amene anawonongedwa ku Endori

ndi kukhala ngati zinyalala.

11Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu

ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,

12amene anati, “Tiyeni tilande dziko

la msipu la Mulungu.”

13Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,

ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.

14Monga moto umatentha nkhalango,

kapena malawi a moto kuyatsa phiri,

15kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,

ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.

16Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi

kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;

awonongeke mwa manyazi.

18Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,

ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

New International Reader’s Version

Psalm 83:1-18

Psalm 83

A song. A psalm of Asaph.

1God, don’t remain silent.

Don’t refuse to listen.

Do something, God.

2See how your enemies are growling like dogs.

See how they are rising up against you.

3They make clever plans against your people.

They make evil plans against those you love.

4“Come,” they say. “Let’s destroy that whole nation.

Then the name of Israel won’t be remembered anymore.”

5All of them agree on the evil plans they have made.

They join forces against you.

6Their forces include the people of Edom,

Ishmael, Moab and Hagar.

7They also include the people of Byblos, Ammon, Amalek,

Philistia and Tyre.

8Even Assyria has joined them

to give strength to the people of Moab and Ammon.

9Do to them what you did to the people of Midian.

Do to them what you did to Sisera and Jabin at the Kishon River.

10Sisera and Jabin died near the town of Endor.

Their bodies were left on the ground like human waste.

11Do to the nobles of your enemies what you did to Oreb and Zeeb.

Do to all their princes what you did to Zebah and Zalmunna.

12They said, “Let’s take over

the grasslands that belong to God.”

13My God, make them like straw that the wind blows away.

Make them like tumbleweed.

14Destroy them as fire burns up a forest.

Destroy them as a flame sets mountains on fire.

15Chase them with your mighty winds.

Terrify them with your storm.

16Lord, put them to shame

so that they will seek you.

17May they always be filled with terror and shame.

May they die in dishonor.

18May you, the Lord, let your enemies know who you are.

You alone are the Most High God over the whole earth.