Masalimo 83 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 83:1-18

Salimo 83

Nyimbo. Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu musakhale chete;

musangoti phee, Mulungu musangoti duu.

2Onani adani anu akuchita chiwawa,

amene amadana nanu autsa mitu yawo.

3Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;

Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.

4Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu

kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

5Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;

Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:

6Matenti a Edomu ndi Aismaeli,

Mowabu ndi Ahagiri,

7Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,

Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.

8Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo

kupereka mphamvu kwa ana a Loti.

Sela

9Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,

monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.

10Amene anawonongedwa ku Endori

ndi kukhala ngati zinyalala.

11Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu

ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,

12amene anati, “Tiyeni tilande dziko

la msipu la Mulungu.”

13Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,

ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.

14Monga moto umatentha nkhalango,

kapena malawi a moto kuyatsa phiri,

15kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,

ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.

16Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi

kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;

awonongeke mwa manyazi.

18Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,

ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 83:1-18

第 83 篇

祈求上帝擊敗仇敵

亞薩的詩。

1上帝啊,求你不要緘默無聲,

一言不發。

2看啊,你的敵人在喧嚷,

恨你的人趾高氣揚。

3他們用詭計害你的子民,

他們一起謀害你所疼愛的人。

4他們說:

「來吧,讓我們剷除以色列

讓他們亡國,被人遺忘。」

5他們串通一氣,

勾結起來抵擋你。

6他們是以東人、以實瑪利人、摩押人、夏甲人、

7迦巴勒人、亞捫人、亞瑪力人、非利士人和泰爾人。

8亞述也跟他們勾結,

要助羅得的後代一臂之力。(細拉)

9求你對付他們,

如同對付米甸人和基順河邊的西西拉耶賓

10他們在隱·多珥滅亡,

成了地上的糞土。

11求你使他們的首領得到俄立西伊伯那樣的下場,

使他們的王侯得到西巴撒慕拿那樣的下場。

12他們曾說:

「讓我們奪取上帝的草場吧。」

13我的上帝啊,求你把他們驅散,

如同狂風吹散塵土和碎稭。

14烈火怎樣燒毀森林,

火焰怎樣吞沒山嶺,

15求你也照樣用狂風追趕他們,

用暴雨恐嚇他們。

16耶和華啊,

求你使他們滿面羞愧,

這樣他們才會來尋求你。

17願他們永遠羞愧驚恐,

願他們在恥辱中滅亡。

18讓他們知道你是耶和華,

唯有你是普天下的至高者。