Masalimo 80 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 80:1-19

Salimo 80

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu.

1Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli,

Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa;

Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani

2kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase.

Utsani mphamvu yanu;

bwerani ndi kutipulumutsa.

3Tibwezereni mwakale Inu Mulungu;

nkhope yanu itiwalire

kuti tipulumutsidwe.

4Inu Mulungu Wamphamvuzonse,

mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka

kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?

5Mwawadyetsa buledi wa misozi;

mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.

6Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu,

ndipo adani athu akutinyoza.

7Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse,

nkhope yanu itiwalire

kuti tipulumutsidwe.

8Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto;

munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.

9Munawulimira munda wamphesawo,

ndipo unamera ndi kudzaza dziko.

10Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake,

mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.

11Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja,

mphukira zake mpaka ku mtsinje.

12Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake

kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?

13Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga

ndipo zirombo za mthengo zimawudya.

14Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse!

Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone!

Uyangʼanireni mpesa umenewu,

15muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala,

mwana amene inu munamukuza nokha.

16Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto;

pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.

17Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja,

mwana wa munthu amene mwalera nokha.

18Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu;

titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.

19Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse

nkhope yanu itiwalire

kuti tipulumutsidwe.

Hoffnung für Alle

Psalm 80:1-20

Der verbrannte Weinstock

1Ein Lied von Asaf, nach der Melodie: »Lilien als Zeugnis«.

2Höre uns, Gott, du Hirte Israels, der du dein Volk80,2 Wörtlich: der du Josef. wie eine Herde hütest!

Der du über den Keruben thronst –

erscheine in deinem strahlenden Glanz!

3Zeige deine Macht den Stämmen Ephraim, Benjamin und Manasse!

Komm und hilf uns doch!

4O Gott, richte uns, dein Volk, wieder auf!

Blicke uns freundlich an, dann sind wir gerettet!

5Du allmächtiger Herr und Gott,

wie lange willst du noch zornig auf uns sein,

obwohl wir zu dir beten?

6Tränen sind unsere einzige Speise –

ganze Krüge könnten wir mit ihnen füllen!

7Unsere Feinde spotten über unsere Ohnmacht,

sie streiten sich schon über unser Land.80,7 Wörtlich: Du hast uns zum Zankapfel für unsere Nachbarn gemacht.

8Allmächtiger Gott, richte uns, dein Volk, wieder auf!

Blicke uns freundlich an, dann sind wir gerettet!

9In Ägypten grubst du den Weinstock Israel aus;

du pflanztest ihn ein in einem Land,

aus dem du fremde Völker verjagt hattest.

10Für ihn hast du den Boden gerodet,

so dass er Wurzeln schlagen konnte

und sich im ganzen Land ausbreitete.

11Mit seinem Schatten bedeckte er das Gebirge,

er wuchs höher als die gewaltigsten Zedern.

12Seine Ranken erstreckten sich bis zum Mittelmeer,

und bis an den Euphrat gelangten seine Zweige.

13Warum nur hast du die schützende Mauer niedergerissen?

Jetzt kann jeder, der vorüberkommt, ihn plündern!

14Die Wildschweine aus dem Wald verwüsten ihn,

die wilden Tiere fressen ihn kahl.

15Allmächtiger Gott, wende dich uns wieder zu!

Schau vom Himmel herab und rette dein Volk!

Kümmere dich um diesen Weinstock,

16den du selbst gepflanzt hast;

sorge für den jungen Spross,

den du hast aufwachsen lassen!

17Unsere Feinde haben ihn abgehauen und ins Feuer geworfen;

doch wenn du ihnen entgegentrittst, kommen sie um.

18Beschütze den König, den du erwählt hast,

den Mann80,18 Wörtlich: Menschensohn. – Vgl. »Menschensohn« in den Sacherklärungen., der durch dich erst stark wurde!

19Dann wollen wir nie mehr von dir weichen.

Erhalte uns am Leben, dann wollen wir dich loben.

20Du allmächtiger Herr und Gott –

richte uns, dein Volk, wieder auf!

Blicke uns freundlich an, dann sind wir gerettet!