Masalimo 78 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 78:1-72

Salimo 78

Ndakatulo ya Asafu.

1Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa;

mvetserani mawu a pakamwa panga.

2Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo,

ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale

3zimene tinazimva ndi kuzidziwa,

zimene makolo athu anatiwuza.

4Sitidzabisira ana awo,

tidzafotokozera mʼbado wotsatira

ntchito zotamandika za Yehova,

mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.

5Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo

ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli,

zimene analamulira makolo athu

kuphunzitsa ana awo,

6kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa,

ngakhale ana amene sanabadwe,

ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.

7Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu

ndipo sadzayiwala ntchito zake

koma adzasunga malamulo ake.

8Iwo asadzakhale monga makolo awo,

mʼbado wosamvera ndi wowukira,

umene mitima yake inali yosamvera Mulungu,

umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.

9Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta,

anathawabe pa nthawi ya nkhondo;

10iwo sanasunge pangano la Mulungu

ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.

11Anayiwala zimene Iye anachita,

zozizwitsa zimene anawaonetsa.

12Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona,

mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.

13Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo,

Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.

14Anawatsogolera ndi mtambo masana

ndi kuwala kwa moto usiku wonse.

15Iye anangʼamba miyala mʼchipululu

ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;

16Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala

ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.

17Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye,

kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.

18Ananyoza Mulungu mwadala

pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.

19Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti,

“Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?

20Iye atamenya thanthwe

madzi anatuluka,

ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi.

Koma iye angatipatsenso ife chakudya?

Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”

21Yehova atawamva anakwiya kwambiri;

moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo,

ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,

22pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu

kapena kudalira chipulumutso chake.

23Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba

ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;

24anagwetsa mana kuti anthu adye,

anawapatsa tirigu wakumwamba.

25Anthu anadya buledi wa angelo,

Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.

26Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba,

ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.

27Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi,

mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.

28Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo,

kuzungulira matenti awo onse.

29Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka

pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.

30Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho,

chakudya chili mʼkamwa mwawobe,

31mkwiyo wa Mulungu unawayakira;

Iye anapha amphamvu onse pakati pawo,

kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.

32Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa;

ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.

33Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya.

Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.

34Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo;

iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.

35Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo,

kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.

36Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo,

kumunamiza ndi malilime awo;

37Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye,

iwo sanakhulupirike ku pangano lake.

38Komabe Iye anali wachifundo;

anakhululukira mphulupulu zawo

ndipo sanawawononge.

Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake

ndipo sanawutse ukali wake wonse.

39Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe,

mphepo yopita imene sibwereranso.

40Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu

ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!

41Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu;

ankamuputa Woyera wa Israeli.

42Sanakumbukire mphamvu zake,

tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,

43tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto,

zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.

44Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi;

Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.

45Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga,

ndiponso achule amene anawasakaza.

46Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala,

zokolola zawo kwa dzombe.

47Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala

ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.

48Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala,

zoweta zawo ku zingʼaningʼani.

49Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo,

anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso.

Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.

50Analolera kukwiya,

sanawapulumutse ku imfa

koma anawapereka ku mliri.

51Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,

zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu

52Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto;

anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.

53Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha

koma nyanja inamiza adani awo.

54Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera,

ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.

55Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo

ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo;

Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.

56Koma iwo anayesa Mulungu

ndi kuwukira Wammwambamwamba;

sanasunge malamulo ake.

57Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo,

anapotoka monga uta wosakhulupirika.

58Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano;

anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.

59Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri;

Iye anakana Israeli kwathunthu.

60Anasiya nyumba ya ku Silo,

tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.

61Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo,

ulemerero wake mʼmanja mwa adani.

62Anapereka anthu ake ku lupanga;

anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.

63Moto unanyeketsa anyamata awo,

ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;

64ansembe awo anaphedwa ndi lupanga,

ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.

65Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo,

ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.

66Iye anathamangitsa adani ake;

anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.

67Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe,

sanasankhe fuko la Efereimu;

68Koma anasankha fuko la Yuda,

phiri la Ziyoni limene analikonda.

69Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda,

dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.

70Anasankha Davide mtumiki wake

ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;

71kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa

kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo,

wa Israeli cholowa chake.

72Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama;

ndi manja aluso anawatsogolera.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

詩篇 78:1-72

第 78 篇

上帝引導祂的子民

亞薩的訓誨詩。

1我的百姓啊!

你們要聽我的教導,

側耳傾聽我的話。

2我要開口講比喻,

道出古時的奧秘,

3是我們所聞所知、世代流傳下來的事。

4我們不要在子孫面前隱瞞事實,

要把耶和華當受稱頌的作為、

祂的權能和所行的奇事告訴下一代。

5因為祂為雅各制定法度,

以色列設立律法,

又吩咐我們的祖先把這些律法傳給兒女,

6好讓他們也照樣教導自己的子孫後代,

世代相傳。

7這樣,他們就會信靠上帝,

遵行祂的命令,

不忘記祂的作為;

8也不會像自己的祖先那樣頑梗叛逆,

對上帝不忠,心懷二意。

9以法蓮人備上了弓箭,

卻臨陣逃命。

10他們不遵守上帝的約,

拒絕遵行祂的律法。

11他們忘記了祂的作為,

忘記了祂為他們所行的奇事。

12祂曾在埃及,在瑣安當著他們祖先的面行神蹟。

13祂把海水分開,

帶領他們安然渡過;

祂使海水堆起如牆壁。

14祂白天以雲柱帶領他們,

晚上用火柱引導他們。

15祂在曠野劈開磐石,

供應他們豐沛的水源。

16祂使水從磐石中滾滾流出,

如滔滔江河。

17然而,他們仍舊犯罪,

在曠野反叛至高的上帝。

18他們頑梗地試探上帝,

索要他們想吃的食物。

19他們抱怨上帝,說:

「難道上帝可以在曠野擺宴席嗎?

20祂擊打磐石,

水就湧出,流淌成河,

但祂能賜給我們——祂的子民食物和肉嗎?」

21耶和華聽後大怒,

祂的怒火燒向雅各

祂的怒氣撒向以色列

22因為他們不相信上帝,也不信靠祂的拯救。

23祂向穹蒼發出命令,

又打開天門,

24降下嗎哪給他們吃,賜下天糧。

25他們吃了天使的食物,

上帝賜給他們豐富的食物。

26祂使空中颳起東風,

用大能引來南風,

27使飛鳥像雨點一般降在他們當中,多如塵埃,

使他們有多如海沙的肉吃。

28祂使飛鳥降落在他們營中的帳篷周圍,

29讓他們盡情地吃,

遂了他們的心願。

30但是,他們還沒有吃完,

肉還在口中的時候,

31上帝就向他們發怒,

殺掉了他們當中最強壯的,

消滅了以色列的青年。

32即使如此,

他們依舊犯罪,

不相信上帝奇妙的作為。

33所以上帝使他們虛度一生,

讓他們的歲月充滿恐懼。

34直到上帝擊殺他們的時候,

他們才回轉,誠心尋求上帝。

35他們才想起上帝是他們的磐石,

至高的上帝是他們的救贖主。

36他們卻虛情假意,滿口謊言。

37他們不忠於祂,

也不信守祂的約。

38但上帝充滿憐憫,

赦免了他們的罪,

沒有毀滅他們。

祂多次收住怒氣,

沒有完全發出祂的烈怒。

39祂顧念他們不過是血肉之軀,

像一陣風轉眼消逝。

40他們在曠野屢屢反叛祂,

使祂傷心。

41他們再三試探上帝,

以色列的聖者發怒。

42他們忘記了祂的大能,

忘記了祂救他們脫離壓迫的日子,

43也忘記了祂在埃及所行的神蹟,

瑣安的田野所行的奇事。

44祂曾使江河溪流變成血,

以致無人能喝。

45祂曾使成群的蒼蠅吞沒他們,

使青蛙毀滅他們。

46祂將他們的五穀賞給蚱蜢,

讓蝗蟲吃盡他們的收成。

47祂用冰雹毀壞他們的葡萄樹,

用嚴霜毀壞他們的無花果樹,

48又用冰雹毀滅他們的牛群,

用閃電毀滅他們的牲畜。

49祂把怒火、烈怒、憤恨和禍患傾倒在他們身上,

遣下一群降災的天使。

50祂的怒氣盡發,

使他們被瘟疫吞噬,難逃一死。

51祂擊殺了埃及人所有的長子,

就是帳篷中頭生的兒子。

52祂領出自己的子民,

好像領出羊群,

引領他們經過曠野,

53使他們一路平安,免受驚嚇,

大海卻淹沒了他們的仇敵。

54祂帶領自己的子民來到聖地的邊界,

來到祂親手為他們預備的山區,

55從他們面前趕出外族人,

把外族人的土地分給他們,

作為他們的產業,

使以色列各支派安頓下來。

56可是,他們仍舊試探上帝,

反叛至高者,不遵行祂的法度。

57他們跟祖先一樣背信棄義,

像斷弓一樣毫不可靠。

58他們建造邱壇,惹祂發怒;

他們豎起神像,令祂憤怒。

59上帝知道了他們的惡行,

怒不可遏,

徹底棄絕了以色列人。

60祂離棄了設在示羅的聖幕,

就是祂在人間的居所。

61祂任憑自己的約櫃被人擄去,

讓自己的榮耀落在敵人手中。

62祂使自己的子民被刀劍殺戮,

向自己的產業大發怒氣。

63青年被烈火吞噬,

少女無法婚嫁。

64祭司喪身刀下,

寡婦無法哭喪。

65那時,主像從睡眠中醒來,

又如酒後醒來的勇士。

66祂擊退仇敵,

叫他們永遠蒙羞。

67祂丟棄了約瑟的子孫,

沒有揀選以法蓮支派。

68祂揀選了猶大支派,

祂所喜愛的錫安山。

69祂為自己建造高聳的聖所,

使它像大地一樣長存。

70祂揀選了祂的僕人大衛

把他從羊圈中召來,

71讓他離開牧羊的生活,

去牧養祂的子民雅各的後裔,

牧養祂的產業以色列

72於是,大衛以正直的心牧養他們,

用靈巧的手帶領他們。