Masalimo 76 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 76:1-12

Salimo 76

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za zingwe. Salimo la Asafu.

1Mulungu amadziwika mu Yuda;

dzina lake ndi lotchuka mu Israeli.

2Tenti yake ili mu Salemu,

malo ake okhalamo mu Ziyoni.

3Kumeneko Iye anathyola mivi yowuluka,

zishango ndi malupanga, zida zankhondo.

Sela

4Wolemekezeka ndinu,

wamphamvu kuposa mapiri amene ali ndi nyama zambiri.

5Anthu owuma mtima amagona atalandidwa chuma,

Iwowo amagona tulo tawo totsiriza;

palibe mmodzi wamphamvu

amene angatukule manja ake.

6Pa kudzudzula kwanu, Inu Mulungu wa Yakobo,

kavalo pamodzi ndi galeta zimakhala chete zitagona pansi.

7Inu nokha ndiye muyenera kuopedwa.

Angathe kuyima pamaso panu ndani mukakwiya?

8Kuchokera kumwamba Inu munalengeza chiweruzo,

ndipo dziko linaopa ndi kukhala chete,

9pamene Inu Mulungu munadzuka kuti muweruze,

kupulumutsa onse osautsidwa mʼdziko.

Sela

10Zoonadi, ukali wanu pa anthu umakubweretserani matamando

ndipo opulumuka ku ukali wanu mumawasunga pafupi nanu.

11Chitani malumbiro kwa Yehova Mulungu wanu ndipo muwakwaniritse;

anthu onse omuzungulira abweretse mphatso

kwa Iye amene ayenera kuopedwa.

12Iye amaswa mzimu wa olamulira;

amaopedwa ndi mafumu a dziko lapansi.

Hoffnung für Alle

Psalm 76:1-13

Gottes Zorn

1Ein Lied von Asaf, mit Saiteninstrumenten zu begleiten.

2Gott ist in Juda jedem bekannt,

in ganz Israel wird sein Name geehrt.

3In Jerusalem76,3 Wörtlich: In Salem. – Anstelle des vollen Namens wird hier der alte Name gewählt, um das Wort »Schalom« (Frieden) anklingen zu lassen. wurde sein Heiligtum errichtet;

auf dem Berg Zion hat er seine Wohnung.

4Dort zerbrach er Pfeile, Schilde und Schwerter,

ja, alles Kriegsgerät!

5Herr, wie kein anderer strahlst du vor Glanz,

du bist mächtiger als die uralten Berge.76,5 So nach der griechischen Übersetzung. Der hebräische Text lautet: Du bist glanzvoller, mächtiger als die Berge der Beute.

6Du hast die stolzen Krieger ihrer Waffen beraubt.

Sie schlafen den Todesschlaf,

und niemals werden sie wieder zur Waffe greifen.

7Du, Gott Jakobs, brauchtest nur zu drohen,

und schon fielen Ross und Reiter.

8Furchterregend bist du, o Gott!

Wer kann vor dir bestehen, wenn dein Zorn losbricht?

9Alle Welt erstarrte vor Schreck und wurde stumm,

als dein Richterspruch vom Himmel ertönte,

10als du dich erhobst, um Gericht zu halten

und den Entrechteten auf der Erde zu helfen.

11Das Wüten der Menschen vermehrt deinen Ruhm,

selbst ihr verzweifeltes Toben machst du dir zunutze76,11 Wörtlich: auch noch mit dem Rest des Zornes wirst du dich gürten.!

12Gebt dem Herrn, eurem Gott, Versprechen und haltet sie!

Ihr Völker rings um Israel – bringt ihm eure Gaben,

denn groß und gewaltig ist er!

13Er bricht den Stolz der hochmütigen Herrscher,

die Mächtigen dieser Welt müssen ihn fürchten!