Salimo 75
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo.
1Tikuthokoza Inu Mulungu,
tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe,
anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera,
ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera,
ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba.
Sela
4Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’
ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba;
musayankhule ndi khosi losololoka.’ ”
6Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo
kapena ku chipululu.
7Koma ndi Mulungu amene amaweruza:
Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8Mʼdzanja la Yehova muli chikho
chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera;
Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi
amamwa ndi senga zake zonse.
9Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya;
ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10Ndidzadula nyanga za onse oyipa
koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
Salmo 75
Para o mestre de música. De acordo com a melodia Não Destruas. Salmo da família de Asafe. Um cântico.
1Damos-te graças, ó Deus,
damos-te graças, pois perto está o teu nome;
todos falam dos teus feitos maravilhosos.
2Tu dizes: “Eu determino o tempo
em que julgarei com justiça.
3Quando treme a terra com todos os seus habitantes,
sou eu que mantenho firmes as suas colunas. Pausa
4Aos arrogantes digo: Parem de vangloriar-se!
E aos ímpios: Não se rebelem!75.4 Hebraico: Não levantem o chifre; também no versículo 5.
5Não se rebelem contra os céus;
não falem com insolência”.
6Não é do oriente nem do ocidente
nem do deserto que vem a exaltação.
7É Deus quem julga:
Humilha a um, a outro exalta.
8Na mão do Senhor está um cálice
cheio de vinho espumante e misturado;
ele o derrama, e todos os ímpios da terra
o bebem até a última gota.
9Quanto a mim, para sempre anunciarei essas coisas;
cantarei louvores ao Deus de Jacó.
10Destruirei o poder75.10 Hebraico: chifre. Duas vezes neste versículo. de todos os ímpios,
mas o poder dos justos aumentará.