Masalimo 75 – CCL & NVI-PT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 75:1-10

Salimo 75

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo.

1Tikuthokoza Inu Mulungu,

tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe,

anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.

2Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera,

ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.

3Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera,

ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba.

Sela

4Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’

ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.

5Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba;

musayankhule ndi khosi losololoka.’ ”

6Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo

kapena ku chipululu.

7Koma ndi Mulungu amene amaweruza:

Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.

8Mʼdzanja la Yehova muli chikho

chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera;

Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi

amamwa ndi senga zake zonse.

9Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya;

ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.

10Ndidzadula nyanga za onse oyipa

koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

Nova Versão Internacional

Salmos 75:1-10

Salmo 75

Para o mestre de música. De acordo com a melodia Não Destruas. Salmo da família de Asafe. Um cântico.

1Damos-te graças, ó Deus,

damos-te graças, pois perto está o teu nome;

todos falam dos teus feitos maravilhosos.

2Tu dizes: “Eu determino o tempo

em que julgarei com justiça.

3Quando treme a terra com todos os seus habitantes,

sou eu que mantenho firmes as suas colunas. Pausa

4Aos arrogantes digo: Parem de vangloriar-se!

E aos ímpios: Não se rebelem!75.4 Hebraico: Não levantem o chifre; também no versículo 5.

5Não se rebelem contra os céus;

não falem com insolência”.

6Não é do oriente nem do ocidente

nem do deserto que vem a exaltação.

7É Deus quem julga:

Humilha a um, a outro exalta.

8Na mão do Senhor está um cálice

cheio de vinho espumante e misturado;

ele o derrama, e todos os ímpios da terra

o bebem até a última gota.

9Quanto a mim, para sempre anunciarei essas coisas;

cantarei louvores ao Deus de Jacó.

10Destruirei o poder75.10 Hebraico: chifre. Duas vezes neste versículo. de todos os ímpios,

mas o poder dos justos aumentará.